彌迦書 3 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

彌迦書 3:1-12

斥責以色列的領袖

1我說:「雅各的首領,以色列家的統治者啊!

你們要聽!

難道你們不知正義嗎?

2你們憎惡良善,

喜愛邪惡,

剝下我百姓的皮,

從他們的骨頭上剔肉。

3你們吃我百姓的肉,

剝我百姓的皮,

打碎他們的骨頭,

把他們切成塊,

如同下在鍋裡、放進釜中的肉。

4你們遭難的時候,

向耶和華呼求,

祂必不應允你們。

因你們的惡行,

祂必掩面不顧你們。」

5耶和華說:

「使我的子民步入歧途的先知啊,

你們向供養你們的人報平安,

出言攻擊那不供養你們的人。

6因此,黑夜必籠罩你們,

使你們看不見異象;

幽暗必臨到你們,

使你們無法占卜。

太陽要因你們而沉落,

白晝變為黑夜。

7假先見必抱愧,

占卜者必蒙羞。

因得不到上帝的答覆,

你們必羞愧地捂著臉。」

8至於我,

因有耶和華的靈,

我充滿權能、正義和力量,

能向雅各宣告他的過犯,

以色列宣告他的罪惡。

9雅各家的首領,以色列家的統治者啊,

你們要聽!

你們厭惡正義,顛倒是非;

10以血腥建立錫安

以罪惡建造耶路撒冷

11城裡的首領為貪贓而枉法,

祭司為銀子而施教,

先知為錢財而占卜。

他們卻宣稱倚靠耶和華,說:

「耶和華不是在我們當中嗎?

災禍不會臨到我們。」

12所以,因你們的緣故,

錫安必像田地被耕犁,

耶路撒冷必淪為廢墟,

聖殿山必成為荒林之岡。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mika 3:1-12

Atsogoleri ndi Aneneri Adzudzulidwa

1Ndipo ine ndinati,

“Tamverani, inu atsogoleri a Yakobo,

inu olamulira nyumba ya Israeli.

Kodi sindinu oyenera kudziwa kuweruza molungama,

2inu amene mumadana ndi zabwino ndi kukonda zoyipa;

inu amene mumasenda khungu la anthu anga,

ndipo mumakungunula mnofu pa mafupa awo;

3inu amene mumadya anthu anga,

mumasenda khungu lawo

ndi kuphwanya mafupa awo;

inu amene mumawadula nthulinthuli

ngati nyama yokaphika?”

4Pamenepo adzalira kwa Yehova,

koma Iye sadzawayankha.

Nthawi imeneyo Iye adzawabisira nkhope yake

chifukwa cha zoyipa zimene anazichita.

5Yehova akuti,

“Aneneri amene

amasocheretsa anthu anga,

ngati munthu wina awapatsa chakudya

amamufunira ‘mtendere;’

ngati munthu wina sawapatsa zakudya

amamulosera zoyipa.

6Nʼchifukwa chake kudzakuderani,

simudzaonanso masomphenya,

mdima udzakugwerani ndipo simudzawombezanso.

Dzuwa lidzawalowera aneneriwo, ndipo mdima udzawagwera.

7Alosi adzachita manyazi

ndipo owombeza mawula adzanyazitsidwa.

Onse adzaphimba nkhope zawo

chifukwa Mulungu sakuwayankha.”

8Koma kunena za ine, ndadzazidwa ndi mphamvu,

ndi Mzimu wa Yehova,

ndi kulungama, ndi kulimba mtima,

kuti ndilalikire za kugalukira kwa Yakobo,

kwa Israeli za tchimo lake.

9Imvani izi, inu atsogoleri a nyumba ya Yakobo,

inu olamulira nyumba ya Israeli,

inu amene mumadana ndi kuweruza kolungama;

ndipo mumakhotetsa zinthu zonse zolondola;

10inu amene mukumanga Ziyoni pokhetsa magazi,

ndi Yerusalemu ndi kuyipa kwanu.

11Atsogoleri ake amalandira chiphuphu kuti aweruze,

ansembe ake amalandira malipiro kuti alalikire,

ndipo aneneri ake amanenera kuti alandire ndalama.

Komatu amatsamira pa Yehova nʼkumanena kuti,

“Kodi Yehova sali pakati pathu?

Palibe tsoka limene lidzatigwere.”

12Choncho chifukwa cha inu,

Ziyoni adzatipulidwa ngati munda,

Yerusalemu adzasanduka bwinja,

ndipo phiri la Nyumba ya Mulungu lidzasanduka nkhalango yowirira.