希伯來書 12 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

希伯來書 12:1-29

仰望耶穌

1既然有這麼多見證人像雲彩一般圍繞著我們,我們就要放下一切重擔,擺脫容易纏累我們的罪,以堅忍的心奔跑我們前面的賽程, 2定睛仰望為我們的信心創始成終的耶穌。祂為了擺在前面的喜樂,就輕看羞辱,忍受了十字架的痛苦,如今已坐在上帝寶座的右邊。 3你們要思想忍受罪人如此頂撞的主,免得疲倦灰心。

愛的管教

4其實你們與罪惡搏鬥,還沒有抵擋到流血的地步。 5你們難道忘了那像勸勉兒子一樣勸勉你們的話嗎?「孩子啊,不可輕視主的管教,被祂責備的時候也不要灰心。 6因為主管教祂所愛的人,責罰12·6 責罰」希臘文是「鞭打」之意。祂收納的兒子。」

7你們要忍受管教,上帝對待你們如同對待自己的兒子。哪有兒子不受父親管教的呢? 8做子女的都會受管教,如果沒人管教你們,那你們就是私生子,不是兒子。 9再者,我們的生身父親管教我們,我們尚且敬重他們,何況是萬靈之父上帝管教我們,我們豈不更要順服祂並得到生命嗎? 10我們的生身父親是按自己以為好的標準暫時管教我們,但上帝是為了我們的益處而管教我們,使我們可以在祂的聖潔上有份。 11被管教的滋味絕不好受,當時都很痛苦,但事後那些受過管教的人會收穫公義和平安的果子。 12所以,你們要舉起下垂的手,挺直發酸的腿, 13修直腳下的路,使瘸腿的人不致扭傷腳,反得痊癒。

切勿違背上帝

14你們要盡力與大家和睦相處,並要追求聖潔的生活,因為不聖潔的人不能見主。 15你們要謹慎,以免有人失去上帝的恩典,長出苦毒的根擾亂你們,玷污眾人。 16要小心,免得有人像以掃那樣淫亂、不敬虔。他為了一時的口腹之慾,賣了自己長子的名分。 17你們知道,他後來想要承受父親對長子的祝福,卻遭到拒絕,雖然聲淚俱下,終無法使父親回心轉意。

18你們並非來到那座摸得到、有火焰、烏雲、黑暗、狂風、 19號角聲和說話聲的西奈山,聽見這些聲音的人都哀求不要再向他們說話了。 20因為他們承擔不了所領受的命令:「即便是動物靠近這山,也要用石頭打死牠!」 21那情景實在可怕,就連摩西也說:「我嚇得發抖。」

22但你們現在來到了錫安山,永活上帝的城邑,天上的耶路撒冷,歡聚著千萬天使的地方。 23這裡有名字記錄在天上的眾長子的教會,有審判眾人的上帝和已達到純全的義人的靈魂, 24還有新約的中保耶穌和祂所流的血。這血比亞伯的血發出更美的信息。

25你們必須謹慎,切勿拒絕對你們說話的上帝。因為以色列人違背了在地上警戒他們的人,尚且逃脫不了懲罰,何況我們違背從天上警戒我們的上帝呢? 26那時上帝的聲音震動了大地,但現在祂應許說:「再一次,我不單要震動地,還要震動天。」 27「再一次」這句話是指上帝要挪去可以被震動的受造之物,使不能被震動的可以長存。 28那麼,既然我們承受的是一個不能被震動的國度,就要感恩,用虔誠和敬畏的心事奉上帝,討祂喜悅。 29因為我們的上帝是烈火。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ahebri 12:1-29

Yesu Chitsanzo Chathu

1Tsono popeza ifenso tazunguliridwa ndi gulu lalikulu la mboni, tiyeni titaye chilichonse chimene chimatitchinga, makamaka tchimo limene limatikola mosavuta, ndipo tithamange ndi khama mpikisano umene tayambawu. 2Tiyeni tiyangʼanitsitse Yesu, amene ndi woyamba ndi wotsiriza wa chikhulupiriro chathu. Chifukwa cha chimwemwe chimene chimamudikira anapirira zowawa zapamtanda. Iye ananyoza manyazi a imfa yotere ndipo tsopano akukhala ku dzanja lamanja la mpando waufumu wa Mulungu. 3Muzilingalira za Iye amene anapirira udani waukulu chotere wochokera kwa anthu ochimwa, kuti musafowoke ndi kutaya mtima. 4Polimbana ndi uchimo, simunafike mpaka pokhetsa magazi.

Mulungu Amalanga Ana ake

5Kodi mwayiwala mawu olimbitsa mtima aja, amene Mulungu anayankhula kwa inu ngati ana ake? Mawuwo ndi awa:

“Mwana wanga, usapeputse kulanga kwa Ambuye

ndipo usataye mtima pamene akukudzudzula.

