撒母耳記下 3 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

撒母耳記下 3:1-39

押尼珥之死

1掃羅大衛兩家長期爭戰,大衛家的勢力越來越強,掃羅家卻日益衰微。

2大衛希伯崙生的兒子有耶斯列亞希暖所生的長子暗嫩3迦密拿八的遺孀亞比該所生的次子基利押基述達買的女兒瑪迦所生的三子押沙龍4哈及所生的四子亞多尼雅亞比她所生的五子示法提雅5大衛的妻子以格拉所生的六子以特念大衛的這些兒子都是在希伯崙生的。

6掃羅大衛兩家爭戰期間,押尼珥掃羅家權勢日增。 7他跟掃羅的一個妃嬪、艾押的女兒利斯巴通姦,伊施波設問他:「你為什麼跟我父親的妃嬪一起睡覺呢?」 8押尼珥聽了非常憤怒,說:「難道我是猶大的走狗嗎?我這樣厚待你父親掃羅家和他的親人朋友,沒有把你交給大衛,今天你竟為了一個女人來責備我! 9-10倘若我不照著耶和華應許大衛的誓言把掃羅的江山奪過來交給大衛,讓他統治全以色列猶大,從別示巴,願耶和華重重地懲罰我!」

11伊施波設一句話也不敢答,因為他害怕押尼珥

12押尼珥派使者送信給大衛,說:「這個國家難道不是你的嗎?如果你與我立約,我必幫助你統一以色列。」 13大衛回答說:「好,但你一定要把掃羅的女兒米甲帶來才能見我。」 14於是,大衛派使者去見掃羅的兒子伊施波設說:「請把我的妻子米甲送回來,因為她是我用一百個非利士人的包皮作聘禮娶來的。」 15伊施波設就派人把米甲從她丈夫——拉億的兒子帕鐵那裡接回來。 16帕鐵一路跟著米甲,邊走邊哭,一直到巴戶琳押尼珥對他說:「你回去吧!」他就回去了。

17押尼珥以色列的長老商量說:「你們以前一直都希望大衛做你們的王, 18現在是時候了,因為耶和華曾說要藉著祂僕人大衛的手,從非利士人和其他敵人手中拯救祂的以色列子民。」 19押尼珥也跟便雅憫人商談,然後到希伯崙以色列人和便雅憫人的願望告訴大衛20當時,他帶了二十個人前往希伯崙大衛大衛就設宴款待他們。 21押尼珥大衛說:「我要為我主我王招聚所有的以色列人,跟你立約,你便可以如願以償,統治全以色列。」於是大衛為他送行,他就平安地回去了。

22大衛押尼珥離開後不久,約押就率領大衛的軍隊帶著許多戰利品凱旋而歸。 23約押率領全軍回來後,有人告訴他:「尼珥的兒子押尼珥剛才來朝見王,王送他平安地離去了。」 24約押聽後,就去見王,說:「你這做的是什麼事?押尼珥來見你,你為什麼放他走呢? 25你要知道,尼珥的兒子押尼珥想來騙你,探聽你的虛實。」

26約押大衛那裡出來,派人去追押尼珥,他們在西拉井追上了他,把他帶了回來。大衛對這件事一無所知。 27押尼珥回到希伯崙的時候,約押就把他帶到城門的甕洞,裝作與他密談,乘機用短劍刺入他的肚子,把他殺死了,為他兄弟亞撒黑報了仇。 28大衛聽到消息就說:「耶和華作證,我和我的人民永遠跟尼珥的兒子押尼珥的死無關。 29約押和他全家要承擔這罪,願他的後代永遠有長瘡的、患皮膚病的、拄拐杖的、被刀劍所殺的或挨餓的。」 30約押和他兄弟亞比篩之所以殺押尼珥,是因為押尼珥基遍殺了他們的兄弟亞撒黑

31大衛約押和部下說:「你們要撕裂衣服,腰束麻布,在押尼珥棺前哭喪!」大衛王也跟在棺後送葬。 32他們就把押尼珥葬在希伯崙大衛王和眾人在墓旁大哭一場。 33大衛王哀悼押尼珥,說:

押尼珥啊!

你怎能死得糊里糊塗3·33 糊里糊塗」希伯來文是「像愚笨人」。呢?

