申命記 27 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

申命記 27:1-26

以巴路山上的律法

1摩西以色列眾長老吩咐民眾說:「你們要遵守我今天吩咐你們的一切誡命。 2你們渡過約旦河、進入你們的上帝耶和華應許給你們的土地那天,要豎立幾塊大石,塗上石灰。 3你們渡過約旦河、進入你們祖先的上帝耶和華應許要賜給你們的奶蜜之鄉後,要把這律法一字不漏地寫在大石上。 4你們渡過約旦河後,要照我今日的吩咐在以巴路山上豎立這些石頭,塗上石灰。 5要在那裡為你們的上帝耶和華築一座石壇,不要用鐵器鑿刻石頭。 6要用未鑿過的石頭為你們的上帝耶和華築一座壇,在上面獻燔祭給祂; 7又要獻上平安祭,在祂面前吃喝快樂。 8你們要把這律法一字不漏、清清楚楚地寫在那幾塊大石上。」

9摩西利未祭司對全體以色列人說:「以色列人啊,要肅靜聆聽!你們今天已成為你們上帝耶和華的子民。 10你們要聽從祂,遵守祂今天藉我吩咐你們的誡命和律例。」

違命必受咒詛

11那天,摩西吩咐民眾說: 12「你們渡過約旦河後,西緬利未猶大以薩迦約瑟便雅憫支派要站在基利心山上為民眾祝福; 13呂便迦得亞設西布倫拿弗他利支派要站在以巴路山上宣告咒詛。 14利未人要對所有以色列人高聲說,

15『凡雕刻或鑄造耶和華所憎惡的神像,並偷偷供奉的必受咒詛!』

全體民眾要回答說,『阿們!』

16『凡不尊敬父母的必受咒詛!』

全體民眾要回答說,『阿們!』

17『凡挪移鄰居界石的必受咒詛!』

全體民眾要回答說,『阿們!』

18『凡故意帶領盲人走錯路的必受咒詛!』

全體民眾要回答說,『阿們!』

19『不公正地對待寄居者和孤兒寡婦的必受咒詛!』

全體民眾要回答說,『阿們!』

20『凡與父親的妻妾亂倫,使父親蒙羞的必受咒詛!』

全體民眾要回答說,『阿們!』

21『凡與獸交合的必受咒詛!』

全體民眾要回答說,『阿們!』

22『凡與同父或同母姊妹亂倫的必受咒詛!』

全體民眾要回答說,『阿們!』

23『凡與岳母亂倫的必受咒詛!』

全體民眾要回答說,『阿們!』

24『凡暗殺鄰居的必受咒詛!』

全體民眾要回答說,『阿們!』

25『凡因收受賄賂而殺害無辜的必受咒詛!』

全體民眾要回答說,『阿們!』

26『凡不遵行這律法的必受咒詛!』

全體民眾要回答說,『阿們!』

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 27:1-26

Guwa Lansembe ku Phiri la Ebala

1Mose ndi akuluakulu a Israeli analamula anthu kuti, “Sungani malamulo onse amene ndikukupatsani lero lino. 2Mukawoloka mtsinje wa Yorodani kulowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, muyimiritse miyala ingapo ikuluikulu ndi kuyikulungiza. 3Mulembepo mawu onse a malamulo amenewa pamene muwoloka kulowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, dziko loyenda mkaka ndi uchi, monga momwe Yehova Mulungu wa makolo anu anakulonjezerani. 4Ndipo mukawoloka Yorodani muyimike miyala iyi pa Phiri la Ebala monga momwe ndikukulamulirani lero lino ndipo muyikulungize. 5Pamenepo mumange guwa lansembe la miyala la Yehova Mulungu wanu. Musagwiritse ntchito chida chilichonse chachitsulo pa miyalapo. 6Mumange guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu ndi miyala yakutchire ndi kuperekerapo nsembe yopsereza kwa Yehova Mulungu wanu. 7Muperekerepo nsembe zopereka za chiyanjano, muzidye ndi kukondwera pamaso pa Yehova Mulungu wanu. 8Ndipo pa miyalapo mudzalembepo mawu onse a malamulo ndi malemba akuluakulu.”

Matemberero Kuchokera ku Phiri la Ebala

9Kenaka Mose ndi ansembe, amene ndi Alevi anati kwa Aisraeli onse, “Khalani chete Aisraeli inu ndipo mumvetsere! Tsopano inu ndinu anthu a Yehova Mulungu wanu. 10Muzimvera Yehova Mulungu wanu ndi kutsata malamulo ake ndi malangizo ake omwe ndikukupatsani lero lino.”

11Tsiku lomwelo Mose analamula anthu kuti:

12Mukawoloka Yorodani, mafuko awa akayimirire pa Phiri la Gerizimu ndi kudalitsa anthu: Simeoni, Levi, Yuda, Isakara, Yosefe ndi Benjamini. 13Ndipo mafuko awa akayimirire pa Phiri la Ebala ndi kutchula matemberero: Rubeni, Gadi, Aseri, Zebuloni, Dani ndi Nafutali.

14Alevi adzayankhula mokweza kwa Aisraeli onse kuti:

15“Ndi wotembereredwa munthu amene asema chifanizo kapena kupanga fano, ndi kuchiyika mobisa, pakuti chimenechi ndi chinthu chodetsedwa pamaso pa Yehova, ntchito za manja a anthu.”

Pamenepo anthu onse adzati, “Ameni!”

16“Ndi wotembereredwa munthu amene sachitira ulemu abambo ake kapena amayi ake.”

Pamenepo anthu onse adzati, “Ameni!”

17“Ndi wotembereredwa munthu amene amasuntha mwala wa malire wa mnzake.”

Pamenepo anthu onse adzati, “Ameni!”

18“Ndi wotembereredwa munthu amene amasocheretsa munthu wosaona pa msewu.”

Pamenepo anthu onse adzati, “Ameni!”

19“Ndi wotembereredwa munthu amene sachitira chilungamo mlendo, ana amasiye kapena mkazi wamasiye.”

Pamenepo anthu onse adzati, “Ameni!”

20“Ndi wotembereredwa munthu amene agonana ndi mkazi wa abambo ake pakuti iye sachitira ulemu pogona pa abambo ake.”

Pamenepo anthu onse adzati, “Ameni!”

21“Ndi wotembereredwa munthu amene achita chigololo ndi nyama ya mtundu uli wonse.”

Pamenepo anthu onse adzati, “Ameni!”

22“Ndi wotembereredwa munthu amene agonana ndi mlongo wake, mwana wamkazi wa abambo ake kapena mwana wamkazi wa amayi ake.”

Pamenepo anthu onse adzati, “Ameni!”

23“Ndi wotembereredwa munthu amene agonana ndi apongozi ake.”

Pamenepo anthu onse adzati, “Ameni!”

24“Ndi wotembereredwa munthu amene apha mnzake mwachinsinsi.”

Pamenepo anthu onse adzati, “Ameni!”

25“Ndi wotembereredwa munthu amene alandira chiphuphu kuti aphe munthu wosalakwa.”

Pamenepo anthu onse adzati, “Ameni!”

26“Ndi wotembereredwa aliyense amene sachita kapena sasunga mawu a malamulo awa.”

Pamenepo anthu onse adzati, “Ameni!”