民數記 4 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

民數記 4:1-49

哥轄子孫的職責

1耶和華對摩西亞倫說: 2「你要按宗族和家系統計利未人中哥轄子孫的人數, 3登記三十歲到五十歲、可在會幕司職的男子。 4他們在會幕裡管理至聖之物。

5「拔營出發的時候,亞倫父子們要進會幕解下聖所和至聖所之間的幔子,用它遮蓋約櫃, 6再在上面依次蓋上海狗皮和純藍色的布,然後穿上抬約櫃的橫杠。

7「要在擺放供餅的桌子上鋪一塊藍布,把盤、碟、杯和獻酒用的瓶子擺在上面。桌上要有供餅。 8這些東西上面要蓋朱紅色的布,再蓋上海狗皮,然後穿上抬桌子的橫杠。

9「要用藍布把燈臺、燈盞、蠟剪、蠟盤和盛油的器皿全遮蓋起來, 10再在上面蓋上海狗皮,然後放在抬架上。

11「金香壇上面要蓋藍色布,再蓋上海狗皮,穿上抬金香壇的橫杠。

12「聖所裡面一切器皿都要用藍色布包好,蓋上海狗皮,放在抬架上。

13「要清除祭壇上的灰燼,鋪上紫色布, 14然後把火鼎、肉叉、鏟、碗等祭壇的器具放在上面,再蓋上海狗皮,穿上抬祭壇的橫杠。

15「拔營出發時,哥轄的子孫要等到亞倫父子們把聖所和聖所的器具都蓋好後,才可以來抬。他們負責抬這些會幕的器具,但不可觸摸這些聖物,免得死亡。 16亞倫祭司的兒子以利亞撒負責管理整個聖幕及裡面的燈油、香料、素祭、膏油等一切物品。」

17耶和華對摩西亞倫說: 18「不要讓哥轄宗族在利未人中滅絕。 19他們走近至聖之物以前,亞倫父子們要先進去指派他們做什麼、抬什麼,以免他們死亡。 20他們不可進去看聖物,一刻都不可,免得死亡。」

革順子孫的職責

21耶和華對摩西說: 22「你要按宗族和家系統計革順子孫的人數, 23登記三十歲到五十歲、可在會幕司職的男子。 24以下是他們負責的事務。

25「他們要抬聖幕的幔子、會幕、會幕頂蓋、頂蓋上的海狗皮、會幕門簾、 26圍繞聖幕和祭壇的院子的帷幔、院門門簾、繩索等器具,還負責其他相關事務。 27你們要把任務分配給革順的子孫,他們要遵照亞倫父子們的吩咐司職。 28這是革順宗族的人在會幕裡的職責,他們要按祭司亞倫的兒子以他瑪的吩咐司職。

米拉利子孫的職責

29「你要按宗族和家系統計米拉利子孫的人數, 30登記三十歲到五十歲、可在會幕司職的男子。 31他們在會幕裡負責抬聖幕的木板、橫閂、柱子、帶凹槽的底座, 32院子四周的柱子及其帶凹槽的底座、橛子、繩索和其他相關器具。你們要把當抬的物件一一指派給他們。 33這是米拉利宗族的人在會幕的職責,由祭司亞倫的兒子以他瑪監督。」

34於是,摩西亞倫和會眾的首領按宗族和家系統計哥轄的子孫, 35登記了三十歲到五十歲、可在會幕司職的男子, 36共兩千七百五十人。 37這是哥轄宗族在會幕司職的人數,是摩西亞倫照耶和華的吩咐統計的。

38-40按宗族和家系統計,革順的子孫中三十歲到五十歲、可在會幕司職的共兩千六百三十人。 41這是革順宗族在會幕司職的人數,是摩西亞倫照耶和華的吩咐統計的。

42-44按宗族和家系統計,米拉利的子孫中三十歲到五十歲、可在會幕司職的共三千二百人。 45這是米拉利宗族的人數,是摩西亞倫照耶和華的吩咐統計的。

46摩西亞倫以色列人的首領按宗族和家系統計了利未人的人數, 47-48三十歲到五十歲可司職、搬運會幕器具的利未人共八千五百八十人。 49照耶和華對摩西的吩咐,每個人都被統計在內,都有指定的職責和當抬的器具。這樣,照耶和華對摩西的吩咐,人口統計完畢。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 4:1-49

Akohati

1Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni: 2“Werengani Akohati omwe ndi gawo limodzi la Alevi monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo. 3Werengani amuna onse amene ali ndi zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu amene amabwera kudzagwira ntchito mu tenti ya msonkhano.

4“Ntchito ya Akohati mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kusamalira zinthu zopatulika kwambiri. 5Pamene anthu akusamuka pa msasa, Aaroni ndi ana ake aamuna azilowa mu tenti ndi kuchotsa chinsalu chotchingira ndi kuphimba nacho bokosi la umboni. 6Ndipo azikuta bokosilo ndi zikopa za akatumbu ndi kuyala pamwamba pake nsalu ya mtundu wa thambo ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.

7“Pa tebulo pamene pamakhala buledi wa ansembe aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo, ndipo aziyikapo mbale, mabeseni, zipande ndi mitsuko yoperekera nsembe yachakumwa. Aziyikaponso buledi wokhala pamenepo nthawi zonse. 8Tsono pamwamba pa izi aziyalapo nsalu yofiira, ndi kuzikuta mʼzikopa za akatumbu ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.

9“Azitenga nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira choyikapo nyale, pamodzi ndi nyale zake, zopanira zake, zotengera zake ndi mitsuko yonse yosungiramo mafuta. 10Kenaka achikulunge pamodzi ndi zipangizo zake zonse mʼzikopa za akatumbu ndi kuchiyika pa chonyamulira chake.

