彼得前書 3 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

彼得前書 3:1-22

夫妻之道

1-2照樣,作妻子的要順服丈夫。這樣,即使丈夫不信從真道,也會因為看見妻子貞潔和敬虔的品行而被無聲地感化。 3你們不要注重外表的妝飾,像編頭髮、戴金飾或穿華麗的衣服, 4要以溫柔、嫺靜這些永不褪色的內在美為妝飾,這是上帝所看重的。 5從前那些仰賴上帝的聖潔婦女,都是以這些來妝飾自己,並順服自己的丈夫, 6正如撒拉順服亞伯拉罕,稱他為主人。所以,如果你們做對的事,不怕恐嚇,就是撒拉的女兒。

7你們作丈夫的也一樣,要按情理3·7 按情理」希臘文是「按知識」。與妻子共同生活,因為她們比你們軟弱。要敬重她們,因為她們和你們一同承受上帝施恩賜下的生命。這樣,你們的禱告就可以暢通無阻了。

要為義受苦

8總而言之,你們要同心合意,互相關懷,彼此相愛,仁慈謙虛。 9不要以惡報惡,以辱駡還辱駡,反要祝福對方,這是你們蒙召的目的,好叫你們得到祝福。 10因為聖經上說:

「若有人熱愛生命,

渴望幸福,

就要舌頭不出惡言,

嘴唇不說詭詐的話。

11要棄惡行善,竭力追求和睦。

12因為主的眼睛看顧義人,

祂的耳朵垂聽他們的祈求。

但主必嚴懲作惡之人。」

13如果你們熱心行善,有誰會害你們呢? 14就算你們為義受苦,也是有福的。不要害怕別人的恐嚇3·14 不要害怕別人的恐嚇」或譯「不要怕別人所怕的」。,也不要驚慌, 15要心裡尊基督為主。如果有人問起你們心中的盼望,你們要隨時準備答覆, 16但態度要溫和恭敬,存無愧的良心。這樣,那些對你們因信基督而有的好品行妄加誣衊的人會自覺羞愧。 17如果上帝的旨意是要你們因行善而受苦,這也總比你們因作惡而受苦強。

18因為基督也曾一次為罪受苦,以無罪之身代替不義之人,為要領你們到上帝面前。祂的肉體雖被處死,但祂藉著聖靈復活了。 19祂還藉著聖靈向那些監獄中的靈魂傳道, 20他們就是從前在挪亞造方舟、上帝耐心等候人們悔改的時代中那些不肯信的人。當時進入方舟,從洪水中得救的人很少,只有八個人。 21這水代表的洗禮現在藉著耶穌基督的復活也拯救了你們。這洗禮要表明的不是除掉肉體的污穢,而是求在上帝面前有無愧的良心。 22基督已經升到天上,坐在上帝的右邊,眾天使、掌權的、有能力的都服從了祂。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Petro 3:1-22

Akazi ndi Amuna

1Momwemonso, akazi inu gonjerani amuna anu kuti ngati ena a iwo sakhulupirira Mawu a Mulungu, akopeke ndi makhalidwe a akazi awo ndipo sipadzafunikanso mawu 2pamene aona moyo wanu wachiyero ndi moyo woopa Mulungu. 3Kudzikongoletsa kwanu kusakhale kwa maonekedwe akunja, monga kuluka tsitsi ndi kuvala zokometsera zagolide ndi zovala zamberewere. 4Mʼmalo mwake kudzikongoletsa kwanu kukhale kwa munthu wa mʼkatimo, kukongola kosatha kwa mtima ofatsa ndi mzimu wachete, zimene ndi za mtengowapatali pamaso pa Mulungu. 5Pakuti umo ndi mmene akazi oyera mtima akale amene anali ndi chiyembekezo pa Mulungu anadzikongoletsera. Iwo ankagonjera amuna awo, 6monga Sara, amene anamvera Abrahamu namutcha iye mbuye wake. Akazi inu ndinu ana ake ngati muchita zoyenera, ndipo musaope choopsa chilichonse.

7Momwemonso amuna inu, khalani mwanzeru ndi akazi anu, ndipo muwachitire ulemu monga anzanu ofowoka ndiponso olandira nanu pamodzi mphatso ya moyo wosatha, kuti pasakhale kanthu kotsekereza mapemphero anu.

Kumva Zowawa Chifukwa cha Chilungamo

8Potsiriza, nonse khalani a mtima umodzi, omverana chisoni. Kondanani monga abale, muchitirane chifundo ndi kudzichepetsa. 9Wina akakuchitirani choyipa musabwezere pochitanso choyipa, kapena kubwezera chipongwe akakuchitirani chipongwe, koma muwadalitse. Munayitanidwa kuti mulandire mdalitso. 10Pakuti,

“Iye amene angakonde moyo

ndi kuona masiku abwino,

aletse lilime lake kuyankhula zoyipa,

ndiponso milomo yake kunena mabodza.

11Apewe zoyipa, ndipo azichita zabwino.

Afunefune mtendere ndi kuyesetsa kuwupeza.

12Pakuti Ambuye amayangʼanira bwino anthu olungama

ndipo amatchera khutu ku mapemphero awo.

Koma Ambuye sawayangʼana bwino amene amachita zoyipa.”

13Ndani angakuchitireni zoyipa ngati muchita changu kuchita zabwino? 14Koma ngakhale mumve zowawa chifukwa cha chilungamo, ndinu odala. “Musaope anthu, musachite mantha.” 15Koma lemekezani Khristu mʼmitima mwanu ngati Ambuye wanu. Khalani okonzeka nthawi zonse kuyankha aliyense amene akufunsani za chiyembekezo chimene muli nacho. 16Koma chitani zimenezi mofatsa ndi mwaulemu, mukhale ndi chikumbumtima chosakutsutsani, kuti anthu ena akanena zoyipa za makhalidwe anu abwino mwa Khristu, achite okha manyazi ndi chipongwe chawocho. 17Nʼkwabwino ngati ndi chifuniro cha Mulungu kumva zowawa chifukwa chochita zabwino kusiyana ndi kumva zowawa chifukwa chochita zoyipa. 18Pakuti Khristu anafa chifukwa cha machimo kamodzi kokha kufera onse, wolungama kufera osalungama, kuti akufikitseni kwa Mulungu. Anaphedwa ku thupi koma anapatsidwa moyo mu mzimu. 19Ndipo ali ngati mzimu chomwecho anapita ndi kukalalikira mizimu imene inali mʼndende, 20ya anthu amene sanamvere Mulungu atadikira moleza mtima pa nthawi imene Nowa ankapanga chombo. Mʼchombo chija anthu owerengeka okha, asanu ndi atatu, ndiwo anapulumutsidwa ku madzi. 21Madziwo akufanizira ubatizo umene lero ukukupulumutsaninso, osati chifukwa chochotsa litsiro la mʼthupi koma chifukwa cha chikumbumtima choona pamaso pa Mulungu. Umakupulumutsani chifukwa cha kuuka kwa Yesu Khristu, 22amene anapita kumwamba ndipo ali kudzanja lamanja la Mulungu komwe angelo ndi maulamuliro ndi amphamvu amamvera Iye.