尼希米記 6 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

尼希米記 6:1-19

敵人陰謀阻撓重建

1參巴拉多比雅阿拉伯基善和我們其餘的敵人聽說我已修完城牆,沒有留下任何缺口——那時我還沒有為城門安上門扇—— 2參巴拉基善就派人告訴我說:「來,我們在阿挪平原的一個村莊見面吧。」其實他們想要害我。 3我派人回覆他們說:「我正在做一件大工程,不能下去見你們。我怎能停止工作下去見你們呢?」 4他們四次派人來告訴我,每次我都這樣拒絕了。 5參巴拉第五次派人送來一封未封口的信, 6上面寫著:「各國都在謠傳,基善也說,你和猶太人計劃謀反,因而才修建城牆,據說你要做他們的王。 7你還派先知在耶路撒冷指著你預言說,『猶大有王了。』如今王必聽到這些傳聞。所以你還是來與我們一同商議吧。」 8我就派人答覆他說:「你所說的並非事實,是你心裡捏造的。」 9因為他們想恐嚇我們,以為我們會嚇得手發軟,無法完成工程。但上帝啊,求你使我的手有力量!

10我到米希達別的孫子、第來雅的兒子示瑪雅的家中,那時他正閉門不出。他對我說:「我們在上帝的殿裡會面,要關上殿門,因為他們要來殺你,要在夜間殺你。」 11但我回答說:「像我這樣的人豈能逃跑?豈能進入殿裡保命?我決不進去。」 12我察覺上帝並沒有差派他,他是被多比雅參巴拉收買才說預言攻擊我的。 13他們收買他是為了恐嚇我,使我依從他去犯罪,好毀壞我的名聲、羞辱我。 14我的上帝啊,求你按照他們的行為報應多比雅參巴拉、女先知挪亞底及其他恐嚇我的先知。

工程竣工

15以祿月6·15 以祿月」即希伯來曆的六月,陽曆是八月中旬到九月中旬。二十五日城牆竣工,前後用了五十二天。 16我們的敵人和周圍各國聽說後,都感到懼怕和氣餒,因為他們知道這工作是在上帝的幫助下完成的。 17在那些日子,多比雅猶大貴族之間多有書信來往。 18猶大有很多人與多比雅結盟,因為他是亞拉的兒子示迦尼的女婿,他兒子約哈難又娶了比利迦的兒子米書蘭的女兒為妻。 19他們常告訴我有關多比雅的善行,並把我的話告訴他。多比雅不斷寫信恐嚇我。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nehemiya 6:1-19

Adani Apitiriza Kutsutsa ndi Kuopseza Nehemiya

1Pamenepo Sanibalati, Tobiya, Gesemu Mwarabu ndi adani athu anamva kuti ndatsiriza ntchito yomanganso khoma ndi kuti palibe mpata umene watsala ngakhale kuti pa nthawi imeneyi ndinali ndisanayike zitseko pa zipata. 2Sanibalati ndi Gesemu, ananditumizira uthenga uwu: “Bwerani tidzakumane pa mudzi wina ku chigwa cha Ono.”

Koma iwo anakonzekera kuti akandichite chiwembu kumeneko. 3Choncho ine ndinatuma amithenga ndi yankho ili: “Ine ndikugwira ntchito yayikulu kuno ndipo sindingathe kubwera kumeneko. Kodi ntchito iyime pofuna kuti ndibwere kumeneko?” 4Ananditumizira uthenga umodzimodzi omwewu kanayi ndipo ndinawayankha chimodzimodzi.

5Tsono kachisanu, Sanibalati anatumiza wantchito wake ndi kalata yosamata. 6Mu kalatamo munali mawu akuti,

“Pali mphekesera pakati pa mitundu ya anthu, ndiponso Gesemu akunena zomwezo kuti inu ndi Ayuda onse mufuna kuwukira boma. Nʼchifukwa chake mukumanga khoma. Mphekeserazo zikutinso inu mukufuna kudzakhala mfumu yawo. 7Mwayikanso kale aneneri amene adzalengeza za iwe mu Yerusalemu kuti ‘Mu Yuda muli mfumu!’ Tsono nkhani iyi imveka ndithu kwa mfumu. Choncho bwerani kuti tidzakambirane.”

8Ine ndinatumiza yankho ili: “Pa zimene mukunenazo, palibe chimene chinachitikapo. Inu mukungozipeka mʼmutu mwanu.”

9Apa adani athu onsewa ankangofuna kutiopseza. Iwo ankaganiza kuti “Tichita mantha ndi kuleka kugwira ntchito.”

Tsono ndinapemphera kuti, “Inu Mulungu ndilimbitseni mtima.”

10Tsiku lina ndinapita ku nyumba ya Semaya mwana wa Delaya mwana wa Mehatabeli. Tsono anandiwuza kuti, “Tiyeni tikakumanire ku Nyumba ya Mulungu. Tikabisale mʼmenemo ndi kutseka zitseko chifukwa akubwera kudzakuphani. Ndithu usiku uno akubwera kudzakuphani.”

11Koma ndinayankha kuti, “Kodi munthu ngati ine nʼkuthawa? Kapena munthu wofanana ndi ine nʼkupita ku Nyumba ya Mulungu kuti apulumutse moyo wake? Ayi, ine sindipita!” 12Ndinazindikira kuti Mulungu sanamutume koma kuti anayankhula mawu oloserawa motsutsana nane chifukwa Tobiya ndi Sanibalati anamulemba ntchitoyi. 13Iye analembedwa ntchitoyi ndi cholinga choti ine ndichite mantha, ndithawe. Ndikanatero ndiye kuti ndikanachimwira Yehova ndiponso iwowo akanandiyipitsira mbiri yanga ndi kumandinyoza.

14Tsono ndinapemphera kuti, “Inu Mulungu wanga, kumbukirani Tobiya ndi Sanibalati chifukwa cha zimene achita. Kumbukiraninso mneneri wamkazi Nowadiya ndi aneneri amene akhala akufuna kundiopseza.”

Kutsiriza kwa Khoma

15Ndipo khoma linatsirizidwa kumanga pa tsiku la 25 la mwezi wa Eluli. Linamangidwa pa masiku okwana 52. 16Adani athu onse atamva izi, mitundu yonse ya anthu yozungulira inachita mantha ndi kuchita manyazi. Iwo anazindikira kuti ntchitoyo inachitika ndi thandizo la Mulungu wathu.

17Komanso masiku amenewo anthu olemekezeka a ku Yuda ankalemberana naye makalata ambiri ndi Tobiyayo, 18pakuti anthu ambiri a ku Yuda anali atalumbira kale kuti adzagwira naye ntchito popeza anali mkamwini wa Sekaniya mwana wa Ara, ndipo mwana wake Yehohanani anakwatira mwana wamkazi wa Mesulamu mwana wa Berekiya. 19Kuwonjezera apo, anthu ankasimba za ntchito zake zabwino ine ndili pomwepo ndipo anakamuwululira mawu anga. Choncho Tobiyayo ankatumiza makalata ondiopseza.