西番雅書 1 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

西番雅書 1:1-18

1猶大亞們的兒子約西亞執政期間,耶和華對希西迦的玄孫、亞瑪利亞的曾孫、基大利的孫子、古示的兒子西番雅說:

耶和華審判的日子

2「我必毀滅地上的一切。

這是耶和華說的。

3我必毀滅人類、獸類、

天上的鳥和海裡的魚。

我必使惡人倒斃,

我必剷除地上的人類。

這是耶和華說的。

4「我必伸手攻擊猶大

以及所有住在耶路撒冷的人,

剷除巴力的餘跡及拜偶像之祭司的名號。

5我必剷除那些在屋頂祭拜天上萬象的人,

剷除敬拜我、憑我起誓又憑米勒公起誓的人,

6剷除離棄我、不尋求我、不求問我的人。」

7要在主耶和華面前肅靜,

因為耶和華的日子近了。

耶和華已準備好祭物,

潔淨了祂邀請的人。

8耶和華說:「在我獻祭的日子,

我必懲罰首領和王子,

以及所有穿外族服裝的人。

9到那日,我必懲罰所有跳過門檻1·9 跳過門檻……的人」指祭拜偶像的人,參見撒母耳記上5·5

使主人的家充滿暴力和欺詐的人。

10到那日,魚門必傳出哭喊聲,

新區必響起哀號聲,

山陵必發出崩裂的巨響。

這是耶和華說的。

11市場區的居民啊,哀哭吧!

因為所有的商人必滅亡,

所有做買賣的必被剷除。

12那時,我必提著燈巡查耶路撒冷

懲罰那些安於罪中的人。

他們心想,『耶和華不賜福也不降禍。』

13他們的財物必遭搶掠,

家園必淪為廢墟。

他們建造房屋,卻不能住在裡面;

栽種葡萄園,卻喝不到葡萄酒。

14「耶和華的大日子近了,

近了,很快就到了。

那將是痛苦的日子,

勇士也必淒聲哀號。

15那是降烈怒的日子,

是困苦艱難的日子,

是摧殘毀壞的日子,

是黑暗幽冥的日子,

是陰霾密佈的日子,

16是吹號呐喊、

攻打堅城高壘的日子。

17「我要使人們災難臨頭,

以致他們行路像瞎子,

因為他們得罪了我。

他們的血必被倒出,如同灰塵;

他們的屍體必被丟棄,如同糞便。

18在耶和華發怒的日子,

他們的金銀救不了他們。

祂的怒火必吞噬大地,

祂必驟然毀滅一切世人。」

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zefaniya 1:1-18

1Yehova anayankhula ndi Zefaniya mwana wa Kusi, mwana wa Gedaliya, mwana wa Amariya, mwana wa Hezekiya pa nthawi ya Yosiya, mwana wa Amoni, mfumu ya Yuda.

Yehova Adzaweruza Dziko Lapansi

2“Ndidzawononga kotheratu zinthu zonse

pa dziko lapansi,”

akutero Yehova.

3“Ndidzawononga anthu pamodzi ndi nyama zomwe;

ndidzawononga mbalame zamlengalenga

ndi nsomba za mʼnyanja.

Ndidzawononga anthu oyipa,

ndipo ndidzafafaniza mtundu wa anthu pa dziko lonse lapansi,”

akutero Yehova.

Chenjezo kwa Yuda

4Ndidzatambasula dzanja langa pa Yuda

ndi onse okhala mu Yerusalemu.

Ndidzawononga pamalo pano otsalira opembedza Baala,

mayina a anthu osapembedza pamodzi ndi ansembe a mafano:

5amene amagwada pa madenga a nyumba zawo

kupembedza zolengedwa zamumlengalenga,

amene amagwada ndi kulumbira mʼdzina la Yehova,

komanso mʼdzina la Moleki,

6amene abwerera mʼmbuyo osatsata Yehova,

osafunafuna kapena kupempha nzeru kwa Yehova.

7Khalani chete pamaso pa Ambuye Yehova,

chifukwa tsiku la Yehova layandikira.

Yehova wakonzekera kupereka nsembe;

wapatula iwo amene wawayitana.

8Pa tsiku la nsembe ya Yehova

ndidzalanga akalonga

ndi ana aamuna a mfumu

ndi onse amene amavala

zovala zachilendo.

9Pa tsiku limenelo ndidzalanga

onse amene safuna kuponda pa chiwundo,

amene amadzaza nyumba ya ambuye awo

ndi chiwawa ndi chinyengo.

10“Pa tsiku limenelo,” akutero Yehova,

“Kufuwula kwakukulu kudzamveka pa Chipata cha Nsomba,

kulira kwa chisoni kuchokera mʼChigawo Chatsopano,

ndi phokoso la kugumuka kochokera ku mapiri.

11Lirani mwachisoni, inu amene mumakhala kumene kuli msika;

a malonda anu onse adzapululidwa,

ndiponso onse amene ali ndi siliva adzawonongedwa.

12Pa nthawi imeneyo ndidzafufuzafufuza mu Yerusalemu ndi nyale

ndi kulanga onse amene sakulabadira,

amene ali ngati vinyo wosakhutchumulidwa,

amene amaganiza kuti, ‘Yehova sadzachita chilichonse,

chabwino kaya choyipa.’

13Chuma chawo chidzafunkhidwa,

nyumba zawo zidzagwetsedwa.

Adzamanga nyumba,

koma osakhalamo;

adzadzala minda ya mpesa

koma sadzamwako vinyo wake.”

Tsiku Lalikulu la Yehova

14Tsiku lalikulu la Yehova layandikira,

layandikira ndipo lifika msanga.

Tamverani! Kulira kwa pa tsiku la Yehova kudzakhala kowawa,

ngakhale munthu wolimba mtima adzalira kwambiri.

15Tsiku limenelo lidzakhala la ukali,

tsiku losautsa ndi lomvetsa chisoni,

tsiku la mavuto ndi la chiwonongeko,

tsiku la mdima ndi lachisoni,

tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani.

16Tsiku loliza lipenga ndi la mfuwu wankhondo,

tsiku la kugwa kwa mizinda yotetezedwa

ndi nsanja za pa ngodya.

17Ndidzabweretsa msautso pa anthu

ndipo adzayenda ngati anthu osaona,

chifukwa achimwira Yehova,

magazi awo adzamwazika ngati fumbi

ndi mnofu wawo ngati ndowe.

18Ngakhale siliva wawo kapena golide wawo

sadzatha kuwapulumutsa

pa tsiku la ukali wa Yehova.

Dziko lonse lapansi lidzanyeka

mʼmoto wa nsanje yake

chifukwa adzakantha modzidzimutsa

onse okhala pa dziko lapansi.