6Chifukwa Ambuye amadzudzula amene amawakonda

ndipo amalanga aliyense amene amamulandira.”

7Pamene mukupirira masautso monga chilango, Mulungu achitira inu monga ana ake. Kodi ndi mwana wotani amene abambo ake samulanga? 8Ngati inu simulangidwa, komatu aliyense amalangidwa, ndiye kuti sindinu ana enieni koma amʼchigololo. 9Komanso, tonsefe tinali ndi abambo athu otibala amene amatilanga ndipo timawapatsa ulemu. Nanga kodi sitidzagonjera Atate a mizimu yathu kuti tikhale ndi moyo? 10Abambo athu ankatilanga kwa kanthawi kochepa monga amaonera kufunika kwake, koma Mulungu amatilanga kuti tipindule, kuti tikhale oyera mtima. 11Palibe chilango chimene chimaoneka kuti ndi chabwino pa nthawiyo, komatu chowawa. Koma pambuyo pake, chimabweretsa chipatso chachilungamo ndi mtendere kwa iwo amene aleredwa mwa njira imeneyi.

12Nʼchifukwa chake limbitsani manja anu otopa ndi mawondo anu ogowoka. 13Muziyenda mʼnjira zowongoka, kuti iwo amene akukutsatirani ngakhale ndi olumala ndi ofowoka asapunthwe ndi kugwa koma adzilimbikitsidwa.

Chenjezo kwa Okana Mulungu

14Yesetsani kukhala pa mtendere ndi anthu onse ndi kukhala oyera mtima, pakuti popanda chiyero palibe ndi mmodzi yemwe adzaona Ambuye. 15Yangʼanitsitsani kuti wina aliyense asachiphonye chisomo cha Mulungu ndiponso kuti pasaphuke muzu wamkwiyo umene udzabweretsa mavuto ndi kudetsa ambiri. 16Yangʼanitsitsani kuti pasakhale wina wachigololo. Kapena wosapembedza ngati Esau, amene chifukwa cha chakudya cha kamodzi kokha anagulitsa ukulu wake. 17Monga inu mukudziwa, pambuyo pake pamene anafuna kuti adalitsidwe anakanidwa. Sanapezenso mpata woti asinthe maganizo, ngakhale anafuna madalitsowo ndi misozi.

18Inu simunafike ku phiri limene mungathe kulikhudza, loyaka moto wa mdima bii, la mphepo yamkuntho; 19limene pali kulira kwa lipenga, ndiponso kumveka kwa mawu. Anthu amene amamva mawuwo anapempha kuti asawayankhulenso mawu ena. 20Iwo anachita mantha ndi lamulo lija lakuti, “Ngakhale nyama ikangokhudza phirilo, iphedwe ndi miyala.” 21Maonekedwenso a Mose anali woopsa kwambiri, ngakhale Mose yemwe anati, “Ine ndinachita mantha ndi kunjenjemera.”

22Koma inu mwafika ku Phiri la Ziyoni, ku mzinda wa Mulungu wamoyo, Yerusalemu wakumwamba. Mwafika mu msonkhano wa angelo osangalala osawerengeka. 23Mwafika mu mpingo wa ana oyamba kubadwa, amene mayina awo analembedwa kumwamba. Inu mwafika kwa Mulungu, woweruza anthu onse, ndiponso kwa mizimu ya anthu olungama ndi osandutsidwa kukhala angwiro. 24Kwa Yesu mʼkhalapakati wa pangano latsopano, ndiponso mwafika ku magazi owazidwa amene amayankhula mawu abwino kuposa magazi a Abele.

25Chenjerani kuti musakane kumvera amene akuyankhula nanu. Anthu amene anakana kumvera iye amene anawachenjeza uja pa dziko lapansi pano, sanapulumuke ku chilango ayi, nanga tsono ife tidzapulumuka bwanji ngati tikufulatira wotichenjeza wochokera kumwamba? 26Pa nthawiyo mawu ake anagwedeza dziko lapansi, koma tsopano Iye walonjeza kuti, “Kamodzi kenanso ndidzagwedeza osati dziko lapansi lokha komanso thambo.” 27Mawu akuti, “Kamodzi kenanso,” akuonetsa kuchotsedwa kwa zimene zitha kugwedezeka, zonse zolengedwa, kotero kuti zimene sizingatheke kugwedezeka zitsale.

28Popeza tikulandira ufumu umene sungagwedezeke, tiyeni tikhale oyamika ndi kupembedza Mulungu movomerezeka ndi mwaulemu ndi mantha. 29Pakuti Mulungu wathu ndi moto wonyeketsa.