耶利米書 14 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

耶利米書 14:1-22

預言旱災

1耶和華告訴耶利米有關旱災的事:

2猶大充滿悲泣,

她的城邑衰敗,

人人坐在地上痛哭,

耶路撒冷哀鳴四起。

3貴族派僕人去水池打水,

僕人去那裡發現沒有水,

就帶著空瓶垂頭喪氣、

羞愧難當地回去了。

4天不下雨,

土地乾裂,

農夫沮喪地抱著頭。

5因為沒有草,

田野的母鹿拋棄了剛生下來的小鹿;

6因為沒有草,

野驢站在光禿的山頭上像豺狼一樣喘氣,雙目無神。」

7耶和華啊,雖然我們的罪控告我們,

我們屢屢叛逆得罪你,

求你為了自己的尊名而拯救我們。

8以色列的盼望和患難時的救主啊,

你為什麼在這裡像一個異鄉人,

像一個只住一夜的旅客呢?

9你為什麼像一個受驚的人,

像一個無力救人的勇士呢?

耶和華啊,你一直都在我們中間,

我們屬於你的名下,

求你不要拋棄我們。

10論到這些百姓,耶和華這樣說:

「他們喜歡流浪,

不約束自己的腳步,

因此耶和華不喜歡他們。

現在祂要清算他們的罪惡,

追討他們的罪。」

11耶和華對我說:「你不要為這百姓禱告。 12他們禁食,我也不會聽他們的呼求;他們獻上燔祭和素祭,我也不會悅納。我要用戰爭、饑荒和瘟疫滅絕他們。」 13我說:「主耶和華啊!眾先知不停地告訴他們不會有戰爭,也不會遭遇饑荒,說耶和華必在這地方賜給他們永久的平安。」

14耶和華對我說:「那些先知奉我的名說假預言,我並沒有差派他們,沒有委任他們,也沒有對他們說話。他們對你們說的預言是假異象,是占卜,是憑空捏造。 15我沒有差派他們,他們卻奉我的名說這地方必沒有戰爭和饑荒。他們必死於戰爭和饑荒。這是耶和華說的。 16至於聽他們說預言的人以及那些人的妻子兒女,必因饑荒和戰爭而曝屍耶路撒冷街頭。因為我要使他們受到應得的報應。

17耶利米,你要對他們說,

『讓我晝夜淚眼汪汪吧,

因為我的同胞遭受重創,

遍體鱗傷。

18我走到田間,

眼前是具具被殺的屍體;

我進入城裡,

見饑荒肆虐,

祭司和先知也流亡異鄉14·18 祭司和先知也流亡異鄉」或譯「連祭司和先知也渾渾噩噩,不知道自己做什麼」。。』」

19耶和華啊,你完全丟棄猶大了嗎?

你厭惡錫安嗎?

你為什麼把我們打得傷痕纍纍,以致無法醫治?

我們期待平安,卻沒有平安;

渴望得到醫治,卻飽受驚嚇。

20耶和華啊,我們承認自己和我們祖先的罪,

我們都得罪了你。

21為了你的尊名,

求你不要厭惡我們,

不要讓你榮耀的寶座蒙羞。

求你顧念你與我們立的約,

不要廢除它。

22在列國供奉的偶像中,

誰能賜下雨水呢?

天能自降甘霖嗎?

我們的上帝耶和華啊,

難道不是只有你能行這些事嗎?

是你賜雨水降甘霖,

所以我們仰望你。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 14:1-22

Chilala, Njala, Lupanga

1Awa ndi mawu amene Yehova anamuwuza Yeremiya onena za chilala:

2“Yuda akulira,

mizinda yake ikuvutika;

anthu ake adzigwetsa pansi mwachisoni,

kulira kwa Yerusalemu kwakula.

3Anthu awo wolemekezeka akutuma antchito awo kuti akatunge madzi.

Apita ku zitsime

osapezako madzi.

Choncho amabwerera ndi mitsuko yopanda madzi.

Amanyazi ndi othedwa nzeru

adziphimba kumaso.

4Popeza pansi pawumiratu

chifukwa kulibe madzi,

alimi ali ndi manyazi

ndipo amphimba nkhope zawo.

5Ngakhale mbawala yayikazi

ikusiya mwana wake wakhanda ku thengo

chifukwa kulibe msipu.

6Mbidzi zikuyima pa zitunda zopanda kanthu

nʼkumapuma wefuwefu ngati nkhandwe;

maso awo achita chidima

chifukwa chosowa msipu.”

