民數記 8 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

民數記 8:1-26

安置七盞燈

1耶和華對摩西說: 2「你告訴亞倫,安放燈的時候,七盞燈都要照向燈臺的前面。」 3亞倫就照耶和華對摩西的吩咐把燈放好,使燈照向前方。 4整座燈臺,從燈座到上面的花苞,都是照耶和華對摩西的吩咐用金子錘製而成的。

為利未人行潔淨與奉獻禮

5耶和華對摩西說: 6「你要把利未人從其他以色列人中分別出來,潔淨他們。 7要用以下的方法潔淨他們,把潔淨水灑在他們身上,叫他們用剃刀剃淨全身,洗淨衣服,這樣他們就潔淨了。 8然後叫他們帶來一頭公牛犢及作素祭的調了油的細麵粉,你要另獻一頭公牛犢作贖罪祭。 9你要招聚以色列全體會眾,將利未人帶到會幕前, 10帶到耶和華面前,會眾要按手在他們身上。 11亞倫要把他們獻給耶和華,作為以色列人獻的搖祭,使他們可以事奉耶和華。 12利未人要按手在那兩頭公牛的頭上,然後你要把一頭作為贖罪祭,一頭作為燔祭獻給耶和華,好為利未人贖罪。 13你要讓利未人站在亞倫父子們面前,把他們當作搖祭獻給耶和華。 14這樣,你就把利未人從其他以色列人中分別出來,使他們歸給我。 15利未人被潔淨、當作搖祭獻上以後,就可以進會幕司職, 16因為在以色列人中,他們完全屬於我,我揀選他們歸我所有,以代替以色列人所有的長子。 17以色列人所有的長子和頭生的牲畜都屬於我。我擊殺埃及人所有的長子和頭生的牲畜那天,已把以色列人所有的長子和頭生的牲畜都分別出來,使之聖潔,歸給我。 18我現在已揀選利未人代替以色列人所有的長子, 19把他們交給亞倫父子們,替以色列人在會幕中司職,為以色列人贖罪,免得以色列人因接近聖所而遭禍。」

20摩西亞倫以色列全體會眾就按照耶和華對摩西的吩咐把利未人獻上。 21利未人自潔、洗淨衣服後,亞倫把他們當作搖祭獻給耶和華,又為他們贖罪,使他們潔淨。 22之後,利未人便進入會幕,在亞倫父子們的監督下司職。以色列人照耶和華對摩西的吩咐奉獻了利未人。

23耶和華對摩西說: 24「二十五歲以上的利未人都要到會幕司職, 25五十歲時退休。 26退休之後,他們可以協助本族弟兄看守會幕,不用再司職。你要這樣給他們分派工作。」

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 8:1-26

Za Nyale

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Yankhula ndi Aaroni kuti pamene uyimika nyale zisanu ndi ziwiri, nyalezo ziziyaka kutsogolo kwa choyikapo nyale.”

3Aaroni anachitadi zomwezo. Anayimika nyale ndi kuziyangʼanitsa kumene kunali choyikapo nyale monga Yehova analamulira Mose. 4Choyikapo nyalecho chinapangidwa motere: chinasulidwa kuchokera ku golide, kuyambira pa tsinde pake mpaka ku maluwa ake. Choyikapo nyalecho chinapangidwa monga momwe Yehova anaonetsera Mose.

Za Kupatulidwa kwa Alevi

5Yehova anawuza Mose kuti, 6“Tenga Alevi pakati pa Aisraeli ndipo uwayeretse. 7Powayeretsa uchite izi: uwawaze madzi oyeretsa ndipo amete thupi lawo lonse ndi kuchapa zovala zawo kuti adziyeretse. 8Atenge ngʼombe yayimuna yayingʼono ndi chopereka cha chakudya cha ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Atengenso ngʼombe ina yayimuna, yayingʼono, ya chopereka chopepesera machimo. 9Ubwere nawo Aleviwo kutsogolo kwa tenti ya msonkhano ndipo usonkhanitse gulu la Aisraeli. 10Ubwere nawo pamaso pa Yehova, ndipo Aisraeli asanjike manja awo pa iwo. 11Aaroni apereke Alevi aja pamaso pa Yehova ngati chopereka choweyula kuchokera kwa Aisraeli kuti akhale okonzeka kugwira ntchito ya Yehova.

12“Alevi akatsiriza kusanjika manja awo pa mitu ya ngʼombe zazimuna, imodzi ikhale ya nsembe yopepesera machimo ndipo inayo ikhale ya nsembe yopsereza ya kwa Yehova, kupepesera machimo a Alevi. 13Uyimiritse Aleviwo pamaso pa Aaroni ndi ana ake aamuna ndipo uwapereke ngati nsembe yoweyula kwa Yehova. 14Pochita zimenezi mudzapatula Alevi pakati pa Aisraeli ndipo Aleviwo adzakhala anga.

15“Utatha kuyeretsa ndi kupereka Aleviwo monga nsembe yoweyula, apite kukagwira ntchito yawo ku tenti ya msonkhano. 16Iwo ndiwo Aisraeli amene aperekedwa kwathunthu kwa Ine. Ndawatenga kuti akhale anga mʼmalo mwa mwana wamwamuna aliyense woyamba kubadwa wa Mwisraeli aliyense wamkazi. 17Mwana aliyense wamwamuna woyamba kubadwa mu Israeli, kaya wa munthu kapena wa ziweto, ndi wanga. Pamene ndinakantha ana oyamba kubadwa ku Igupto, ndinawapatulira kwa Ine mwini. 18Ndipo ndatenga Alevi mʼmalo mwa ana aamuna onse oyamba kubadwa mu Israeli. 19Mwa Aisraeli onse, ndapereka Alevi kuti akhale mphatso kwa Aaroni ndi ana ake aamuna kugwira ntchito ya ku tenti ya msonkhano mʼmalo mwa Aisraeli onse kuti azikapereka nsembe yopepesera machimo, kuti mliri usadzaphe Aisraeli pamene ayandikira ku malo wopatulika.”

20Mose, Aaroni pamodzi ndi gulu lonse la Israeli anachita kwa Alevi monga momwe Yehova analamulira Mose. 21Alevi anadziyeretsa ndi kuchapa zovala zawo. Kenaka Aaroni anawapereka ngati nsembe yoweyula pamaso pa Yehova ndi kuchita nsembe yopepesera machimo yowayeretsa. 22Zitatha zimenezi, Alevi anapita kukagwira ntchito yawo ku tenti ya msonkhano motsogozedwa ndi Aaroni ndi ana ake aamuna. Anachita kwa Alevi monga momwe Yehova analamulira Mose.

23Yehova anawuza Mose kuti, 24“Ntchito za Alevi ndi izi: Amuna a zaka 24 kapena kuposera pamenepa ndiye azibwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano. 25Koma akakwana zaka makumi asanu, apume pa ntchito yawo ya tsiku ndi tsiku ndi kulekeratu kugwira ntchitoyo. 26Atha kuthandiza abale awo kugwira ntchito za ku tenti ya msonkhano, koma iwowo asamagwire ntchitoyo. Mmenemu ndimo ugawire ntchito yomwe azigwira Alevi.”