歷代志上 5 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

歷代志上 5:1-26

呂便的後裔

1以色列的長子原是呂便,但因為他玷污了父親的床5·1 指跟父親的妾通姦一事,參見創世記35·22,他長子的名分就給了他弟弟約瑟的後代。因此,按家譜他不是長子。 2猶大雖然在眾弟兄中最強大,君王也是出自他的後裔,長子的名分卻屬於約瑟3以色列長子呂便的兒子是哈諾法路希斯倫迦米4約珥的兒子是示瑪雅示瑪雅的兒子是歌革歌革的兒子是示每5示每的兒子是米迦米迦的兒子是利·亞雅利·亞雅的兒子是巴力6巴力的兒子是備·拉備·拉呂便支派的首領,被亞述提革拉·毗尼色擄去。 7按家譜記載,他做族長的親族是耶利撒迦利雅比拉8比拉亞撒的兒子,亞撒示瑪的兒子,示瑪約珥的兒子。約珥住在亞羅珥尼波巴力·免一帶。 9他們的牲畜在基列繁殖眾多,便又向東遷移到幼發拉底河西邊的曠野。 10掃羅執政期間,呂便人與夏甲人交戰,打敗了夏甲人,佔領了基列東邊的整片土地。

迦得的後裔

11迦得的後代住在毗鄰呂便支派的巴珊,向東遠至撒迦12巴珊做首領的有族長約珥、副族長沙番以及雅乃沙法13他們同族的弟兄有米迦勒米書蘭示巴約賴雅幹細亞希伯,共七人。 14這些都是亞比孩的兒子。亞比孩戶利的兒子,戶利耶羅亞的兒子,耶羅亞基列的兒子,基列米迦勒的兒子,米迦勒耶示篩的兒子,耶示篩耶哈多的兒子,耶哈多布斯的兒子。 15古尼的孫子、押比碟的兒子亞希是他們家族的族長。 16他們住在基列巴珊巴珊附近的鄉村以及沙崙所有的草原,直到四圍的邊界地帶。 17這些人是在猶大約坦以色列耶羅波安執政期間被記錄在族譜裡的。

18呂便支派、迦得支派和瑪拿西半個支派中善用盾牌、刀劍、弓箭、能征善戰的勇士共有四萬四千七百六十人。 19他們與夏甲人、伊突人、拿非施人和挪答人打仗, 20擊敗了夏甲人及其盟軍,因為他們信靠上帝,在作戰的時候向上帝求助,上帝應允了他們的祈求。 21他們從敵人那裡擄走了五萬隻駱駝、二十五萬隻羊、兩千頭驢和十萬人口。 22敵人傷亡慘重,因為他們有上帝的幫助。他們佔據敵人的土地,一直到被擄的時候。

瑪拿西的半個支派

23瑪拿西半個支派的人住在從巴珊巴力·黑們示尼珥黑門山一帶。 24他們的族長以弗以示以列亞斯列耶利米何達威雅雅疊都是英勇的戰士,是著名的人物和各家族的首領。

25可是,他們卻背棄他們祖先的上帝,與當地居民的神明苟合。上帝曾在他們面前毀滅那些居民。 26因此,以色列的上帝驅使亞述普勒,即提革拉·毗尼色,把呂便人、迦得人、瑪拿西半個支派的人擄到哈臘哈博哈拉歌散河邊,他們至今還在那裡。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mbiri 5:1-26

Fuko la Rubeni

1Ana a Rubeni mwana woyamba wa Israeli (iye anali woyamba kubadwa, koma atagona ndi mkazi wamngʼono wa abambo ake, ulemu wake wokhala mwana woyamba unaperekedwa kwa ana a Yosefe. Kotero iye sanalembedwe pa mndandanda wa mayina ngati mwana woyamba kubadwa, 2ndipo ngakhalenso Yuda anali wamphamvu kwambiri pakati pa abale ake, ndi kuti wolamulira anachokera mwa iye, ulemu wa mwana woyamba kubadwa unaperekedwa kwa Yosefe) 3ana a Rubeni mwana woyamba wa Israeli ndi awa:

Hanoki, Palu, Hezironi, ndi Karimi.

4Ana a Yoweli anali awa:

Semaya, Gogi,

Simei, 5Mika,

Reaya, Baala,

6ndiponso Beeri, amene Tigilati-Pileseri mfumu ya Asuri anamugwira ukapolo. Mtsogoleri wa fuko la Rubeni anali Beeri.

