撒母耳記上 13 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

撒母耳記上 13:1-23

掃羅犯罪

1掃羅四十歲13·1 希伯來文無「四十歲」,一些七十士希臘譯本有此數字。登基。他在統治以色列的第二年, 2以色列人中選出三千人,親自帶領其中的兩千人到密抹伯特利山,另外一千人和約拿單留在便雅憫境內的基比亞。他把其餘的人遣散回家。 3約拿單攻打迦巴非利士駐軍,非利士人聽到了這消息。於是,掃羅在各地吹響號角,通告希伯來人。 4以色列眾人聽說掃羅攻打非利士人的駐軍,並聽說非利士人對以色列人恨之入骨,便回應掃羅的號召,聚集在吉甲5非利士人調兵遣將,要攻打以色列。他們有三萬輛戰車和六千騎兵,步兵多如海邊的沙。大軍來到伯·亞文以東的密抹,駐紮在那裡。 6以色列人看見敵軍壓境,情勢危急,紛紛躲進山洞、叢林、石穴、地洞和坑裡。 7有些希伯來人過了約旦河,逃到迦得基列。但掃羅仍然留在吉甲,跟隨他的人都害怕得發抖。

8掃羅按著撒母耳所定的日期在吉甲等了七天,可是撒母耳還沒有來。掃羅的軍兵開始溜走。 9於是,掃羅說:「你們把燔祭和平安祭帶到我這裡來」。他就獻上了燔祭。 10掃羅剛把燔祭獻完,撒母耳就來了,掃羅出去迎接他,向他問安。 11撒母耳掃羅說:「你做的是什麼事?」掃羅答道:「我看見手下的人不斷離我而去,你到了約定的時候還沒有來,而且非利士人就聚集在密抹12我想非利士人就要到吉甲來攻打我們了,但我們還沒有向耶和華求助,我迫不得已,就獻上燔祭了。」 13撒母耳說:「你真糊塗!你違背了你的上帝耶和華的命令。祂本來要使你的王位在以色列永遠堅立, 14但現在你的王位不能長久了,耶和華已經找到一個合祂心意的人,要立他做百姓的君王。因為你沒有遵守耶和華的命令。」 15撒母耳離開吉甲便雅憫境內的基比亞掃羅數了一下跟隨他的人,約有六百人。

16掃羅及其兒子約拿單和隨從留在便雅憫境內的迦巴非利士人則在密抹紮營。 17非利士人分成三隊施行突襲,一隊前往書亞境內的俄弗拉18一隊前往伯·和崙,一隊前往邊境地區,那裡可以俯瞰曠野附近的洗波音穀

19那時,以色列全境找不到一個鐵匠,這是因為非利士人的禁令,以免希伯來人製造刀槍。 20以色列人都要到非利士的鐵匠那裡去磨鋤、犁、斧和鏟。 21磨鋤或犁要花八克銀子,磨三齒叉、斧頭或趕畜棒要花四克銀子。 22所以在交戰的日子,除了掃羅約拿單外,其他以色列人手上都沒有刀槍。 23當時非利士的一隊防兵前往密抹的隘口駐守。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Samueli 13:1-23

Samueli Adzudzula Sauli

1Sauli analowa ufumu ali ndi zaka makumi atatu, ndipo analamulira Israeli kwa zaka 42.

2Nthawi ina Sauli anasankha Aisraeli 3,000. Mwa iwowa, 2,000 anali ndi Sauliyo ku Mikimasi ndi ku dziko la mapiri ku Beteli, ndipo 1,000 anali ndi Yonatani ku Gibeya ku Benjamini. Anthu ena onse otsala anawabweza kwawo.

3Yonatani anakantha mkulu wa ankhondo wa Afilisti ku Geba, ndipo Afilisti anamva kuti Aheberi awukira. Tsono Sauli anawuza amithenga kuti alize lipenga mʼdziko lonse la Israeli. 4Choncho Aisraeli onse anamva kuti Sauli wakantha mkulu wa ankhondo Wachifilisiti ndi kuti Afilisti anayipidwa nawo Aisraeli. Ndiye anthu anayitanidwa kuti abwere kwa Sauli ku Giligala.

