約書亞記 20 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

約書亞記 20:1-9

避難城

1耶和華對約書亞說: 2「你吩咐以色列人,照我以前藉摩西所吩咐你們的,設立一些城邑作為避難城, 3好讓那些誤殺了人的可以逃到那裡,免遭仇人追殺。 4逃進城的人要先站在城門口,向避難城的長老陳明事情的經過,長老就把他們收容到城裡,給他們地方住。 5如果他們的仇人追到,長老們不可把他們交出來,因為他們是無意殺的,跟被殺者無冤無仇。 6這些人要住在城內,直到在會眾面前受了審訊,並且還要等到在任的大祭司死後,才可離城回鄉。」

7於是,民眾便設立拿弗他利山區加利利境內的基低斯以法蓮山區的示劍猶大山區的基列·亞巴,即希伯崙作為避難城。 8他們又在約旦河、耶利哥東面空曠的平原上設立呂便支派的比悉迦得支派基列境內的拉末瑪拿西支派巴珊境內的哥蘭作為避難城。 9這是為以色列人和那些從外地來寄居的人所設立的避難城,誤殺了人的可以逃到那裡,不致未在會眾面前受審便死在報仇的人手裡。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoswa 20:1-9

Mizinda Yopulumukiramo

1Pambuyo pake Yehova anati kwa Yoswa: 2“Uza Aisraeli kuti apatule mizinda yopulumukiramo, monga ine ndinakulangizira kudzera mwa Mose, 3kuti aliyense amene wapha munthu mosazindikira osati mwadala azithawirako. Motero adzatetezedwa kwa wolipsira. 4Ngati munthu wathawira ku umodzi mwa mizinda imeneyi, akafike pa malo oweruzira milandu amene ali pa chipata cha mzindawo ndipo akafotokoze mlandu wake pamaso pa akuluakulu a mzindawo. Kenaka iwo adzamulola kulowa mu mzinda wawo ndi kumupatsa malo woti akhale nawo. 5Ngati munthu wolipsirayo amutsatira komweko atsogoleriwo asapereke munthu wakuphayo chifukwa anapha Mwisraeli mnzakeyo mosazindikira, osati mwachiwembu. 6Munthu wakuphayo adzakhalabe mu mzindawo mpaka atayimbidwa mlandu pamaso pa gulu lonse, ndiponso mpaka atamwalira mkulu wa ansembe amene akutumikira pa nthawiyo. Pamenepo munthuyo atha kubwereranso ku mudzi kwawo kumene anachoka mothawa kuja.”

7Choncho iwo anapatula Kedesi mʼdera la Galileya ku mapiri a Nafutali, Sekemu ku mapiri a Efereimu, ndi Kiriati Ariba (ndiye Hebroni) ku mapiri a Yuda. 8Kummawa kwa Yorodani, mʼmapiri a chipululu a kummawa kwa Yeriko, anapatula Bezeri pakati pa dera la fuko la Rubeni. Anapatulanso Ramoti ku Giliyadi mʼdera la fuko la Gadi, ndiponso Golani ku Basani mʼdera la fuko la Manase. 9Imeneyi ndiyo inali mizinda yopulumukiramo ya Aisraeli onse ngakhalenso mlendo wokhala pakati pawo. Munthu aliyense wopha mnzake mwangozi ankathawira ku mizinda imeneyi. Munthu wolipsira sankaloledwa kuti aphe munthu wothawayo ngati mlandu wake sunazengedwe pamaso pa gulu lonse.