7Anthu akuti, “Ngakhale machimo athu akutitsutsa,

koma Inu Yehova chitanipo kanthu chifukwa cha dzina lanu.

Pakuti kusakhulupirika kwathu nʼkwakukulu;

ife takuchimwirani.

8Inu Yehova amene Aisraeli amakukhulupirirani

ndi amene mumawapulumutsa pa nthawi ya masautso,

chifukwa chiyani mukukhala ngati mlendo mʼdziko muno?

Chifukwa chiyani muli ngati wapaulendo amene akungogona tsiku limodzi?

9Chifukwa chiyani muli ngati munthu amene wadzidzimutsidwa,

kapena ngati wankhondo amene alibe mphamvu yopulumutsa?

Komabe Inu Yehova, muli pakati pathu,

ndipo tikudziwika ndi dzina lanu;

musatitaye ife!”

10Zimene Yehova akunena za anthuwa ndi izi:

“Iwo amakonda kuyendayenda kwambiri;

samatha kudziretsa.

Nʼchifukwa chake Ine Yehova sindingawalandire,

ndipo tsopano ndidzakumbukira zoyipa zawo

ndi kuwalanga chifukwa cha machimo awo.”

11Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Usawapempherere anthu awa kuti zinthu ziwayendere bwino. 12Ngakhale asale zakudya, Ine sindidzamva kulira kwawo; ngakhale apereke nsembe zopsereza ndi chopereka cha chakudya, sindidzazilandira. Mʼmalo mwake, ndidzawapha ndi lupanga, njala ndi mliri.”

13Koma ine ndinati, “Aa, Ambuye Yehova, aneneri amawawuza anthuwo kuti, sadzaphedwa ndi lupanga kapena kuvutika ndi njala. Koma kuti Inu mudzawapatsa mtendere wokhawokha pamalo pano.”

14Ndipo Yehova anandiwuza kuti, “Ndi zabodza kuti aneneriwa akunenera mʼdzina langa. Ine sindinawatume kapena kuwasankha kapenanso kuyankhula nawo. Iwo amakuwuzani zinthu zabodza zomwe amati anaziona mʼmasomphenya, kapena pogwiritsa ntchito mawula achabechabe. Zimene amayankhula ndi zongopeka mʼmutu mwawo. 15Nʼchifukwa chake Ine Yehova ndikuti aneneri amenewa akulosera mʼdzina langa pamene Ine sindinawatume. Iwo amati simudzafa pa nkhondo kapena ndi njala mʼdziko muno. Koma tsono ndi iwowo, aneneriwa amene adzafe pa nkhondo kapena ndi njala. 16Ndipo anthu amene anawaloserawo adzaponyedwa mʼmisewu ya mu Yerusalemu atafa ndi njala ndi lupanga. Sipadzapezeka wowayika mʼmanda popeza iwowo, akazi awo, ana awo aamuna, onse adzakhala atafa. Ine ndidzawagwetsera chilango chowayenera.

17“Awuze mawu awa:

“ ‘Maso anga akugwetsa misozi kosalekeza

usana ndi usiku;

chifukwa anthu anga okondedwa

apwetekeka kwambiri,

akanthidwa kwambiri.

18Ndikapita kuthengo,

ndikuona amene aphedwa ndi lupanga;

ndikapita mu mzinda,

ndikuona amene asakazidwa ndi njala.

Ngakhale aneneri pamodzi

ndi ansembe onse atengedwa.’ ”

19Kodi anthu a ku Yuda mwawakana kwathunthu?

Kodi mtima wanu wanyansidwa nawo anthu a ku Ziyoni?

Chifukwa chiyani mwatikantha chotere

kuti sitingathenso kuchira?

Ife tinayembekezera mtendere

koma palibe chabwino chomwe chabwera,

tinayembekezera kuchira

koma panali kuopsezedwa kokhakokha.

20Inu Yehova, ife tikuvomereza kuyipa kwathu

ndiponso kulakwa kwa makolo athu;

ndithu ife tinakuchimwiranidi.

21Musatikane kuopa kuti dzina lanu linganyozedwe;

musanyoze mpando wanu waufumu waulemerero.

Kumbukirani pangano lanu ndi ife

ndipo musachiphwanye.

22Mwa milungu yachabechabe ya anthu a mitundu ina,

kodi pali mulungu amene angagwetse mvula?

Ife chikhulupiriro chathu chili pa Inu,

popeza Inu nokha ndinu Yehova Mulungu wathu

amene mukhoza kuchita zimenezi.