提摩太前書 6 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

提摩太前書 6:1-21

1作奴僕的要全心尊重自己的主人,免得上帝的名和我們的教導被人褻瀆。 2若主人是基督徒,作奴僕的不可因為同是信徒就不尊敬自己的主人,反而要更好地服侍他,因為這些接受服侍的人是信徒,是主所愛的。你要教導這些事並勉勵眾人。

異端與貪財

3如果有人傳的教義不符合我們主耶穌基督純正的道和敬虔的教導, 4他就是狂妄自大、一無所知。這種人專好問難,爭辯字句,結果引起嫉妒、紛爭、毀謗和猜忌, 5使那些思想敗壞、失去真理的人爭論不休,甚至把敬虔當作生財之道。 6其實敬虔和知足才是真正的財富, 7因為我們空手來到世上,也要空手離開。 8只要有吃有穿,就該知足。 9那些渴望發財的人卻陷入誘惑、網羅和許多愚蠢有害的慾望中,以致落入敗壞和滅亡中。 10貪財是萬惡之根,有人因為貪財就離棄了信仰,結果飽嚐種種錐心般的痛苦。

保羅對提摩太的囑咐

11但你這屬上帝的人要遠避這些事,要追求公義、敬虔、信心、愛心、忍耐和溫柔, 12要為真道打美好的仗,要持定永生。你是為永生蒙召的,並在許多見證人面前做過美好的見證。 13在賜萬物生命的上帝面前,也在向本丟·彼拉多做過美好見證的基督耶穌面前,我囑咐你: 14要遵守這命令,做純潔無瑕、無可指責的人,一直到我們的主耶穌基督再來。 15到了時候,配得稱頌、獨有權能的萬王之王、萬主之主要使基督顯現。 16上帝是獨一不朽的,住在人不能接近的光中,從來沒有人見過祂,也沒有人能夠看見祂。願尊貴和永遠的權柄都歸給祂。阿們!

17你要勸誡那些今世富足的人不要高傲,也不要冀望於靠不住的錢財,要信靠將萬物厚賜給我們享用的上帝。 18你要勸他們多多行善、慷慨施捨、樂意助人。 19這樣,他們可以為自己的將來奠定美好的基礎,以便持守真正的生命。

20提摩太啊,你要持守所託付給你的,避開世俗的空談和那些違背真理、似是而非的學問。 21有些自稱有這種學問的人已經偏離了信仰。

願恩典與你們同在!

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Timoteyo 6:1-21

1Onse amene ali mu ukapolo ayenera kuona ambuye awo ngati oyenera kuwachitira ulemu, kuti anthu anganyoze dzina la Mulungu ndi chiphunzitso chathu. 2Amene ambuye awo ndi okhulupirira, asawapeputse chifukwa ambuye ndi abale mʼchikhulupiriro. Mʼmalo mwake akuyenera kuwatumikira bwino chifukwa ambuye wawo ndi okondedwa monga okhulupirira ndiponso ndi odzipereka kusamalira akapolo awo.

Aphunzitsi Onyenga ndi Kukonda Ndalama

Zinthu izi ukuyenera kuziphunzitsa ndi kuwalamula anthu. 3Ngati wina aphunzitsa zosiyana ndi zimenezi, wosagwirizana ndi malangizo woona a Ambuye athu Yesu Khristu ndi chiphunzitso cholemekeza Mulungu, 4ameneyo ndi wodzitukumula ndipo sakudziwa chilichonse. Iyeyo ali ndi maganizo oyipa, wokonda kusemphana mawu ndi kutsutsana. Zimenezi zimabweretsa nsanje, mikangano, mʼnyozo, kuganizirana zoyipa, 5ndi kulimbana kosatha pakati pa anthu amitima yopotoka amene alandidwa choonadi ndipo amaganiza kuti kulemekeza Mulungu ndi njira yopezera chuma.

6Koma kulemekeza Mulungu kuli ndi phindu lalikulu. 7Pakuti sitinabweretse kanthu mʼdziko lapansi, ndipo sitingatengenso kanthu pochoka mʼdziko lapansi. 8Koma ngati tili ndi chakudya ndi zovala, zimenezi zitikwanire. 9Anthu amene amafuna kulemera amagwa mʼmayesero ndi mu msampha ndi mʼzilakolako zambiri zopusa ndi zoopsa zimene zimagwetsera anthu mʼchitayiko ndi mʼchiwonongeko. 10Pakuti kukonda ndalama ndiye muzu wa zoyipa za mitundu yonse. Anthu ena ofunitsitsa ndalama, asochera ndipo asiya njira yachikhulupiriro ndipo adzitengera zowawitsa zambiri.

Malangizo Otsiriza kwa Timoteyo

11Koma iwe, munthu wa Mulungu, thawa zinthu zonsezi. Tsatira chilungamo, moyo wolemekeza Mulungu, chikhulupiriro, chikondi, kupirira ndi kufatsa. 12Menya nkhondo yabwino yachikhulupiriro. Gwiritsitsa moyo wosatha umene anakuyitanira pamene unavomereza bwino lomwe pamaso pa mboni zambiri. 13Ndikukulamula pamaso pa Mulungu amene amapatsa moyo zinthu zonse, ndiponso pamaso pa Khristu Yesu amene pochitira umboni pamaso pa Pontiyo Pilato, ananena zoona zenizeni. 14Usunge lamuloli mopanda banga ndi cholakwa kufikira Ambuye athu Yesu Khristu ataonekera. 15Pa nthawi yake Mulungu adzamubweretsa kwa ife. Mulungu ndi wodalitsika ndipo Iye yekha ndiye Wolamulira, Mfumu ya mafumu, Mbuye wa ambuye. 16Ndiye yekha wosafa ndipo amakhala mʼkuwala koopsa. Mulungu amene munthu aliyense sanamuone. Kwa Iye kukhale ulemu ndi mphamvu mpaka muyaya. Ameni.

Za Kudalira Chuma

17Anthu onse amene ali ndi chuma uwalamule kuti asanyade kapena kuyika mitima yawo pa chuma chimene nʼchosadalirika. Koma chiyembekezo chawo chikhale mwa Mulungu amene amatipatsa mowolowamanja zonse zotisangalatsa. 18Uwalamule kuti azichita zabwino, kuti azikhala olemera pa ntchito zabwino, owolowamanja ndi okonda kugawana zinthu zawo ndi anzawo. 19Potero adzadziwunjikira chuma chokhalitsa ngati maziko okhazikika a nthawi zakutsogolo, kuti akalandire moyo, umene ndi moyo weniweni.

Mawu Otsiriza

20Timoteyo, samalitsa zimene unapatsidwa. Upewe nkhani zopanda pake zosalemekeza Mulungu ndiponso maganizo otsutsana amene amaganizidwa molakwika kuti ndi nzeru. 21Anthu ena chifukwa chovomereza nzeru zotere, asochera nʼkutaya chikhulupiriro chawo.

Chisomo chikhale nawe.