34你的手沒有被捆,

你的腳沒有被鎖,

你是死在陰險小人的手裡啊!」

於是眾人都為押尼珥哀哭。 35大衛整天沒有進食,眾人來勸他吃一點東西,但他起誓說:「我若在日落以前吃任何東西,願上帝重重地懲罰我!」 36眾人聽見了,都很喜悅,王做的每一件事都令他們喜悅。 37那天全國的人都看出尼珥的兒子押尼珥的死與大衛無關。 38大衛王對他的隨從說:「你們難道不知道今天以色列損失了一位偉大的將領嗎? 39今天我雖然是耶和華所膏立的王,但仍勢單力薄,無法對付洗魯雅的兩個兒子,願耶和華報應他們的惡行。」

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Samueli 3:1-39

1Nkhondo ya pakati pa banja la Sauli ndi banja la Davide inachitika nthawi yayitali. Mphamvu za Davide zinkakulirakulirabe, pamene banja la Sauli mphamvu zake zimapita zicheperachepera.

2Ana aamuna a Davide amene anabadwira ku Hebroni anali awa: Woyamba anali Amnoni, amayi ake anali Ahinoamu wa ku Yezireeli.

3Mwana wachiwiri anali Kileabu, amayi ake anali Abigayeli mkazi wamasiye wa Nabala wa ku Karimeli.

Wachitatu anali Abisalomu, amayi ake anali Maaka mwana wa Talimai mfumu ya Gesuri;

4wachinayi anali Adoniya, amayi ake anali Hagiti;

wachisanu, Sefatiya amayi ake anali Abitali;

5ndipo wachisanu ndi chimodzi anali Itireamu, amayi ake anali Egila, mkazi wa Davide.

Ana awa a Davide anabadwira ku Hebroni.

Abineri Agwirizana ndi Davide

6Pamene kunali nkhondo pakati pa banja la Sauli ndi banja la Davide, Abineri anayamba kudzipatsa yekha mphamvu pakati pa banja la Sauli. 7Sauli anali ndi mzikazi dzina lake Rizipa mwana wa Ayiwa. Ndipo Isiboseti anati kwa Abineri, “Nʼchifukwa chiyani unagona ndi mzikazi wa abambo anga?”

8Abineri anakwiya kwambiri chifukwa cha zimene Isi-Boseti ananena ndipo anamuyankha kuti “Kodi ukuyesa ndine mutu wagalu umene ali mbali ya Ayuda? Lero lino ndine wokhulupirika ku nyumba ya abambo ako, Sauli ndi banja lake ndi anzake. Ine sindinakupereke kwa Davide, koma tsopano ukundinena pa cholakwa chimene ndachita pa mkazi uyu! 9Mulungu andilange ine Abineri, andilange kwambiri, ngati sindichitira Davide zimene Yehova anamulonjeza iye mwa lumbiro. 10Ndidzachotsa ufumu ku nyumba ya Sauli ndi kukhazikitsa ufumu wa Davide pa Aisraeli onse ndi Yuda kuchokera ku Dani mpaka ku Beeriseba.” 11Isiboseti sanayerekezenso kunena mawu ena kwa Abineri, chifukwa ankamuopa.

12Kenaka Abineri anatuma amithenga kwa Davide kukanena kuti, “Kodi dzikoli ndi la yani? Uchite mgwirizano ndi ine ndipo ndidzakuthandiza kuti Aisraeli onse azikutsatira.”

13Davide anati, “Chabwino. Ine ndichita mgwirizano ndi iwe. Koma ndikukupempha chinthu chimodzi: Usabwere pamaso panga pokhapokha utabweretsa Mikala mwana wamkazi wa Sauli, ukamabwera kudzandiona.” 14Ndipo Davide anatuma amithenga kwa Isi-Boseti mwana wa Sauli, kumulamula kuti, “Patse mkazi wanga Mikala, amene ndinamukwatira ndi makungu 100 a msonga za mavalo a Afilisti.”

15Kotero Isi-Boseti analamulira ndipo anakamutenga kwa mwamuna wake Palitieli mwana wa Laisi. 16Koma mwamuna wake anapita naye akulira pambuyo pake njira yonse mpaka ku Bahurimu. Kenaka Abineri anati kwa iye, “Bwerera kwanu!” Ndipo anabwerera kwawo.

17Abineri anakambirana ndi akuluakulu a Israeli ndipo anati, “Kwa kanthawi mwakhala mukufuna kulonga Davide kuti akhale mfumu yanu. 18Tsopano chitani zimenezo! Pakuti Yehova analonjeza Davide kuti, ‘Kudzera mwa mtumiki wanga Davide ndidzapulumutsa anthu anga Aisraeli mʼdzanja la Afilisti ndi kuwachotsa mʼmanja mwa adani awo.’ ”

19Abineri anayankhulanso nawo yekha anthu a fuko la Benjamini. Kenaka anapita ku Hebroni kukamuwuza Davide zonse zimene Aisraeli ndi fuko lonse la Benjamini amafuna kuchita. 20Abineri, amene anali ndi anthu makumi awiri, atafika kwa Davide ku Hebroni, Davide anamukonzera phwando pamodzi ndi anthu ake. 21Ndipo Abineri anawuza Davide kuti, “Loleni kuti ndipite msanga kukasonkhanitsa Aisraeli onse kuti abwere kwa inu kuno, mbuye wanga mfumu, kuti adzachite nanu pangano, ndipo kuti muzilamulira kulikonse kumene mtima wanu ufuna.” Kotero Davide analola Abineri kuti apite, ndipo anapita mwamtendere.

