啟示錄 22 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

啟示錄 22:1-21

1天使讓我看城內街道當中一道流淌著生命水的河,清澈如水晶,從上帝和羔羊的寶座那裡流出。 2河兩岸有結十二種果子的生命樹,每個月都結果子,葉子能醫治萬民。 3再也沒有咒詛,因為城裡有上帝和羔羊的寶座,祂的奴僕都要事奉祂。 4他們必見上帝的面,上帝的名字必印在他們的額上。 5再沒有黑夜,也不需要燈光和陽光,因為主上帝必作他們的光。他們要執掌王權直到永永遠遠。

基督的再來

6天使對我說:「這些話真實可靠。賜聖靈感動眾先知的主上帝已差遣祂的天使,將那些快要發生的事指示給祂的奴僕們。」

7「看啊,我快要來了。遵行這書中預言的人有福了!」

8以上都是我約翰親眼看見、親耳聽見的事。當我聽見、看見這些事後,就俯伏敬拜將這一切指示給我的天使。 9天使對我說:「千萬不可!我與你、你的眾先知弟兄和那些遵行這書上話語的人同是上帝的奴僕,你要敬拜上帝。」

10他又對我說:「不可封住這卷書上的預言,因為時候快到了。 11不義的,讓他繼續不義;污穢的,讓他繼續污穢;公義的,讓他保持公義;聖潔的,讓他保持聖潔。」

12「看啊,我快要來了,到時候我要按各人的行為施行賞罰。 13我是阿拉法,我是俄梅加;我是首先的,我是末後的;我是開始,我是終結。 14那些洗淨自己衣裳的人有福了!他們有權吃生命樹的果子,也可以從城門進入城中。 15那些如同惡犬的敗類、行邪術的、淫亂的、殺人的、拜偶像的和一切喜歡弄虛作假的,都要被拒之城外。 16我耶穌差遣我的天使到眾教會,向你們證明這些事。我是大衛的根,也是大衛的後裔,又是明亮的晨星。」

17聖靈和新娘都說:「來吧!」聽見的也要說:「來吧!」口渴的,讓他來吧!願意的,讓他白白享用生命水吧!

警告

18我鄭重警告所有聽見這書上預言的人:如果誰在這書上增添什麼,上帝必將這書上所記載的災禍加在他身上; 19如果有人從這預言書上刪減什麼,上帝必使他無份於這書上所記載的生命樹和聖城。

20那位證明這些事的說:「是的,我快要來了。」阿們!主耶穌啊,我願你來!

21願主耶穌的恩典與眾聖徒同在。阿們!

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chivumbulutso 22:1-21

Mtsinje Wamoyo

1Ndipo mngeloyo anandionetsa mtsinje wamadzi amoyo, oyera ngati mwala wa krustalo ukutuluka ku mpando waufumu wa Mulungu ndi wa Mwana Wankhosa, 2Ukuyenda pakati pa msewu waukulu wa mu mzindawo. Mbali iliyonse ya mtsinjewo kunali mtengo wamoyo, utabala zipatso khumi ndi ziwiri. Kubereka zipatso mwezi uliwonse. Ndipo masamba a mtengowo ndi mankhwala wochiritsa anthu a mitundu ina. 3Sipadzakhalanso temberero lililonse. Mpando waufumu wa Mulungu ndi wa Mwana Wankhosa udzakhala mu mzindawo, ndipo atumiki ake adzamutumikira. 4Iwo adzaona nkhope yake ndipo dzina lake lidzalembedwa pa mphumi zawo. 5Sipadzakhalanso usiku. Sadzafuna kuwala kwa nyale kapena kwa dzuwa pakuti Ambuye Mulungu adzakhala kuwala kwawo. Ndipo adzalamulira kwamuyaya.

6Mngeloyo anandiwuza kuti, “Mawu awa ndi okhulupirika ndi owona. Ambuye Mulungu wa mizimu ya aneneri anatumiza mngelo wake kudzaonetsa atumiki ake zinthu zimene ziyenera kuchitika posachedwapa.”

Yesu Akubweranso

7“Taonani, ndikubwera posachedwa! Wodala ndi amene asunga mawu oneneratu za kutsogolo a mʼbuku ili.”

8Ine Yohane, ndine amene ndinamva ndi kuona zinthu izi. Ndipo pamene ndinamva ndi kuona izi ndinagwa pansi kuti ndipembedze mngelo amene amandionetsa zimenezi. 9Koma mngeloyo anandiwuza kuti, “Usatero ayi! Ine ndine wotumikira monga iwe pamodzi ndi abale ako aneneri ndi onse amene amasunga mawu a mʼbuku pembedzani Mulungu.”

10Kenaka anandiwuza kuti, “Usabise mawu onena zamʼtsogolo a mʼbuku ili chifukwa nthawi yayandikira. 11Wochita zoyipa apitirire kuchita zoyipazo; wochita zonyansa apitirire kuchita zonyansazo; wochita zabwino apitirire kuchita zabwinozo; ndipo woyera mtima apitirire kukhala woyera mtima.”

Mawu Otsiriza: Kuyitanidwa ndi Chenjezo

12“Taonani, ndikubwera posachedwa! Ndikubwera ndi mphotho zanga kuti ndidzapereke kwa aliyense malinga ndi zimene anachita. 13Ine ndine Alefa ndi Omega, Woyamba ndi Wotsiriza, Chiyambi ndi Chimaliziro ndine.

14“Odala amene achapa mikanjo yawo, kuti akhale ndi ufulu wopita ku mtengo wamoyo ndi kuti akalowe mʼzipata za mu mzindawo. 15Kunja kuli agalu, amatsenga, achiwerewere, akupha anthu, opembedza mafano ndi aliyense amene amakonda bodza ndi kulichita.

16“Ine Yesu, ndatuma mngelo wanga kuti achitire umboni uwu ku mipingo. Ine ndine Muzu ndi Chipatso cha Davide ndipo ndine Nthanda Yonyezimira.”

17Mzimu Woyera ndi mkwatibwi akuti, “Bwerani!” Ndipo amene akumva anena kuti Bwerani! Iye amene ali ndi ludzu abwere, ndipo aliyense amene afuna alandire mphatso yaulere ya madzi amoyo.

18Ndikuchenjeza aliyense amene akumva mawu onena zamʼtsogolo a mʼbukuli kuti, “Ngati wina awonjezerapo kalikonse, Mulungu adzamuwonjezera miliri imene yalembedwa mʼbuku ili. 19Ndipo wina akachotsapo mawu onena zamʼtsogolo a mʼbuku ili, Mulungu adzachotsa gawo lake pa mtengo wamoyo ndi la mu mzinda woyera zimene zanenedwa mʼbuku ili.”

20Iye amene akuchitira umboni pa zinthu izi akuti, “Inde, Ine ndikubwera posachedwa.”

Ameni. Bwerani Ambuye Yesu.

21Chisomo cha Ambuye Yesu chikhale ndi anthu onse. Ameni.