歷代志上 18 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

歷代志上 18:1-17

大衛的勝利

1後來,大衛打敗並征服了非利士人,奪取了迦特及其周圍的村莊。 2他又打敗了摩押人,使他們稱臣、進貢。 3瑣巴哈大底謝出來要鞏固他在幼發拉底河一帶的權勢,大衛打敗了他,一直攻到哈馬4俘獲一千輛戰車、七千騎兵、兩萬步兵,砍斷拉戰車的馬匹的蹄筋,只留下夠拉一百輛戰車的馬匹。 5大馬士革亞蘭人前來支援瑣巴哈大底謝大衛殺了他們兩萬二千人, 6還派軍駐守亞蘭國的大馬士革亞蘭人臣服大衛,向他進貢。耶和華使大衛無往而不勝。 7大衛奪走哈大底謝侍從的金盾牌,帶回耶路撒冷8又從哈大底謝統治的提巴兩座城中奪走大量的銅。後來所羅門用這些銅製造銅海、銅柱及各種銅器。

9哈馬陀烏聽說大衛打敗瑣巴哈大底謝全軍, 10就派兒子哈多蘭帶著許多金銀銅器去朝見大衛王,向他請安,祝賀他打敗了哈大底謝。因為陀烏常常和哈大底謝交戰。 11於是,大衛把這些器皿和他從以東摩押亞捫非利士亞瑪力各國奪來的金銀都分別出來,奉獻給耶和華。

12洗魯雅的兒子亞比篩在鹽谷擊殺了一萬八千名以東人。 13大衛以東駐兵,以東人都臣服他。耶和華使他無往而不勝。

14大衛在全以色列秉公行義,治理百姓。 15那時,洗魯雅的兒子約押做元帥,亞希律的兒子約沙法做史官, 16亞希突的兒子撒督亞比亞他的兒子亞希米勒做祭司長,沙威沙做書記, 17耶何耶大的兒子比拿雅統管基利提人和比利提人。大衛王的眾子都在他左右做首領。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mbiri 18:1-17

Nkhondo za Davide ndi Kupambana Kwake

1Patapita nthawi, Davide anagonjetsa Afilisti ndipo anakhala pansi pa ulamuliro wake. Iye analanda Gati ndi midzi yake yozungulira mʼmanja mwa Afilistiwo.

2Davide anagonjetsanso Amowabu, nakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho kwa iye.

3Komanso Davide anagonjetsa Hadadezeri mfumu ya Zoba, mpaka ku Hamati, pamene anapita kukakhazikitsa ulamuliro wake mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate. 4Davide analanda magaleta 1,000, anthu okwera magaleta 7,000 pamodzi ndi asilikali oyenda pansi 20,000. Iye anadula mitsempha ya akavalo onse okoka magaleta, koma anasiyapo akavalo 100 okha.

5Aramu wa ku Damasiko atabwera kudzathandiza Hadadezeri mfumu ya ku Zoba, Davide anakantha asilikali 22,000. 6Iye anakhazikitsa maboma mu ufumu wa Aramu wa ku Damasiko, ndipo Aaramu anakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho. Yehova ankamupatsa chipambano Davide kulikonse kumene ankapita.

7Davide anatenga zishango zagolide zimene ankanyamula akuluakulu ankhondo a Hadadezeri ndi kubwera nazo ku Yerusalemu. 8Kuchokera ku Teba ndi Kuni, mizinda ya Hadadezeri, Davide anatengako mkuwa wambiri umene Solomoni anapangira chimbiya, zipilala ndi zida zosiyanasiyana zamkuwa.

9Tou, mfumu ya Hamati atamva kuti Davide wagonjetsa gulu lonse lankhondo la Hadadezeri mfumu ya Zoba, 10anatumiza mwana wake Hadoramu kwa mfumu Davide kukamulonjera ndi kukamuyamikira chifukwa cha kupambana kwake pa nkhondo yake ndi Hadadezeriyo, amene analinso pa nkhondo ndi Tou. Hadoramu anabweretsa ziwiya zosiyanasiyana zagolide, zasiliva ndi zamkuwa.

11Mfumu Davide inapereka zinthu zimenezi kwa Yehova, monga anachitira ndi siliva ndi golide zochokera ku mayiko ena onse monga Edomu ndi Mowabu, Aamoni ndi Afilisti, ndi Aamaleki.

12Abisai mwana wa Zeruya anakantha Aedomu 18,000 mu Chigwa cha Mchere. 13Iye anayika maboma ku Edomu, ndipo Aedomu onse anakhala pansi pa Davide. Yehova ankapambanitsa Davide kulikonse kumene ankapita.

Akuluakulu a Davide

14Davide analamulira dziko lonse la Israeli ndipo ankachita zonse mwachilungamo ndi molondola pamaso pa anthu ake onse. 15Yowabu, mwana wa Zeruya anali mkulu wa ankhondo; Yehosafati mwana wa Ahiludi anali mlembi wa zochitika; 16Zadoki, mwana wa Ahitubi ndi Ahimeleki mwana wa Abiatara anali ansembe; Savisa anali mlembi; 17Benaya mwana wa Yehoyada anali mtsogoleri wa Akereti ndi Apeleti, ndipo ana a Davide anali alangizi a mfumu.