耶利米書 25 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

耶利米書 25:1-38

預言被擄七十年

1猶大約西亞的兒子約雅敬執政第四年,即巴比倫尼布甲尼撒元年,耶和華告訴了耶利米有關猶大百姓的事。 2耶利米先知對猶大人和耶路撒冷的居民說: 3「從猶大亞們的兒子約西亞執政第十三年,到今天已有二十三年。在這期間,我不斷把耶和華對我說的話傳給你們,你們卻充耳不聞。 4耶和華屢次差遣祂的僕人——眾先知警告你們,你們卻充耳不聞,毫不理會。 5他們對你們說,『要改邪歸正,停止作惡,以便可以永遠住在耶和華賜給你們和你們祖先的土地上。 6不要隨從、供奉、祭拜其他神明,不要製造神像惹耶和華發怒,免得祂懲罰你們。』」 7耶和華說:「然而,你們不聽我的話,製造神像惹我發怒,自招懲罰。」

8因此,萬軍之耶和華說:「由於你們不遵行我的命令, 9我要召集北方各族和我的僕人巴比倫尼布甲尼撒,去攻擊這片土地和其中的居民以及周圍各國。我要徹底毀滅他們,使他們的下場很可怕、令人嗤笑、土地永遠荒涼。這是耶和華說的。 10我要使他們的歡樂聲、新郎新娘的歡笑聲、推磨聲和燈光都消失。 11整片土地要變得荒涼可怕,他們要臣服於巴比倫王七十年。 12七十年後,我要報應巴比倫王和他國民迦勒底人的罪,使他們的土地永遠荒涼。這是耶和華說的。 13我藉耶利米所說有關列國的預言都記在這書上了,我的話必應驗在他們的土地上。 14他們必受許多國家和強大君王的奴役,我要按他們的所作所為報應他們。」

上帝審判列國

15以色列的上帝耶和華對我說:「你從我手中接過這盛滿我烈怒的酒杯,到我差遣你去的國家給他們喝。 16他們喝了這杯烈怒後必東倒西歪、行為瘋狂,因為我要使戰禍臨到他們。」 17於是,我從耶和華手中接過杯,奉祂的差遣到列國去給他們喝。 18我給耶路撒冷猶大的城邑,以及猶大的君王和官員喝這杯烈怒,使他們的城邑淪為廢墟,令人驚懼,被嘲笑和咒詛,正如今日一樣。 19喝這杯烈怒的還有埃及王法老及其王公大臣和全體百姓, 20他們當中所有的外族人,烏斯的眾王和統治亞實基倫迦薩以革倫以及亞實突餘民的非利士眾王, 21以東摩押亞捫人, 22泰爾的眾王、西頓的眾王和海島上的眾王, 23底但提瑪布斯和所有剃鬢髮的人, 24阿拉伯的眾王和荒野各族的諸王, 25心利的眾王、以攔的眾王和瑪代的眾王, 26北方諸王——無論遠近、一個接一個,以及天下萬國,最後是巴比倫王。 27耶和華對我說:「你要告訴他們,以色列的上帝——萬軍之耶和華說,『你們要喝這杯烈怒,喝得大醉、嘔吐、倒地不起,因為我要使戰爭臨到你們。』 28如果他們不肯從你手中接過杯來喝,你就告訴他們,萬軍之耶和華說,『你們必須喝! 29看啊,我已在屬我的城中降下災禍,難道你們可以逃脫懲罰嗎?你們必逃不過懲罰,因為我要使戰爭臨到天下萬民。』這是萬軍之耶和華說的。 30耶利米啊,你要告訴他們這些預言,

『耶和華要在高天怒吼,

從祂的聖所發出雷鳴;

祂要向祂的子民怒吼,

向地上的居民吶喊,

好像踩踏葡萄的人一樣。

31耶和華的聲音傳到地極,

因為祂要指控列國,審判萬民,

使惡人喪身刀下。

這是耶和華說的。』」

32萬軍之耶和華說:

「看啊,災難正蔓延到列國,

有暴風從地極捲起。」

33到那日,遍地都是被耶和華殺戮的人,無人哀悼、收殮和埋葬,他們好像地上的糞便。

34你們這群牧人啊,要悲哀哭泣!