5Tsono Afilisti anasonkhana kuti amenyane ndi Aisraeli. Iwo anali ndi magaleta 3,000, okwera pa akavalo 2,000 ndiponso asilikali kuchuluka kwake ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja. Iwo anapita ndi kukamanga misasa yawo ku Mikimasi, kummawa kwa Beti-Aveni. 6Pamene Aisraeli anaona kuti anali pamavuto akulu, poti anali atapanikizidwa kwambiri, anabisala mʼmapanga, mʼmaenje, mʼmatanthwe, mʼmakwalala ndi mʼzitsime. 7Ahebri ena anawoloka Yorodani mpaka kukafika ku dziko la Gadi ndi ku Giliyadi.

Koma Sauli anakhalabe ku Giligala ndipo ankhondo onse amene anali naye anali njenjenje ndi mantha. 8Saulo anadikirira masiku asanu ndi awiri, monga mwa nthawi imene ananena Samueli. Koma Samueli sanabwere ku Giligala, ndipo anthu anayamba kumuthawa Sauli uja. 9Kotero iye anati, “Bwera nayoni nsembe yopsereza ndi nsembe ya chiyanjano.” Ndipo Sauli anapereka nsembe yopsereza. 10Atangomaliza kupereka nsembe, anangoona Samueli watulukira ndipo Sauli anapita kukamulonjera.

11Samueli anafunsa kuti, “Nʼchiyani chimene wachita?”

Sauli anayankha kuti, “Nditaona kuti anthu ayamba kundithawa, ndi kuti inu simunabwere pa nthawi munanena ija, ndiponso kuti Afilisti akusonkhana ku Mikimasi, 12ndinati, ‘Tsopano Afilisti abwera kudzandithira nkhondo ku Giligala kuno, chonsecho sindinapemphe Yehova kuti andikomere mtima.’ Motero ndinakakamizika kupereka nsembe yopsereza.”

13Samueli anati, “Mwachita zopusa. Simunatsate zimene Yehova Mulungu wanu anakulamulani kuti muchite. Mukanazitsata, Yehova akanawukhazikitsa ufumu wanu mu Israeli mpaka kalekale. 14Koma tsopano ufumu wanu sudzakhalitsa. Yehova wapeza munthu wapamtima pake ndipo wamusankha kukhala mtsogoleri wa anthu ake chifukwa inu simunasunge malamulo a Yehova.”

15Kenaka Samueli anachoka ku Giligala ndi kupita ku Gibeyati ku dziko la Benjamini. Saulo anawerenga anthu amene anali naye ndipo analipo 600.

Sauli Akonzekera Nkhondo

16Sauli ndi mwana wake Yonatani pamodzi ndi asilikali amene anali naye aja amakhala ku Geba ku dziko la Benjamini. Koma Afilisti anamanga misasa yawo ku Mikimasi. 17Ankhondo a Afilisti anatuluka mʼmisasa yawo mʼmagulu atatu. Gulu lina linapita ku Ofiri ku dziko la Suwala. 18Gulu lina linalunjika ku Beti-Horoni, ndipo gulu lachitatu linalunjika ku malire oyangʼanana ndi chigwa cha Zeboimu cha ku chipululu.

19Nthawi imeneyo nʼkuti mulibe osula zitsulo mʼdziko lonse la Israeli, pakuti Afilisti anati, “Tisawalole Aheberi kudzipangira okha malupanga kapena mikondo!” 20Kotero Aisraeli onse amapita kwa Afilisti kukanoletsa mapulawo, makasu, nkhwangwa ndi zikwakwa zawo. 21Mtengo wonolera mapulawo ndi makasu unali zigawo ziwiri za sekeli, mtengo wonolera zisonga ndi nkhwangwa unali gawo limodzi la Sekeli.

22Motero tsiku la nkhondolo panalibe lupanga kapena mkondo mʼdzanja la aliyense amene anatsatira Saulo ndi Yonatani. Koma Saulo ndi Yonatani, iwo okha ndiwo anali ndi zida.

Yonatani Athira Nkhondo Afilisti

23Tsono gulu lina lankhondo la Chifilisti linapita kukalonda mpata wa Mikimasi.