撒母耳記下 11 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

撒母耳記下 11:1-27

大衛犯罪

1第二年春天,諸王又要發動戰爭。大衛差遣約押率領眾將領和以色列大軍出征,自己卻留在耶路撒冷。他們打敗了亞捫人之後又圍攻拉巴2一天黃昏,大衛從床上起來在王宮頂上散步,看見一個長得非常漂亮的女人在沐浴。 3大衛就派人去打聽這個女人是誰,得知她是以連的女兒、烏利亞的妻子拔示芭4大衛差人把她接來,她來了,大衛就與她同寢,那時她的月經剛潔淨。事後,她便回家去了。 5拔示芭懷孕了,就派人去告訴大衛

6大衛便傳信給約押,說:「你派烏利亞來見我。」約押就派烏利亞去見大衛7烏利亞來了,大衛問他有關約押、士兵和戰爭的情況, 8然後吩咐他回家休息。烏利亞離開王宮後,收到大衛送的一份禮物。 9但他跟王的其他僕人一同睡在王宮門口,沒有回家。 10大衛得知烏利亞沒有回家,便對他說:「你遠道而來,為什麼不回家休息呢?」 11烏利亞答道:「約櫃、以色列人和猶大人都在帳篷裡,而我主約押及其軍隊也在田間紮營,我怎麼可以回家吃喝快樂,與妻子同房呢?我敢在王面前起誓,我決不做這樣的事!」 12大衛烏利亞說:「你再住一天,明天我會派你回去。」於是烏利亞那日就留在耶路撒冷13第二天,大衛邀請他一同吃飯,把他灌醉了。可是到了晚上,烏利亞還是不肯回家,仍然跟王的其他士兵一同住宿。

14第二天早上,大衛約押寫了一封信,要烏利亞帶去。 15大衛在信上吩咐約押:「你把烏利亞派到前線最險惡的地方,到時其他人都要撤退,好讓敵人殺死他。」 16於是約押圍攻城池時,便派烏利亞到最強悍的敵人那裡。 17敵人出來迎戰,大衛的軍中有幾位陣亡,烏利亞也死了。 18約押就派人去向大衛稟告戰爭的詳情, 19並叮囑信使:「你向王稟告戰情後, 20他若發怒責問你,『為什麼還冒死逼近呢?你們難道不知道敵人會從城牆上射箭嗎? 21難道你們不知道耶路·比設11·21 耶路·比設」又名「耶路·巴力」,參見士師記6·32的兒子亞比米勒是誰殺的嗎?一個婦人從城牆上扔下一塊磨石,把他砸死在提備斯。你們為什麼還要逼近城牆呢?』你就對王說,『你的僕人烏利亞也死了。』」

22於是,信使前來見大衛,照約押的吩咐向大衛稟告。 23他說:「敵軍勢力強大,在城外跟我們交戰,但我們把他們追到城門口。 24敵軍的弓箭手從城牆上射死了王的幾個士兵,烏利亞也死了。」 25大衛便對信使說:「你去告訴約押不要為這事難過,因為刀劍無情。讓他只管竭力攻陷城池。要這樣勉勵約押。」

26拔示芭聽到丈夫烏利亞的死訊之後就為他守喪。 27守喪結束後,大衛便派人把她接進宮裡,她就做了大衛的妻子,並給他生了個兒子。然而,大衛的所作所為令耶和華十分不悅。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Samueli 11:1-27

Davide ndi Batiseba

1Nthawi ya mphukira, nthawi imene mafumu amapita ku nkhondo, Davide anatumiza Yowabu ndi ankhondo a mfumu pamodzi ndi gulu lonse lankhondo la Aisraeli. Iwo anawononga Aamoni ndi kuzungulira mzinda wa Raba. Koma Davide anatsala ku Yerusalemu.

2Tsiku lina cha kumadzulo Davide anadzuka pa bedi lake ndipo ankayenda pamwamba pa nyumba yake. Ali pa dengapo anaona mkazi akusamba. Mkaziyo anali wokongola kwambiri. 3Ndipo Davide anatuma munthu wina kuti akafufuze za iye. Munthuyo anati, “Kodi uyu si Batiseba, mwana wa Eliamu, mkazi wa Uriya Mhiti?” 4Ndipo Davide anatumiza amithenga kwa iye kukamuyitana. Batiseba anabwera kwa Davide ndipo anagona naye. (Nʼkuti mkaziyu atayeretsedwa ku masiku ake osamba). Kenaka anabwerera ku nyumba yake. 5Mkaziyo anakhala woyembekezera ndipo anatumiza mawu kwa Davide kunena kuti, “Ine ndine woyembekezera.”

