希伯來書 8 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

希伯來書 8:1-13

更美之約的大祭司

1我們所講的要點是:我們有這樣一位大祭司,祂現在已經坐在天上至高上帝的寶座右邊, 2並在聖所裡供職。這聖所就是真正的聖幕,不是人建立的,而是主親手建立的。 3所有的大祭司都是為了向上帝獻禮物和祭物而設立的,因此我們這位大祭司也必須有所獻上。 4祂如果是在地上,根本不會做祭司,因為地上已經有照律法向上帝獻禮物的祭司了。 5這些祭司的事奉都是仿效和反映天上的事,正如摩西建聖幕的時候,上帝指示他說:

「你務要照著在山上指示你的樣式造各樣的器具。」

6但如今,基督得到了一個更超越的職任,正如祂擔任了更美之約的中保,這約是根據更美的應許所立的。 7因為如果第一個約沒有缺點,就不必另立新約了。 8然而,上帝指責祂的百姓,說:

「看啊,時候將到,

我要與以色列家和猶大家另立新約,

9這約不同於我與他們祖先所立的約,

就是我牽著他們祖先的手領他們離開埃及時所立的。

因為他們不持守我的約,

所以我不再理會他們。

這是主說的。

10主又說,那些日子以後,

我將與以色列家立這樣的約,

我要把我的律法放在他們腦中,

寫在他們心上。

我要作他們的上帝,

他們要作我的子民。

11誰都無需再教導自己的鄰居和弟兄,

說,『你要認識主。』

因為他們無論尊卑都必認識我。

12我要赦免他們的過犯,

忘掉他們的罪惡。」

13上帝既然說要立新約,就是把以前的約當作舊的了,那漸漸過時、陳舊的東西很快就會消失。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ahebri 8:1-13

Mkulu wa Ansembe wa Pangano Latsopano

1Fundo yayikulu pa zimene tikunenazi ndi iyi: Tili naye ife Mkulu wa ansembe, amene anakhala ku dzanja lamanja la mpando waufumu wa Mulungu Waulemerero kumwamba. 2Ndipo akutumikira mʼmalo opatulika, mu Tenti yeniyeni yoyikidwa ndi Ambuye, osati ndi munthu.

3Mkulu wa ansembe aliyense amasankhidwa kuti azipereka mphatso ndi nsembe kwa Mulungu, ndipo kunali koyenera kuti wansembe wathunso akhale nʼkanthu kopereka. 4Ngati iye akanakhala pa dziko lapansi, sakanakhala wansembe pakuti alipo kale anthu amene amapereka mphatso zolembedwa mʼMalamulo. 5Iwo amatumikira pamalo opatulika amene ndi chithunzi ndi chifanizo cha zimene zili kumwamba. Ichi ndi chifukwa chake Mose anachenjezedwa pamene anali pafupi kumanga Tenti: “Uwonetsetse kuti wapanga zonse monga momwe ndikukuonetsera pa phiri pano.” 6Koma Yesu analandira utumiki wopambana kuposa wawo monga Iyenso ali Nkhoswe ya pangano lopambana kuposa lakale lija, chifukwa pangano latsopano lakhazikika pa malonjezano opambana kwambiri.

7Ngati pangano loyamba lija likanakhala langwiro, sipakanafunikanso lina mʼmalo mwake. 8Koma Mulungu anapeza zolakwika pakati pa anthu ndipo anati,

“Masiku akubwera,” akutero Yehova,

“pamene ndidzachita pangano latsopano

ndi Aisraeli

ndiponso nyumba ya Yuda.

9Silidzakhala ngati pangano

limene ndinachita ndi makolo awo,

pamene ndinawagwira padzanja

nʼkuwatulutsa ku Igupto

chifukwa iwo sanasunge pangano langa lija

ndipo Ine sindinawasamalire,

akutero Ambuye.

10Tsono ili ndi pangano ndidzapangane ndi nyumba ya Israeli:

Atapita masiku amenewa, akutero Ambuye,

Ine ndidzayika malamulo anga mʼmaganizo mwawo,

ndi kulemba mʼmitima mwawo.

Ine ndidzakhala Mulungu wawo,

ndipo iwo adzakhala anthu anga.

11Sipadzafunikanso wina kuti aphunzitse mnzake,

kapena munthu kuphunzitsa mʼbale wake, kunena kuti, udziwe Ambuye

chifukwa onse adzandidziwa,

kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu.

12Pakuti Ine ndidzawakhululukira zoyipa zawo,

ndipo sindidzakumbukiranso machimo awo.”

13Ponena kuti, pangano “latsopano” Mulungu wapanga pangano loyamba lija kukhala lotha ntchito, ndipo chilichonse chimene chayamba kutha ntchito ndi kukalamba, chili pafupi kuchokeratu.