詩篇 108 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 108:1-13

第 108 篇

祈求上帝的幫助

大衛的詩歌。

1上帝啊!我的心堅定不移,

我要用心靈歌頌你。

2琴瑟啊,彈奏吧,

我要喚醒黎明。

3耶和華啊,我要在列邦稱謝你,

在列國歌頌你。

4因為你的慈愛廣及諸天,

你的信實高達穹蒼。

5上帝啊,

願你得到的尊崇超過諸天,

願你的榮耀覆蓋大地。

6求你應允我們的禱告,

伸出右手幫助我們,

使你所愛的人獲救。

7上帝在祂的聖所說:

「我要歡然劃分示劍,丈量疏割谷。

8基列是我的,瑪拿西也是我的,

以法蓮是我的頭盔,

猶大是我的權杖。

9摩押是我的洗腳盆,

我要把鞋扔給以東

我要在非利士高唱凱歌。」

10誰能帶我進入堅固的城池?

誰能領我到以東

11上帝啊,你拋棄了我們嗎?

上帝啊,你不再和我們的軍隊一同出戰了嗎?

12求你幫助我們攻打仇敵,

因為人的幫助徒然無益。

13我們依靠上帝才能取勝,

祂必把我們的敵人踩在腳下。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 108:1-13

Salimo 108

Nyimbo. Salimo la Davide.

1Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu;

ndidzayimba nyimbo, inde ndidzayimba nyimbo zotamanda ndi moyo wanga wonse.

2Dzukani, zeze ndi pangwe!

Ine ndidzadzutsa mʼbandakucha.

3Ndidzakutamandani Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina;

ndidzayimba za Inu pakati pa anthu a mitundu ina.

4Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kutalika kwake kuposa kumwamba;

kukhulupirika kwanu kumafika mlengalenga.

5Kwezekani Inu Mulungu, kuposa mayiko akumwamba,

ndipo ulemerero wanu uphimbe dziko lonse lapansi.

6Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja

kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.

7Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika:

“Mwachipambano Ine ndidzagawa Sekemu

ndipo ndidzayesa chigwa cha Sukoti.

8Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso;

Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera,

Yuda ndi ndodo yanga yaufumu.

9Mowabu ndi mbale yanga yosambiramo

ndidzaponya nsapato zanga pa Edomu;

ndidzafuwula mopambana pa Filisitiya.”

10Ndani adzandifikitsa ku mzinda wotetezedwa?

Ndani adzanditsogolera ku Edomu?

11Kodi sindinu Mulungu, Inu amene mwatikana

ndipo simuperekezanso magulu athu ankhondo?

12Tithandizeni ife kulimbana ndi mdani,

pakuti thandizo la munthu ndi lopanda pake.

13Chifukwa cha Mulungu wathu, ife tidzapeza chipambano,

ndipo adzapondereza pansi adani athu.