6Ndipo Davide anatumiza mawu awa kwa Yowabu: “Nditumizire Uriya Mhiti.” Ndipo Yowabu anamutumiza kwa Davide. 7Uriya atafika kwa Davide, Davide anamufunsa za momwe analili Yowabu, za asilikali ndi momwe nkhondo inkayendera. 8Kenaka Davide anati kwa Uriya, “Pita ku nyumba yako ukapumule.” Choncho Uriya anachoka ku nyumba yaufumu, ndipo mfumuyo inatumiza mphatso kwa Uriya. 9Koma Uriya anagona pa chipata cha nyumba yaufumu pamodzi ndi antchito onse a mbuye wake ndipo sanapite ku nyumba yake.

10Davide atawuzidwa kuti, “Uriya sanapite ku nyumba yake.” Iye anafunsa kuti, “Kodi iwe sunachokera kutali? Nʼchifukwa chiyani sunapite ku nyumba yako?”

11Uriya anayankha Davide kuti, “Bokosi la Chipangano ndi Israeli ndiponso Yuda akukhala mʼmatenti, ndipo mbuye wanga Yowabu ndi ankhondo anu mbuye wanga amanga misasa pa mtetete. Ine ndingapite bwanji ku nyumba yanga kukadya ndi kumwa ndiponso kugona ndi mkazi wanga? Pali inu wamoyo, ine sindidzachita chinthu chimenechi.”

12Ndipo Davide anati kwa iye, “Ukhale konkuno tsiku lina limodzi, ndipo mawa ndikulola kuti upite.” Kotero Uriya anakhala mu Yerusalemu tsiku limenelo ndi tsiku linalo. 13Davide anayitana Uriya nadya ndi kumwa naye, ndipo Davide anamuledzeretsa. Koma madzulo Uriya anapita kukagona pa mphasa pamodzi ndi antchito a mbuye wake. Iye sanapite ku nyumba yake.

14Mmawa Davide analemba kalata kwa Yowabu ndipo anayitumiza ndi Uriya. 15Mʼkalatayo analembamo kuti, “Uriya mumuyike patsogolo penipeni, pamene pali nkhondo yoopsa. Ndipo mumusiye yekha kuti akanthidwe ndi kufa.”

16Kotero Yowabu atawuzinga mzindawo, anamuyika Uriya pamalo pamene amadziwa kuti pali asilikali amphamvu. 17Ankhondo a mu mzindawo atabwera kudzamenyana ndi Yowabu, anthu ena a gulu la ankhondo la Davide anaphedwa ndipo Uriya Mhiti uja anaphedwanso.

18Yowabu anatumiza wamthenga kwa Davide kukafotokoza mwatsatanetsatane za nkhondoyo. 19Iye anamulangiza wa mthengayo kuti, “Pamene ukatsiriza kufotokozera mfumu za ku nkhondozi, 20mfumu ikapsa mtima, ndipo akakakufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani munapita pafupi ndi mzindawo kukamenya nkhondo? Inu simunadziwe kuti atha kukuponyerani mivi kuchokera pa khoma? 21Kodi anapha Abimeleki mwana wa Yerubeseti ndani? Kodi mkazi sanamuponyere mphero kuchokera pa khoma? Kotero kuti anakafera ku Tebezi. Nʼchifukwa chiyani munafika pafupi ndi khoma?’ Ngati iye akafunsa zimenezi, iwe ukanene kwa iye kuti, ‘Mtumiki wanunso Uriya Mhiti wafa.’ ”

22Mthengayo ananyamuka, ndipo atafika anamuwuza Davide zonse zimene Yowabu anamutuma kuti akanene. 23Mthengayo anati kwa Davide, “Anthuwo anatiposa mphamvu ndipo anabwera kudzalimbana nafe poyera, koma ife tinawabwezera ku chipata cha mzindawo. 24Ndipo anthu oponya mivi anatiponyera kuchokera pa khoma, anthu ena a mfumu afa. Kuwonjezera apo, mtumiki wanu Uriya Mhiti wafanso.”

25Davide anamuwuza mthengayo kuti, “Ukanene izi kwa Yowabu: ‘Zimenezi zisakukhumudwitse; lupanga limapha wina nthawi zinanso wina. Limbikitsa nkhondo pa mzindawo ndipo uwuwononge!’ Ukanene zimenezi pomulimbikitsa Yowabu.”

26Mkazi wa Uriya atamva kuti mwamuna wake wafa, analira maliro. 27Nthawi yolira maliro itatha, Davide anamubweretsa ku nyumba yake, ndipo anakhala mkazi wake nabala mwana wamwamuna. Koma Yehova sanakondwe ndi zimene Davide anachitazo.