你們這群百姓的首領啊,

要在灰塵中傷心地打滾!

因為你們被宰殺、驅散的時候到了,

你們將像精美的器皿一樣被摔得粉碎。

35牧人必無路可逃,

百姓的首領必無處藏身。

36聽聽牧人的哭喊,

百姓首領的哀號吧,

因為耶和華正在毀滅他們的家園。

37因為耶和華的烈怒,

寧靜的草場變得一片荒涼。

38耶和華離開了祂的居所,

就像獅子離開了洞穴。

他們的土地因刀劍的蹂躪和耶和華的烈怒而一片荒涼。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 25:1-38

Zaka 70 za Ukapolo

1Yehova anayankhula ndi Yeremiya za anthu onse a ku Yuda mʼchaka chachinayi cha ufumu wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda, chimene chinali chaka choyamba cha ufumu wa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni. 2Choncho mneneri Yeremiya anawuza anthu onse a ku Yuda pamodzi ndi onse amene amakhala mu Yerusalemu kuti: 3Kwa zaka 23, kuyambira chaka cha 13 cha ufumu wa Yosiya mwana wa Amoni mfumu ya ku Yuda mpaka lero lino, Yehova wakhala akundipatsa mauthenga ake ndipo ine ndakhala ndikuyankhula ndi inu kawirikawiri, koma inu simunamvere.

4Ndipo ngakhale Yehova kawirikawiri wakhala akukutumizirani atumiki ake onse, aneneri, inuyo simunamvere kapena kutchera khutu. 5Aneneriwo ankanena kuti, “Ngati aliyense wa inu abwerere, kusiya njira zake zoyipa ndi machitidwe ake oyipa, ndiye kuti mudzakhala mʼdziko limene Yehova anapereka kwa makolo anu kwamuyaya. 6Musatsatire milungu ina nʼkuyitumikira ndi kuyipembedza. Musapute mkwiyo wanga ndi mafano amene mwapanga ndi manja anu. Mukatero Ine sindidzakuwonongani.

7“Koma inu simunandimvere,” akutero Yehova, “ndipo munaputa mkwiyo wanga ndi mafano amene munapanga ndi manja anu. Choncho munadziwononga nokha.”

8Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Chifukwa simunamvere mawu anga, 9ndidzayitana mafuko onse akumpoto, pamodzi ndi mtumiki wanga Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni,” akutero Yehova, “ndipo adzathira nkhondo dziko lino ndi anthu ake pamodzi ndi mitundu yonse ya anthu ozungulira dzikoli. Ndidzawawononga kwathunthu ndi kuwasandutsa chinthu chochititsa mantha ndi chonyozeka, mpaka muyaya. 10Ndidzathetsa mfuwu wachimwemwe ndi wachisangalalo, mawu a mkwati ndi mkwatibwi, phokoso la mphero ndi kuwala kwa nyale. 11Dziko lonse lidzakhala bwinja ndi chipululu, ndipo mitundu ina idzatumikira mfumu ya ku Babuloni kwa 70.

12“Koma zaka 70 zikadzatha, ndidzalanga mfumu ya ku Babuloni pamodzi ndi anthu ake, chifukwa cha zolakwa zawo,” akutero Yehova, “ndipo dziko lawo lidzakhala chipululu mpaka muyaya. 13Ndidzachita zinthu zonse zimene ndinayankhula zotsutsa dzikolo, zonse zimene zalembedwa mʼbuku lino, ndiponso zonse zimene Yeremiya analosera zotsutsa anthu amenewa. 14Iwo eni adzakhala akapolo a anthu a mitundu yochuluka ndi mafumu amphamvu. Ndidzawabwezera molingana ndi zochita zawo ndi ntchito za manja awo.”

Chikho cha Ukali wa Mulungu

15Yehova, Mulungu wa Israeli, anandiwuza kuti, “Tenga chikho ichi chodzaza ndi vinyo wa ukali wanga, ndipo ukamwetse anthu a mitundu yonse kumene ndikukutuma. 16Akadzamwa adzayamba kudzandira ndi kuchita misala chifukwa cha nkhondo imene ndikuyitumiza pakati pawo.”

