耶利米書 5 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

耶利米書 5:1-31

耶路撒冷的罪

1耶和華說:

「你們在耶路撒冷街頭四處看看,

在廣場找找,

如果你們能找到一個公正誠實的人,

我就赦免這城。

2雖然他們憑永活的耶和華起誓,

卻口是心非。」

3耶和華啊,你要的不是誠實嗎?

你責打他們,他們不感到疼痛;

你嚴懲他們,他們仍不受教。

他們屢教不改,

臉比石頭還硬。

4我想:「他們貧窮、愚昧,

不明白他們上帝耶和華的道,

也不知道祂的法令。

5我要找他們的首領說話,

因為這些首領明白耶和華的道,

知道他們上帝的法令。」

然而,他們卻一致違背耶和華的律法,

不服從祂的法令。

6因此,林中的獅子必襲擊他們,

荒野的豺狼必殘害他們,

豹子也蹲伏在他們的城外,

伺機撕裂出城的人,

因為他們罪大惡極,屢屢叛道。

7耶和華說:

耶路撒冷啊,我怎能赦免你呢?

你的兒女背棄我,

憑假神起誓。

我供應他們的一切需要,

他們卻縱情淫亂,

湧向娼妓的家。

8他們像吃得肥壯、發情的公馬,

垂涎鄰居的妻子。

9我怎能不懲罰他們呢?

我怎能不親自報應這樣的國民呢?

這是耶和華說的。

10你們要去毀壞她的葡萄園,

但不可徹底毀壞。

要砍掉枝子,

因為那些枝子不屬於耶和華。

11以色列人和猶大人根本不忠於我。

這是耶和華說的。

12「他們撒謊說,

『耶和華不會管我們,

我們必不會遇到災禍、戰爭和饑荒。

13先知的話不過是一陣風,

不是來自上帝,

他們預言的災禍必降臨到自己身上。』」

14因此,萬軍之上帝耶和華對我說:

「因為他們說了這話,

我要使我的話在你口中成為火,

使他們像柴一樣被燒毀。

15以色列人啊,我要使一個國家,

一個歷久不衰的古國從遠方來攻擊你們,

你們不明白他們的語言,

也聽不懂他們說的話。

這是耶和華說的。

16他們都是勇士,

他們的弓箭殺人無數。

17他們必吞噬你們的兒女、牛羊、

糧食、葡萄和無花果,

用刀劍摧毀你們所依靠的堅城。」

18耶和華說:「即使在那時,我也不會徹底毀滅你們。 19耶利米啊,如果有人問,『為什麼我們的上帝耶和華這樣待我們?』你可以對他們說,『你們怎樣背棄耶和華,在自己的土地上供奉外族的神明,也要怎樣在異地他鄉服侍外族人。』

20「要在猶大雅各家高聲宣佈,

21『聽著,你們這群愚昧無知的人啊,

你們視而不見,

聽而不聞。

22難道你們不敬畏我嗎?

這是耶和華說的。

難道你們在我面前不顫抖嗎?

我以沙石為海的界限,

使水永遠不能越過它。

洶湧的波濤不能逾越,

澎湃的海浪不能漫過。

23但你們這些人頑固不化,

悖逆成性。

你們離我而去。

24你們心中從未說,

我們要敬畏我們的上帝耶和華,

祂按時降下秋雨和春雨,

讓我們按時收割。

25你們的罪過使你們不再風調雨順,

你們的罪惡使你們失去祝福。』

26我的子民中有惡人,

他們像捕鳥人一樣埋伏等候,

設下網羅陷害人。

27他們的家裡充滿了詭詐,

就像籠子裝滿了鳥。

他們變得有財有勢,

28吃得肥胖紅潤,

壞事做盡,不為孤兒伸冤,

不為窮人主持公道。」

29耶和華說:「我怎能坐視不理呢?

我怎能不懲罰這樣的國家呢?

30這地方發生了一件令人震驚、恐懼的事,

31就是先知說假預言,

祭司濫用權力,

我的子民卻以此為樂。

但當最後的結局來臨時,

他們還能做什麼呢?

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 5:1-31

Palibe Munthu Wolungama

1“Pitani uku ndi uku mʼmisewu ya Yerusalemu,

mudzionere nokha,

funafunani mʼmabwalo ake.

Ngati mungapeze munthu mmodzi

amene amachita zachilungamo ndi kufunafuna choonadi,

ndipo ndidzakhululukira mzinda uno.

2Ngakhale anthu akulumbira kuti, ‘Pali Yehova wamoyo,’

komabe akungolumbira mwachinyengo.”

3Inu Yehova, kodi suja mumafuna anthu onena zoona?

Inu munawakantha anthuwo, koma sanamve kupweteka;

munawaphwanya anthuwo, koma sanatengepo phunziro.

Anawumitsa mitima yawo ngati mwala

ndipo anakaniratu kulapa.

4Ndiye ndinati, “Awa ndi amphawi chabe;

anthu ochita zopusa.

Sadziwa njira ya Yehova,

sazindikira zimene Mulungu wawo amafuna.

5Tsono ndidzapita kwa atsogoleri

ndi kukayankhula nawo;

ndithu iwo amadziwa njira ya Yehova,

amadziwa zomwe Mulungu wawo amafuna.”

Koma ayi, iwonso anathyola goli la Yehova

ndipo anadula msinga zawo.

