箴言 22 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

箴言 22:1-29

1美名勝過巨富,

恩寵比金銀寶貴。

2富人和窮人相同:

都由耶和華所造。

3明哲人遇禍躲避,

愚昧人前往受害。

4心存謙卑、敬畏耶和華,

必得財富、尊榮和生命。

5奸徒之道有荊棘和陷阱,

想保全生命的必須遠避。

6教導孩童走正路,

他到老也不偏離。

7富人管轄窮人,

欠債的是債主的僕人。

8播種不義的必收災禍,

他的惡勢力終必瓦解。

9慷慨的人必蒙福,

因他給窮人食物。

10趕走嘲諷者,紛爭平息,

爭吵和羞辱也會消除。

11喜愛清心、口吐恩言的人,

必與君王為友。

12耶和華的眼目護衛真理,

祂必推翻奸徒的言論。

13懶惰人說:「外面有獅子,

我會喪命街頭。」

14淫婦的口是深坑,

耶和華憎惡的人必陷進去。

15愚昧纏住孩童的心,

教棍能遠遠趕走它。

16靠壓榨窮人斂財和送禮給富人的,

都必窮困潦倒。

智者之言

17你要側耳聽智者之言,

專心領受我的教誨,

18銘記在心、隨時誦詠,

方為美事。

19今天我將這些指示你,

為要使你倚靠耶和華。

20關於謀略和知識,

我已寫給你三十條,

21要使你認識真理,

能準確答覆差你來的人。

22不可仗勢剝削貧窮人,

法庭上不可欺凌弱者,

23因為耶和華必為他們伸冤,

奪去掠奪他們之人的性命。

24不可結交脾氣暴躁者,

不要跟易怒之人來往,

25免得你沾染他們的惡習,

不能自拔。

26不要為人擊掌作保,

不要為欠債的抵押。

27如果你還不起,

連你的床也會被抬走。

28不可移動祖先定下的界石。

29你看那精明能幹的人,

他必侍立在君王面前,

不會效力於泛泛之輩。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 22:1-29

1Mbiri yabwino ndi yofunika kuposa chuma chambiri;

kupeza kuyanja nʼkwabwino kuposa siliva kapena golide.

2Wolemera ndi wosauka ndi ofanana;

onsewa anawalenga ndi Yehova.

3Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala,

koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amadzanongʼoneza bondo.

4Mphotho ya munthu wodzichepetsa

ndi woopa Yehova ndi chuma, ulemu ndi moyo.

5Mʼnjira za anthu oyipa muli minga ndi misampha,

koma amene amasala moyo wake adzazipewa zonsezo.

6Mwana muzimuphunzitsa njira yake,

ndipo akadzakalamba sadzachokamo.

7Wolemera amalamulira wosauka,

ndipo wokongola zinthu amakhala kapolo wa womukongozayo.

8Amene amafesa zoyipa amakolola mavuto,

ndipo ndodo yaukali wake idzathyoka.

9Amene ali ndi diso lachifundo adzadalitsika,

pakuti iye amagawana chakudya chake ndi anthu osauka.

10Chotsani munthu wonyoza, ndipo kukangana kudzatha;

mapokoso ndi zonyoza zidzaleka.

11Amene amakonda kukhala woyera mtima ndi kumayankhula mawu abwino,

adzakhala bwenzi la mfumu.

12Maso a Yehova amakhala pa anthu odziwa bwino zinthu,

koma Iye adzalepheretsa mawu a anthu osakhulupirika.

13Munthu waulesi amati,

“Kunjaku kuli mkango. Ine ndidzaphedwa mʼmisewu!”

14Pakamwa pa mkazi wachigololo pali ngati dzenje lozama;

amene Yehova wamukwiyira adzagwamo.

15Uchitsiru umakhala mu mtima mwa mwana,

koma ndodo yomulangira mwanayo idzachotsa uchitsiruwo.

16Amene amapondereza anthu osauka kuti awonjezere chuma chake,

ndiponso amene amapereka mphatso kwa anthu olemera onsewa adzasauka.

Malangizo a Anthu Anzeru

17Utchere khutu lako ndipo umvere mawu anzeru;

uyike mtima wako pa zimene ndikukuphunzitsa kuti udziwe.

18Zidzakhala zokondweretsa ngati uzisunga mu mtima mwako

ndi wokonzeka kuziyankhula.

19Ndakuphunzitsa zimenezi lero

koma makamaka uziopa Yehova.

20Kodi suja ndinakulembera malangizo makumi atatu

okuchenjeza ndi okupatsa nzeru,

21malangizo okudziwitsa zolungama

ndi zoona

ndi kuti ukawayankhe zoona amene akutumawo?

22Mʼmphawi usamubere chifukwa ndi osauka,

ndipo usawapondereze anthu osowa mʼbwalo la milandu,

23pakuti Yehova adzawateteza pa mlandu wawo

ndipo adzalanda moyo onse amene amawalanda iwo.

24Usapalane naye ubwenzi munthu wosachedwa kupsa mtima

ndipo usayanjane ndi munthu amene sachedwa kukwiya

25kuopa kuti iwe ungadzaphunzire njira zake

ndi kukodwa mu msampha.

26Usakhale munthu wopereka chikole

kapena kukhala mboni pa ngongole;

27ngati ulephera kupeza njira yolipirira

adzakulanda ngakhale bedi lako lomwe.

28Usasunthe mwala wamʼmalire akalekale

amene anayikidwa ndi makolo ako.

29Kodi ukumuona munthu waluso pa ntchito yake?

Iye adzatumikira mafumu;

sadzatumikira anthu wamba.