7Abale awo mwa mabanja awo, potsata mndandanda wa mʼbado wawo, ndi awa:

Yeiyeli, mtsogoleri, Zekariya, 8ndiponso Bela mwana wa Azazi, mwana wa Sema, mwana wa Yoweli. Iwo ankakhala ku Aroeri mpaka ku Nebo ndi Baala-Meoni. 9Iwo anakhala cha kummawa mpaka kukafika polowera mʼchipululu cha mbali ina ya Mtsinje wa Yufurate, chifukwa ziweto zawo zinaswana kwambiri mʼdziko la Giliyadi.

10Pa nthawi ya Sauli anachita nkhondo ndi Ahagiri ndi kuwagonjetsa. Tsono iwo anakhala mʼmatenti a Ahagiri ku dera lonse la kummawa kwa Giliyadi.

Fuko la Gadi

11Anthu a fuko la Gadi anakhala moyandikana ndi fuko la Rubeni ku Basani mpaka ku Saleka:

12Mtsogoleri wawo ku Basani anali Yoweli, wachiwiri anali Safamu, kenaka Yanayi ndi Safati.

13Abale awo mwa mabanja awo anali awa:

Mikayeli, Mesulamu, Seba, Yorayi, Yakani, Ziya ndi Eberi, onse ali asanu ndi awiri.

14Amenewa ndiwo anali ana a Abihaili, mwana wa Huri, mwana wa Yarowa, mwana wa Giliyadi, mwana wa Mikayeli, mwana wa Yesisayi, mwana wa Yahido, mwana wa Buzi.

15Ahi mwana wa Abdieli, mwana wa Guni, anali mtsogoleri wa banja la makolo awo.

16Fuko la Gadi linakhala ku Giliyadi, ku Basani ndi midzi yozugulira, madera onse a msipu a ku Saroni mpaka kumene amalekezera.

17Mayina onsewa analembedwa potsata mndandanda wa mibado yawo pa nthawi ya ulamuliro wa Yotamu mfumu ya Yuda ndi Yeroboamu mfumu ya Israeli.

18Mafuko a Rubeni, Gadi ndi theka la Manase, anali ndi anthu 44, 760 okonzeka kulowa usilikali; anthu amatupi amphamvu, amene amatha kugwiritsa ntchito chishango ndi lupanga, amene amatha kugwiritsa ntchito uta, amene anaphunzitsidwa kumenya nkhondo. 19Iwo anachita nkhondo ndi Ahagiri, Yeturi, Nafisi ndi Nodabu. 20Iwowo anathandizidwa polimbana nawo ndipo Mulungu anapereka Ahagiri mʼmanja mwawo; popeza iwo anafuwulira kwa Mulungu pa nkhondopo. Iye anayankha mapemphero awo chifukwa anamudalira. 21Choncho iwo analanda ziweto za Ahagiri: ngamira 50,000, nkhosa ndi mbuzi 250,000 ndi abulu 2,000. Ndiponso anagwira akapolo 100,000, 22enanso ambiri anaphedwa, chifukwa nkhondoyo inali ya Mulungu. Ndipo iwo anakhala mʼdzikomo mpaka pa nthawi ya ukapolo.

Theka la Fuko la Manase

23Theka la fuko la Manase linkakhala ku dziko la kummawa kuyambira ku Basani mpaka ku Baala-Herimoni, kumene ndi ku Seniri (Phiri la Herimoni) ndipo anthuwo anali ochuluka kwambiri.

24Atsogoleri a mabanja awo anali awa: Eferi, Isi, Elieli, Azirieli, Yeremiya, Hodaviya ndi Yahidieli. Iwo anali asilikali olimba mtima, anthu otchuka, ndiponso atsogoleri a mabanja awo. 25Koma iwo anali osakhulupirika kwa Mulungu wa makolo awo ndipo anadzipereka okha kwa milungu ya anthu okhala mʼdzikomo amene Mulungu anawawononga pamene iwowo ankafika. 26Kotero Mulungu wa Israeli anayika mkwiyo mwa Puli mfumu ya Asuri (ameneyu ndi Tigilati-Pileseri mfumu ya Asuri) amene anatenga fuko la Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase kupita nawo ku ukapolo. Iye anapita nawo ku Hala, Habori, Hara ndi ku mtsinje wa Gozani, kumene ali mpaka lero lino.