士師記 14 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

士師記 14:1-20

參孫娶非利士女子為妻

1參孫下到亭拿,在那裡看中了一個非利士女子。 2他回到家裡便對父母說:「我在亭拿看中一個非利士女子,把她給我娶來做妻子吧!」 3他父母說:「難道我們的親族和同胞中,沒有一個令你滿意的女子嗎?你為什麼要娶未受割禮的非利士人的女子呢?」參孫卻說:「我很喜歡她,請給我把她娶過來吧!」

4他的父母不知道這事是出於耶和華的旨意,祂要找機會對付非利士人。那時,非利士人統治著以色列

5參孫跟父母一起去亭拿,走到亭拿的葡萄園時,有一頭壯獅吼叫著撲向他。 6耶和華的靈降在參孫身上,他雖然手無寸鐵,竟撕裂了那頭獅子,就像撕裂一隻山羊羔一樣。他沒有把這事告訴父母。 7到了亭拿參孫跟那女子交談,很喜歡她。 8過了些日子,參孫下去迎娶她,途中他順便去看那隻死獅子,見死獅子體內有一群蜜蜂和一些蜂蜜, 9就用手取了一些蜜,邊走邊吃。到了父母那裡,他給了他們一些,他們也吃了。但他沒有告訴父母蜂蜜是從死獅子體內取的。

10參孫的父親去那女子家,參孫按習俗擺設宴席。 11眾人看見參孫,就安排了三十個人陪他。 12參孫對他們說:「我出一個謎語,如果你們可以在這七天的婚宴期間猜出來,我就送你們三十件細麻衣和三十件外袍。 13如果猜不中,你們就要給我三十件細麻衣和三十件外袍。」他們說:「請你出謎語吧!」 14參孫說:

「食物出自食者,

甜物出自強者。」

三天過後,他們仍然猜不出來。

15到了第四天,他們對參孫的妻子說:「你要哄你的丈夫把謎底說出來,不然我們就把你和你父親一家全燒死。你們邀請我們來,難道是要叫我們傾家蕩產嗎?」 16於是,參孫的妻子向他哭訴說:「你是恨我,不是愛我。你給我的族人出了謎語,卻沒有告訴我謎底。」參孫回答說:「我連父母都沒有告訴,又怎能告訴你呢?」 17在七天的婚宴期間,她一直在丈夫跟前哭哭啼啼。到了第七天,參孫經不住妻子的催逼就把謎底告訴了她。她把謎底告訴了她的族人。 18在第七天日落之前,城裡的人對參孫說:

「有什麼比蜂蜜更甜?

有什麼比獅子更強?」

參孫說:

「你們若不是利用我的小母牛耕田,

肯定猜不出來。」

19耶和華的靈降在參孫身上,他便去亞實基倫殺了三十個人,擄走他們的衣服,交給猜中謎語的那些人,然後怒氣沖沖地回父親家去了。 20參孫的妻子後來歸了他的伴郎。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Oweruza 14:1-20

Ukwati wa Samsoni

1Samsoni anapita ku Timna ndipo kumeneko anaonako mtsikana wa Chifilisiti. 2Atabwerera kwawo, anawuza abambo ndi amayi ake kuti, “Ine ndaona mtsikana wa Chifilisiti ku Timna, tsono mukanditengere ameneyo kuti akhale mkazi wanga.”

3Koma abambo ndi amayi ake anayankha kuti, “Kodi palibe mkazi pakati pa abale akowa kapena pakati pa anthu a mtundu wako, kuti iwe upite kukapeza mkazi kwa Afilisti anthu osachita mdulidwe?”