17Choncho ine ndinatenga chikhocho mʼdzanja la Yehova ndipo ndinamwetsa mitundu yonse ya anthu kumene Iye ananditumako: 18Anandituma ku Yerusalemu ndi ku mizinda ya Yuda, kwa mafumu ake ndi nduna zake kuti ndikawasandutse ngati bwinja ndi chinthu chochititsa mantha ndi chonyozeka ndiponso chotembereredwa, monga mmene alili lero lino. 19Ananditumanso kwa Farao, mfumu ya ku Igupto, kwa atumiki ake, nduna zake ndi kwa anthu ake onse, 20ndi kwa anthu ena onse a mitundu yachilendo; mafumu onse a ku Uzi; mafumu onse a Afilisti, a ku Asikeloni, ku Gaza, ku Ekroni ndiponso kwa anthu a ku chigwa chotsala cha Asidodi; 21Edomu, Mowabu ndi Amoni. 22Ananditumanso kwa mafumu onse a ku Turo ndi ku Sidoni; kwa mafumu a kutsidya la nyanja; 23ku Dedani, ku Tema, ku Buzi ndi kwa onse ometa chamʼmbali. 24Ananditumanso kwa mafumu onse a ku Arabiya ndi mafumu onse a anthu achilendo amene amakhala mʼchipululu. 25Anandituma kwa mafumu onse a ku Zimuri, Elamu ndi Mediya; 26ndiponso kwa mafumu onse a kumpoto, akufupi ndi kutali omwe, mafumu onse a dziko lapansi. Ndipo potsiriza pake, idzamwenso ndi mfumu Sesaki.

27“Ndipo uwawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Imwani, ledzerani ndipo musanze, mugwe osadzukanso chifukwa cha nkhondo imene ndikutumiza pakati panu.’ 28Koma ngati akana kutenga chikhocho mʼdzanja lako ndi kumwa, uwawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti: Muyenera kumwa ndithu!’ ” 29Taonani, tsopano ndiyamba kulanga mzinda uno umene umadziwika ndi dzina langa. Kodi inu muganiza kuti simudzalangidwa? Ayi, simudzapulumuka chifukwa ndikutumiza nkhondo pa onse okhala pa dziko lapansi, akutero Yehova Wamphamvuzonse.

30“Tsopano iwe nenera mawu owatsutsa ndipo uwawuze kuti,

“ ‘Yehova adzabangula kumwamba;

mawu ake adzamveka ngati bingu kuchokera ku malo ake opatulika.

Adzabangula mwamphamvu kukalipira dziko lake.

Iye adzafuwula ngati anthu oponda mphesa,

kukalipira onse amene akukhala pa dziko lapansi.

31Phokoso lalikulu lidzamveka mpaka kumalekezero a dziko lonse lapansi,

chifukwa Yehova adzazenga mlandu anthu a mitundu yonse;

adzaweruza mtundu wonse wa anthu

ndipo oyipa adzawapha ndi lupanga,’ ”

akutero Yehova.

32Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Taonani! Mavuto akuti akachoka

pa mtundu wina akukagwa pa mtundu wina;

mphepo ya mkuntho ikuyambira

ku malekezero a dziko.”

33Pa tsiku limenelo, onse ophedwa ndi Yehova adzangoti mbwee ponseponse, pa dziko lonse lapansi. Palibe amene adzawalire kapena kusonkhanitsa mitemboyo kuti ikayikidwe mʼmanda, koma idzakhala mbwee ngati ndowe.

34Khetsani misozi ndi kufuwula mwamphamvu, abusa inu;

gubudukani pa fumbi, inu atsogoleri a nkhosa.

Pakuti nthawi yanu yophedwa yafika;

mudzagwa ndi kuphwanyika ngati mbiya yabwino kwambiri.

35Abusa adzasowa kothawira,

atsogoleri a nkhosa adzasowa malo opulumukira.

36Imvani kulira kwa abusa,

atsogoleri a nkhosa akulira,

chifukwa Yehova akuwononga msipu wawo.

37Makola awo a nkhosa amene anali pamtendere adzasanduka bwinja

chifukwa cha mkwiyo woopsa wa Yehova.

38Ngati mkango, Yehova wasiya phanga lake,

pakuti dziko lawo lasanduka chipululu

chifukwa cha nkhondo ya owazunza

ndiponso chifukwa cha mkwiyo woopsa wa Yehova.