耶利米書 21 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

耶利米書 21:1-14

預言耶路撒冷的淪陷

1西底迦王派瑪基雅的兒子巴施戶珥瑪西雅的兒子西番雅祭司來見耶利米的時候,耶利米聽到了耶和華的話。當時,他們對耶利米說: 2「請你為我們求問耶和華,因為巴比倫尼布甲尼撒來攻打我們,或許耶和華會像以往一樣行神蹟,使敵人撤軍。」

3耶利米對他們說:「你們要告訴西底迦4以色列的上帝耶和華說,『看啊,你們與圍城的巴比倫王及其率領的迦勒底人作戰,我要把你們的兵器掉轉過來,我要把它們收集在城中心。 5我要在烈怒中伸出大能的臂膀下手擊打你們, 6我要擊打這城裡的居民和牲畜,使他們死於瘟疫。 7然後,我要把猶大西底迦及其臣僕以及城中逃過瘟疫、戰爭和饑荒的人都交給巴比倫尼布甲尼撒等仇敵,使他們落在想殺滅他們的人手中。巴比倫王必殘酷無情地殺戮他們。這是耶和華說的。』

8耶利米啊,你要告訴百姓,『耶和華說,看啊,我把生命之路和死亡之路擺在你們面前, 9留在這城裡的必死於戰爭、饑荒和瘟疫,出城向迦勒底人投降的必保全性命、逃過一死。 10我必嚴懲這城,向它降禍不降福。它必落在巴比倫王手中,被付之一炬。這是耶和華說的。』

11「你要對猶大的王室說,『你們要聽耶和華的話。 12大衛家啊,耶和華說,

『你們要天天秉公行義,

從壓迫者手中解救受剝削的人,

免得你們的惡行激起我的怒火,

如烈焰燃起,無人能滅。

13耶和華說,耶路撒冷啊,

你座落在山谷之上,

如平原的磐石,

自以為無人能攻擊你,

無人能闖入你的住處。

但我要攻擊你,

14照你的所作所為懲罰你;

我要點燃你的樹林,

燒光你周圍的一切。

這是耶和華說的。』」

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 21:1-14

Mulungu Akana Pempho la Zedekiya

1Mfumu Zedekiya inatuma Pasuri mwana wa Malikiya ndi wansembe Zefaniya mwana wa Maseya kwa Yeremiya. 2Iwo amati akanene kwa Yeremiya mawu akuti, “Tinenere kwa Yehova chifukwa Nebukadinezara mfumu ya Babuloni akutithira nkhondo. Mwina mwake Yehova nʼkutichitira zodabwitsa kuti Nebukadinezarayo achoke kwathu kuno.”

3Koma Yehova anawuza Yeremiya kuti ayankhe Pasuri ndi Zefaniya kuti, “Kamuwuzeni Zedekiya kuti, 4‘Yehova, Mulungu wa Israeli akuti ndikulandeni zida zimene zili mʼmanja mwanu zimene mukugwiritsa ntchito polimbana ndi mfumu ya ku Babuloni ndi ankhondo ake amene akuzingani kunja kwa lingali. Ndipo ndidzasonkhanitsa zidazo mʼkati mwa mzindawu. 5Ineyo mwini wakene ndi mkono wotambasula ndi dzanja lamphamvu, ndidzachita nanu nkhondo ndili wokwiya, wokalipa ndi waukali. 6Ndidzakantha amene amakhala mu mzinda muno, anthu pamodzi ndi zirombo, ndipo zidzafa ndi mliri woopsa. 7Pambuyo pake, ndidzapereka Zedekiya mfumu ya ku Yuda, nduna zake pamodzi ndi anthu a mu mzinda muno amene adzapulumuke pa nthawi ya mliri, lupanga ndi njala kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni ndi kwa adani awo amene ankafuna kuwapha. Iye adzawapha ndi lupanga. Sadzawachitira chifundo kapena kuwamvera chisoni kapenanso kuwakomera mtima.’

8“Yehova anati ndiwawuzenso anthu amenewa kuti asankhe pakati pa moyo ndi imfa. 9Aliyense amene akhale mu mzinda muno adzaphedwa ndi lupanga, njala kapena mliri. Koma aliyense amene apite kukadzipereka kwa Ababuloni amene akuzinganiwa adzakhala ndi moyo, adzapulumuka. 10Ine ndatsimikiza kuchitira mzinda uno choyipa osati chabwino, akutero Yehova. Udzaperekedwa mʼdzanja la mfumu ya ku Babuloni, ndipo iyeyo adzawutentha ndi moto.

11“Komanso, uwuze banja laufumu la Yuda kuti, ‘Imva mawu a Yehova; 12inu a mʼbanja la Davide, Yehova akuti,

“ ‘Weruzani mwachilungamo mmawa uliwonse;

pulumutsani mʼdzanja la wozunza

aliyense amene walandidwa katundu wake,

kuopa kuti ukali wanga ungabuke

ndi kuyaka ngati moto wosazimitsika

chifukwa cha zoyipa zimene mwachita.

13Ndidzalimbana nanu,

inu amene mukukhala pamwamba pa chigwa,

inu okhala ngati thanthwe lapachidikha,

akutero Yehova.

Inu amene mumanena kuti, ‘Ndani amene angabwere kudzalimbana nafe?

Ndani amene angathe kulowa mʼmalinga mwathu?’

14Ndidzakulangani molingana ndi ntchito zanu,

akutero Yehova.

Ndidzatentha nkhalango zanu;

moto udzapsereza zonse zimene zakuzungulirani.’ ”