箴言 4 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

箴言 4:1-27

父親的教誨

1孩子們啊,

你們要聽從父親的教誨,

留心學習,以便領悟,

2因為我給你們的訓誨是美好的,

不可背棄我的教導。

3我年幼時在父親身邊,

是母親唯一的寵兒。

4父親教導我說:

「要牢記我的話,

遵守我的誡命,就必存活。

5你要尋求智慧和悟性,

不要忘記或違背我的吩咐。

6不可離棄智慧,智慧必護佑你;

你要熱愛智慧,智慧必看顧你。

7智慧至上,要尋求智慧,

要不惜一切,求得悟性。

8高舉智慧,她必使你受尊崇;

擁抱智慧,她必使你得尊榮。

9她必為你戴上華冠,

加上榮冕。」

10孩子啊,你要聽從我的教導,

就必延年益壽。

11我已經指示你走智慧之道,

引導你行正確的路。

12你行走,必不受妨礙;

你奔跑,絕不會跌倒。

13你要持守教誨,不要鬆懈;

要守護好,因為那是你的生命。

14不要涉足惡人的道,

不要行走壞人的路;

15要避開,不可踏足,

要繞道而行。

16因為他們不作惡就無法入睡,

不絆倒人就無法安眠;

17他們吃的是邪惡餅,

喝的是殘暴酒。

18義人的道路好像黎明的曙光,

越照越亮,直到大放光明。

19惡人的道路一片幽暗,

他們不知被何物絆倒。

20孩子啊,你要聆聽我的吩咐,

側耳聽我的訓言;

21不要讓它們離開你的視線,

要牢記在心。

22因為得到它們就得到生命,

全身也必康健。

23要一絲不苟地守護你的心,

因為生命之泉從心中湧出。

24不講欺詐之言,

不說荒謬的話。

25眼睛要正視前方,

雙目要向前直看。

26要鋪平腳下的路,

使所行之道穩妥。

27不可偏右偏左,

要遠離惡事。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 4:1-27

Nzeru Iposa Zonse

1Ananu, mverani malangizo a abambo anu;

tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu.

2Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino.

Choncho musasiye malangizo anga.

3Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga;

mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga.

4Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti,

“Ugwiritse mawu anga pa mtima pako,

usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.

5Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu;

usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.

6Usasiye nzeru ndipo idzakusunga.

Uziyikonda ndipo idzakuteteza.

7Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru.

Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu.

8Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza;

ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu.

9Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako;

idzakupatsa chipewa chaufumu chaulemu.”

10Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena,

ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka.

11Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru.

Ndakutsogolera mʼnjira zolungama.

12Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana;

ukamadzathamanga, sudzapunthwa.

13Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi.

Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa.

14Usayende mʼnjira za anthu oyipa

kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa.

15Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo;

uzilambalala nʼkumangopita.

16Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa;

tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina.

17Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi

ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa.

18Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha

kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu.

19Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani;

iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa.

20Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena;

tchera khutu ku mawu anga.

21Usayiwale malangizo angawa,

koma uwasunge mu mtima mwako.

22Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza

ndipo amachiritsa thupi lake lonse.

23Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu

pakuti ndiwo magwero a moyo.

24Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota;

ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa.

25Maso ako ayangʼane patsogolo;

uziyangʼana kutsogolo molunjika.

26Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako

ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa.

27Usapatukire kumanja kapena kumanzere;

usapite kumene kuli zoyipa.