6Choncho mkango wochokera ku nkhalango udzawapha,

mmbulu wochokera ku thengo udzawawononga,

kambuku adzawabisalira pafupi ndi mizinda yawo

kuti akhadzule aliyense amene adzayesera kutuluka mʼmizindamo

pakuti kuwukira kwawo ndi kwakukulu

ndipo abwerera mʼmbuyo kwambiri.

7Yehova akuti, “Kodi ndingakukhululukireni bwanji ndi zimene mwachita?

Ana anu andisiya Ine

ndipo amapembedza milungu imene si milungu konse.

Ine ndinawapatsa zonse zimene ankasowa,

komabe iwo anachita chigololo

namasonkhana ku nyumba za akazi achiwerewere.

8Monga amachitira akavalo onenepa akamamemesa,

aliyense wa iwo ankathamangira mkazi wa mnzake.

9Tsono ndingaleke kuwalanga chifukwa cha zimenezi?”

akutero Yehova.

“Kodi nʼkuleka kuwulipsira

mtundu woterewu?

10“Pitani ku minda yake ya mipesa ndi kukayiwononga,

koma musakayiwononge kotheratu.

Sadzani nthambi zake

pakuti anthu amenewa si a Yehova.

11Nyumba ya Israeli ndi nyumba ya Yuda

onse akhala osakhulupirika kotheratu kwa Ine.”

12Iwowa ankanama ponena za Yehova kuti,

“Yehova sangachite zimenezi!

Choyipa sichidzatigwera;

sitidzaona nkhondo kapena njala.

13Mawu a aneneri azidzangopita ngati mphepo;

ndipo mwa iwo mulibe uthenga wa Yehova.

Choncho zimene amanena zidzawachitikira okha.”

14Chifukwa chake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse akuti,

“Popeza kuti anthu awa ayankhula mawu amenewa,

tsono mawu anga ndidzawasandutsa moto mʼkamwa mwako

ndipo anthu awa ndidzawasandutsa nkhuni zimene moto udzapserezeretu.

15Inu Aisraeli,” Yehova akuti,

“Ndikukubweretserani mtundu wa anthu ochokera kutali,

ndi mtundu umene sunagonjetsedwepo,

mtundu wakalekale umene chiyankhulo chawo inu simuchidziwa,

zimene akunena inu simungazimvetse.

16Zida zawo za nkhondo zapha anthu ambirimbiri;

onsewo ndi ankhondo amphamvu okhaokha.

17Adzakudyerani zokolola zanu ndi chakudya chanu,

adzapha ana anu aamuna ndi aakazi;

adzakupherani nkhosa zanu ndi ngʼombe zanu,

adzawononga mpesa wanu ndi mikuyu yanu.

Ndi malupanga awo adzagwetsa

mizinda yanu yotetezedwa imene mumayidalira.

18“Komabe pa masiku amenewo sindidzakuwonongani kotheratu,” akutero Yehova. 19Ndipo pamene anthu adzafunsa Yehova kuti, “Chifukwa chiyani Yehova Mulungu wathu wachita zimenezi?” Iwe udzawawuze kuti, “Monga momwe mwasiyira Ine ndi kutumikira milungu yachilendo mʼdziko mwanu, momwemonso mudzatumikira anthu a mʼdzikonso lachilendo.”

20“Lengeza izi kwa ana a Yakobo

ndipo mulalikire kwa anthu a ku Yuda kuti,

21Imvani izi, inu anthu opusa ndi opanda nzeru,

inu amene maso muli nawo koma simupenya,

amene makutu muli nawo koma simumva.

22Kodi simuyenera kuchita nane mantha?”

Akutero Yehova.

“Kodi simuyenera kunjenjemera pamaso panga?

Ine ndinayika mchenga kuti ukhale malire a nyanja,

malire a muyaya amene nyanjayo singadutsepo.

Mafunde angawombe motani, koma sangathe kupitirira malirewo;

mafunde angakokome motani, koma sangadutse malirewo.

23Koma anthu awa ndi nkhutukumve ndiponso a mitima yowukira;

andifulatira ndipo andisiyiratu.

24Sananenepo mʼmitima mwawo kuti,

‘Tiyeni tizipembedza Yehova Mulungu wathu.

Kodi suja amatipatsa pa nthawi yake mvula yachizimalupsa ndi yamasika.

Iye salephera konse kutipatsa nyengo ya kholola.’

25Koma zolakwa zanu zalepheretsa zonsezi;

ndipo machimo anu akumanitsani zabwino.

26“Pakati pa anthu anga pali anthu ena oyipa

amene amabisalira anzawo monga amachitira mlenje mbalame

ndiponso ngati amene amatchera misampha kuti akole anthu anzawo.

27Nyumba zawo zadzaza ndi chuma chochipeza mwa chinyengo

ngati zikwere zodzaza ndi mbalame.

Nʼchifukwa chake asanduka otchuka ndi olemera.

28Ndipo ananenepa ndi kukhala ndi matupi osalala.

Ntchito zawo zoyipa nʼzopanda malire;

saweruza mwachilungamo nkhani ya ana amasiye kuti iyende bwino,

sateteza ufulu wa anthu osauka.

29Kodi Ine ndingaleke kuwalanga chifukwa cha zimenezi?

Kodi ndisawulipsire

mtundu woterewu?

Akutero Yehova.

30“Chinthu chothetsa nzeru ndi choopsa kwambiri

chachitika mʼdzikomo:

31Aneneri akunenera zabodza,

ndipo ansembe akuvomerezana nawo,

ndipo anthu anga akukonda zimenezi.

Koma mudzatani potsiriza?