詩篇 12 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 12:1-8

第 12 篇

祈求上帝幫助

大衛的詩,交給樂長。

1耶和華啊,求你救我們!

因為世上的敬虔人不見了,

忠信的人在人間消失了。

2人人謊話連篇,

花言巧語,口是心非。

3願你剷除一切花言巧語和狂妄自誇的人。

4他們說:「我們必靠舌頭制勝,

嘴唇是我們自己的,

誰管得著我們?」

5耶和華說:「我要保護受欺壓的困苦人和哀歎的貧窮人,

使他們如願以償。」

6耶和華的應許純全,

就像在爐中煉過七次的銀子。

7耶和華啊,你必保護我們,

永遠不容惡人侵害我們。

8眾人若抑善揚惡,

惡人必橫行無忌。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 12:1-8

Salimo 12

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe seminiti. Salimo la Davide.

1Thandizeni Yehova pakuti palibe munthu wokhulupirika;

okhulupirika akusowa pakati pa anthu.

2Aliyense amanamiza mʼbale wake;

ndi pakamwa pawo pabodza amayankhula zachinyengo.

3Inu Yehova tsekani milomo yonse yachinyengo

ndi pakamwa paliponse podzikuza.

4Pakamwa pamene pamati, “Ife tidzapambana ndi kuyankhula kwathu;

pakamwapa ndi pathupathu, tsono mbuye wathu ndani?”

5“Chifukwa cha kuponderezedwa kwa anthu opanda mphamvu

ndi kubuwula kwa anthu osowa,

Ine ndidzauka tsopano,” akutero Yehova,

“Ndidzawateteza kwa owazunza.”

6Ndipo mawu a Yehova ndi angwiro

monga siliva oyengedwa mʼngʼanjo yadothi,

oyengedwa kasanu nʼkawiri.

7Inu Yehova mudzatitchinjiriza ndipo

mudzatiteteza kwa anthu otere kwamuyaya.

8Oyipa amangoyendayenda ponseponse

anthu akamayamikira zochita zawo.