Yowabu Apha Abineri

22Nthawi yomweyo ankhondo a Davide ndi Yowabu anafika kuchokera kumene anakathira nkhondo ndipo anabweretsa katundu wambiri wolanda ku nkhondo. Koma Abineri sanalinso ndi Davide ku Hebroni, chifukwa Davide anamulola kuti apite, ndipo anapita mu mtendere. 23Yowabu ndi asilikali onse amene anali naye atafika, anawuzidwa kuti Abineri mwana wa Neri anabwera kwa mfumu ndipo kuti mfumu yamulola kuti apite ndi kuti wapita ndi mtendere.

24Choncho Yowabu anapita kwa mfumu ndipo anati, “Mwachita chiyani? Taonani, Abineri anabwera kwa inu. Nʼchifukwa chiyani mwamulola kuti apite? Tsopanotu wapitadi! 25Inu mukumudziwa bwino Abineri mwana wa Neri. Iye anabwera kudzakunamizani ndi kudzaona mayendedwe anu ndiponso kudzaona zonse zimene mukuchita.”

26Kenaka Yowabu anachoka pamaso pa Davide ndipo anatumiza amithenga kutsatira Abineri, ndipo anabwera naye kuchokera ku chitsime cha Sira. Koma Davide sanadziwe zimenezi. 27Tsono Abineri atabwerera ku Hebroni, Yowabu anamutengera pambali ku chipata, kukhala ngati akufuna kuyankhula naye mwamseri. Ndipo kumeneko pobwezera imfa ya mʼbale wake Asaheli, Yowabu analasa iyeyo mʼmimba, ndipo anafa.

28Patapita nthawi, Davide atamva zimenezi anati, “Ine ndi ufumu wanga tidzakhala osalakwa pamaso pa Yehova pa imfa ya Abineri mwana wa Neri. 29Mlandu umenewu ukhala pa Yowabu ndi banja lonse la abambo ake! Mʼbanja la Yowabu musadzasowe munthu wodwala matenda a chizonono kapena khate, kapena wolumala woyendera ndodo kapena wophedwa ndi lupanga, kapena wosowa chakudya.”

30(Yowabu ndi mʼbale wake Abisai anapha Abineri chifukwa iye anapha mʼbale wawo Asaheli ku nkhondo ku Gibiyoni).

31Ndipo Davide anati kwa Yowabu ndi anthu onse amene anali nawo, “Ngʼambani zovala zanu ndipo muvale ziguduli, muyende mukulira patsogolo pa Abineri.” Mfumu Davide mwini anayenda motsatira chitandacho. 32Iwo anamuyika Abineri mʼmanda ku Hebroni ndipo mfumu inalira mokweza pa manda a Abineri. Ndipo anthu onse analiranso.

33Mfumu inayimba nyimbo iyi ya maliro a Abineri:

“Abineri nʼkufa motere monga mmene chimafera chitsiru.

34Manja ako anali osamanga,

mapazi ako anali osakulungidwa.

Iwe wafa monga mmene amafera anthu pamaso pa anthu oyipa.”

Ndipo anthu onse analiranso kulirira Abineri.

35Kenaka onse anabwera kwa Davide kumuwumiriza kuti adye kusanade. Koma Davide analumbira kuti, “Mulungu andilange ine, andilange kwambiri, ngati ndilawe buledi kapena chilichonse dzuwa lisanalowe!”

36Anthu onse anadziwa zimenezi ndipo zinawakondweretsa ndithu. Zonse zimene mfumu inachita zinawakondweretsa. 37Kotero tsiku limeneli anthu onse ndi Aisraeli onse anadziwa kuti sikunali kufuna kwa mfumu kuti Abineri mwana wa Neri aphedwe.

38Ndipo mfumu inati kwa ankhondo ake, “Kodi inu simukudziwa kuti lero mu Israeli mwagwa kalonga ndi munthu wamkulu? 39Ndipo lero, ngakhale ine ndine mfumu yodzozedwa, ndilibe mphamvu ndipo ana awa a Zeruya ndi amphamvu kwa ine. Yehova abwezere woyipa molingana ndi zoyipa zake!”