11“Pamwamba pa guwa la golide aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira ndi zikopa za akatumbu ndi kuyika mʼmalo mwake mitengo yonyamulira.

12“Azitenga zipangizo zonse zogwiritsira ntchito ku malo wopatulika, azizikulunga mʼnsalu ya mtundu wa thambo, azizikuta ndi zikopa za akatumbu ndi kuziyika pa zonyamulira zake.

13“Azichotsa phulusa la pa guwa lansembe lamkuwa ndi kuyalapo nsalu yapepo pamwamba pake. 14Kenaka aziyikapo zipangizo zonse zogwiritsira ntchito potumikira pa guwa, kuphatikizapo miphika yowotchera nyama, mafoloko otengera nyama, zowolera phulusa ndi mbale zowazira magazi pa guwa lansembe ndipo pamwamba pake aziyalapo zikopa za akatumbu ndi kuziyika mʼzonyamulira zake.

15“Aaroni ndi ana ake aamuna akamaliza kukutira ziwiya za ku malo wopatulika ndi zipangizo zopatulika zonse, ndipo akakonzeka kusamuka pamalopo, Akohati abwere kudzazinyamula koma asagwire zinthu zopatulikazo. Akatero adzafa. Izi ndizo zinthu zimene Akohati ayenera kunyamula mu tenti ya msonkhano.

16“Eliezara mwana wa Aaroni, wansembe, aziyangʼanira mafuta a nyale, ndi lubani wa nsembe zofukiza, nsembe yaufa yoperekedwa nthawi zonse ndi mafuta odzozera. Aziyangʼaniranso chihema ndi zonse zili mʼmenemo, kuphatikizapo zida ndi ziwiya zonse zopatulika.”

17Yehova anawuzanso Mose ndi Aaroni kuti, 18“Onetsetsani kuti mabanja a fuko la Kohati asachotsedwe kwa Alevi. 19Koma muziwachitira izi kuti asafe, akhalebe ndi moyo pamene ayandikira zinthu za ku malo wopatulika kwambiri: Aaroni ndi ana ake aamuna azipita ku malo wopatulika ndi kumamupatsa munthu aliyense ntchito yake ndi zimene ayenera kunyamula. 20Koma Akohati asalowe kukaona zinthu zopatulika, ngakhale kanthawi pangʼono, chifukwa akatero adzafa.”

Ageresoni

21Yehova anawuza Mose kuti, 22“Werenganso Ageresoni monga mwa mabanja ndi mafuko awo. 23Uwerenge amuna onse a zaka makumi atatu mpaka a zaka makumi asanu zakubadwa amene amabwera kudzatumikira ku tenti ya msonkhano.

24“Ntchito ya mafuko a Ageresoni pamene akugwira ntchito ndi kunyamula katundu ndi iyi: 25Azinyamula makatani a ku chihema, tenti ya msonkhano, zokutira zake ndi zokutira kunja za zikopa za akatumbu, makatani a pa khomo la ku tenti ya msonkhano, 26makatani wotchingira bwalo lozungulira chihema ndi guwa, katani ya pa khomo, zingwe ndi zida zonse zimene zimagwiritsidwa ntchito mʼchihema. Ageresoni azichita zonse zofunika kuchitika ndi zinthu zimenezi. 27Ntchito yawo yonse, kaya kunyamula kapena kugwira ntchito zina, achite Ageresoni motsogozedwa ndi Aaroni ndi ana ake aamuna. Uwagawire ntchito zonse zimene akuyenera kugwira. 28Iyi ndiye ntchito ya fuko la Ageresoni ku tenti ya msonkhano. Ntchito zawo zichitike motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.

Amerari

29“Werenga Amerari monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo. 30Werenga amuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu zakubadwa amene akatumikire mu tenti ya msonkhano. 31Ntchito yawo pamene azikatumikira mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kunyamula matabwa a chihema, mitanda, mizati ndi matsinde, 32ndiponso mizati yozungulira bwalo ndi matsinde ake, zikhomo za chihema, zingwe ndi zipangizo zake zonse ndiponso zonse zokhudzana ndi ntchito yake. Uwuze munthu aliyense chomwe ayenera kuchita. 33Iyi ndiyo ntchito ya mafuko a Amerari pamene akugwira ntchito ku tenti ya msonkhano motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.”

Chiwerengero cha Fuko la Levi

34Mose, Aaroni ndi atsogoleri a magulu a anthu anawerenga Akohati monga mwa mafuko ndi mabanja awo. 35Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano, 36atawawerenga mwa mafuko awo, anali 2,750. 37Ichi chinali chiwerengero cha mafuko a Akohati onse omwe ankatumikira mu tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.

38Ageresoni anawerengedwanso monga mwa mafuko ndi mabanja awo. 39Amuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano, 40atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 2,630. 41Ichi chinali chiwerengero cha Ageresoni mwa mabanja awo amene ankatumikira ku tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.

42Amerari anawawerenga monga mwa mafuko ndi mabanja awo. 43Amuna onse kuyambira zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzatumikira ntchito mu tenti ya msonkhano, 44atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 3,200. 45Ichi ndicho chinali chiwerengero cha mabanja a Amerari. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga momwe Yehova anawalamulira kudzera mwa Mose.

46Kotero Mose, Aaroni ndi atsogoleri a Israeli anawerenga Alevi onse monga mwa mafuko ndi mabanja awo. 47Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu omwe anabwera kudzagwira ntchito yonyamula zinthu ku tenti ya msonkhano 48analipo 8,580. 49Aliyense anamupatsa ntchito ndi kumuwuza choti anyamule monga mwa lamulo la Yehova kudzera mwa Mose.

Anawawerenga chomwechi potsata zimene Yehova analamula Mose.