撒母耳記上 29 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

撒母耳記上 29:1-11

非利士人不信任大衛

1非利士人把全部軍隊聚集在亞弗以色列軍則在耶斯列水泉旁紮營。 2非利士首領統率以百人和千人為單位的士兵向前推進,大衛和他的部下跟著亞吉走在隊伍的後面。 3非利士人的官長說:「這些希伯來人在這裡做什麽?」亞吉告訴他們說:「這是以色列掃羅的臣僕大衛,他追隨我有一段日子了,自從他投奔我以來,我沒發現他有什麼過錯。」 4他們卻生氣地說:「請送這個人回到你安置他的地方,他不可和我們一起去打仗,免得他在戰場上倒戈。他提著我們的腦袋去重投故主豈不是最好的方法嗎? 5以前婦女們跳舞歌唱『掃羅殺死千千,大衛殺死萬萬』,歌頌的不就是這個大衛嗎?」

6亞吉便叫大衛過來,對他說:「我憑永活的耶和華起誓,你一向忠心耿耿,自從你投奔我以來,我沒發現你有什麼過錯,我很願意你與我一同作戰,只是眾首領不贊成。 7你安心地回去吧,免得他們不悅。」 8大衛說:「我究竟做錯了什麼?自從僕人投奔你以來,你發現僕人有什麼過錯?為什麼不讓我為我主我王殺敵呢?」 9亞吉說:「你在我眼中就像上帝的天使一樣好,只是非利士眾官長反對你與我們一起出戰。 10明天一早,你就和從掃羅手下投奔你的人啟程回去吧。」

11於是,大衛和部下清早起來返回非利士非利士軍則前往耶斯列

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Samueli 29:1-11

Afilisti Akana Davide

1Afilisti anasonkhanitsa asilikali awo onse ku Afeki, ndipo Israeli anamanga misasa yawo pa chitsime cha Yezireeli. 2Pamene atsogoleri a Afilisti ankatsogolera magulu awo ankhondo a miyandamiyanda, Davide ndi ankhondo ake ankayenda pambuyo pamodzi ndi Akisi. 3Tsono atsogoleri a Afilisti aja anafunsa kuti, “Kodi Ahebri awa akufuna chiyani?”

Akisi anayankha kuti, “Uyu ndi Davide, mtumiki wa Sauli mfumu ya Israeli. Iye wakhala ndi ine kwa masiku ndithu, kapena titi zaka ndipo kuyambira tsiku limene anachoka kwa Sauli mpaka lero, ine sindinapeze cholakwa mwa iye.”

4Koma atsogoleri a ankhondo a Afilisti anamukwiyira Akisi kwambiri ndipo anati, “Mubweze munthuyu kuti abwerere ku malo amene unamupatsa. Iye asapite nafe ku nkhondo kuopa kuti angadzasanduke mdani wathu. Kodi iyeyu adzadziyanjanitsa bwanji ndi mbuye wake? Iyeyutu adzadziyanjanitsa ndi mbuye wake pakupha anthu ali panowa? 5Paja ameneyu ndi Davide yemwe ankamuvinira namuyimbira kuti,

“ ‘Sauli wapha anthu 1,000

koma Davide wapha miyandamiyanda?’ ”

6Kotero Akisi anayitana Davide ndipo anamuwuza kuti, “Pali Yehova wamoyo, iwe wakhala wodalirika ndipo chikanakhala chinthu chabwino kuti uzimenya nkhondo pamodzi nane popeza chibwerere iwe kuno ine sindinapeze cholakwa chilichonse ndi iwe. Koma atsogoleri enawa ndiwo sakukufuna. 7Tsono bwerera. Upite mu mtendere kuopa kuti ungachite kanthu kena koyipira atsogoleri a Afilistiwa.”

8Davide anafunsa Akisi kuti, “Kodi ndachita chiyani? Kodi mwapeza cholakwa chotani mwa ine mtumiki wanu chiyambire kukutumikirani mpaka lero? Tsono chifukwa chiyani sindingapite kukamenya nkhondo ndi adani a mbuye wanga mfumu?”

9Akisi anayankha kuti, “Ine ndikudziwa kuti ndiwe wangwiro ngati mngelo wa Mulungu. Komabe atsogoleri a ankhondo a Afilisti akuti, ‘Davide asapite nafe ku nkhondo.’ 10Tsono udzuke mmamawa, pamodzi ndi ankhondo ako amene unabwera nawo, ndipo unyamuke kukangocha.”

11Choncho Davide ndi anthu ake anadzuka mmamawa kubwerera ku dziko la Afilisti. Koma Afilistiwo anapita ku Yezireeli.