Koma Samsoni anawuza abambo ake kuti, “Kanditengereni ameneyu basi, pakuti ndamukonda.” 4(Abambo ndi amayi ake sankadziwa kuti zimenezi zinali zochokera kwa Yehova, pakuti Yehova amafuna powapezera chifukwa Afilistiwo. Nthawi imeneyo nʼkuti Afilisti akulamulira Aisraeli). 5Choncho Samsoni pamodzi ndi abambo ake anapita ku Timna. Akuyandikira minda ya mpesa ya ku Timna, mwadzidzidzi anamva kubuma kwa mkango waungʼono ukubwera kumene kunali iye. 6Tsono Mzimu wa Yehova unafika ndi mphamvu pa Samsoni ndipo ngakhale analibe chida mʼmanja mwake, iye anakadzula mkangowo ngati akukadzula mwana wambuzi. Koma sanawuze abambo kapena amayi ake zimene anachitazo. 7Kenaka Samsoni anapita kukakambirana ndi mkaziyo, ndipo anamukonda mtsikanayo.

8Patapita nthawi, Samsoni anabwerera kukatenga mtsikana uja. Panjira anapatuka kukaona mkango unawupha uja, ndipo anangoona njuchi zili mu mkangowo pamodzi ndi uchi wake. 9Tsono anakomberako uchi uja mʼmanja mwake ndi kumapita akudya. Atabwereranso kwa abambo ndi amayi ake, anawapatsako uchiwo ndipo anadya. Koma sanawawuze kuti uchi umenewo anawufula mu mkango wakufa.

10Tsopano Samsoni anapita ku nyumba kwa mtsikanayo. Ndipo kumeneko Samsoni anakonza phwando monga ankachitira anyamata. 11Makolo a mkwatibwiyo atamuona, anasankha anyamata makumi atatu kuti akhale naye.

12Samsoni anawawuza kuti, “Bwanji ndikuphereni mwambi. Mukandiwuza tanthauzo lake asanathe masiku asanu ndi awiri aphwandowa, ndidzakupatsani zovala makumi atatu za bafuta ndi zina makumi atatu za tsiku la chikondwerero. 13Koma ngati simutha kundiwuza tanthauzo lake, inuyo mudzandipatsa zovala makumi atatu zabafuta ndi zina za tsiku la chikondwerero.”

Iwo anamuyankha kuti, “Tiwuze mwambi wakowo tiwumve.”

14Iye anati,

“Chakudya chinatuluka mu chinthu chodya chinzake;

ndipo chozuna chinatuluka mu chinthu champhamvu.”

Panapita masiku atatu anthuwo akulephera kumasulira mwambiwo.

15Tsiku lachinayi anthuwo anawuza mkazi wa Samsoni kuti, “Umunyengerere mwamuna wako kuti akuwuze tanthauzo la mwambiwu. Ngati sutero tikutentha iweyo pamodzi ndi nyumba ya abambo ako. Kodi unatiyitana kuti mudzatilande zinthu zathu?”

16Kenaka mkazi wa Samsoni anayamba kulira pamaso pake namuwuza kuti, “Inu mumandida ndipo simundikonda. Mwaphera anyamata a mtundu wathu mwambi, koma ine wosandiwuza tanthauzo lake.”

Samsoni anamuyankha kuti, “Taona sindinawuze abambo kapena amayi anga, ndiye ndiwuze iweyo?” 17Mkaziyo anamulirira masiku onse asanu ndi awiri aphwandowo. Choncho pa tsiku lachisanu ndi chiwiri anamuwuza tanthauzo lake popeza amamukakamiza. Ndipo mkaziyo anakawuza abale ake aja tanthauzo la mwambiwo.

18Pambuyo pake anthu a mu mzinda aja anamuwuza Samsoni pa tsiku lachisanu ndi chiwiri dzuwa lisanalowe kuti,

“Chozuna nʼchiyani choposa uchi?

Champhamvu nʼchiyani choposa mkango?”

Samsoni anawawuza kuti,

“Mukanapanda kutipula ndi ngʼombe yanga yayingʼono,

simukanatha kumasulira mwambi wangawu.”

19Ndipo Mzimu wa Yehova unafika pa iye mwamphamvu. Choncho anatsikira ku Asikeloni naphako anthu makumi atatu, natenga zovala zawo za tsiku la chikondwerero napereka kwa anthu amene anamasulira mwambi wake. Kenaka anabwerera ku nyumba ya abambo ake ndi mkwiyo waukulu. 20Ndipo mkazi wa Samsoniyo anamukwatitsa kwa amene anali mnzake womuperekeza pa ukwati paja.