哥林多後書 6 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

哥林多後書 6:1-18

1身為上帝的同工,我們勸你們不要辜負祂的恩典。 2因為祂說:

「在悅納的時候,

我應允了你;

在拯救的日子,

我幫助了你。」

看啊,現在正是悅納的時候!看啊,現在正是拯救的日子!

上帝僕人的品格

3為了避免有人毀謗我們的職分,我們凡事儘量不妨礙別人, 4反倒在任何事上都顯明自己是上帝的僕人。不論遭遇什麼患難、艱苦、貧窮、 5鞭打、囚禁、暴亂、辛勞、無眠或饑餓,我們都堅忍到底, 6靠著純潔、知識、忍耐、仁慈、聖靈的感動、無偽的愛心、 7真理之道、上帝的大能、左右手中的公義兵器, 8無論是得榮耀還是受羞辱,遭毀謗還是得稱讚,都顯明自己是上帝的僕人。我們被視為騙子,卻是誠實無偽; 9似乎默默無聞,卻是家喻戶曉;似乎快死了,看啊!我們卻仍然活著;受嚴刑拷打,卻沒有喪命; 10似乎鬱鬱寡歡,卻常常喜樂;似乎一貧如洗,卻使多人富足;似乎一無所有,卻樣樣都有!

11哥林多人啊!我們對你們推心置腹,開誠佈公, 12毫無保留,只是你們自己心胸太窄。 13現在請你們也向我們敞開心懷。我這樣說,是把你們當成自己的兒女。

永活上帝的殿

14不要和非信徒同負一軛,因為公義和不法怎能合作呢?光明和黑暗怎能共存呢? 15基督與魔鬼6·15 魔鬼」希臘文是「彼列」。怎能相容呢?信徒與非信徒有什麼相干呢? 16上帝的殿與偶像怎能相提並論呢?因為我們就是永活上帝的殿,正如上帝說:

「我要住在他們中間,

在他們當中往來;

我要作他們的上帝,

他們要作我的子民。」

17又說:

「所以,你們要從他們中間出來,

離開他們,不要沾染污穢之物,

我就接納你們。

18我要作你們的父親,

你們要作我的兒女。

這是全能的主說的。」

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Akorinto 6:1-18

1Pogwira naye ntchito pamodzi, tikukudandaulirani kuti musangolandira chisomo cha Mulungu pachabe. 2Pakuti akunena kuti,

“Pa nthawi yanga yabwino yokomera anthu mtima ndinakumvera,

ndipo pa nthawi yopulumutsa ndinakuthandiza.

Taonani, ndikukuwuzani kuti, ino ndiyo nthawi yabwino ya Ambuye, lero ndiye tsiku la chipulumutso.”

Masautso a Paulo

3Ife sitikuyika chokhumudwitsa pa njira ya wina aliyense, kuti utumiki wathu usanyozeke. 4Mʼmalo mwake, mwanjira iliyonse timasonyeza kuti ndife atumiki a Mulungu popirira kwambiri mʼmasautso, mʼzowawa ndi mʼzodetsa nkhawa. 5Pomenyedwa, kuponyedwa mʼndende ndi mʼzipolowe. Pogwira ntchito mwamphamvu, posagona usiku onse, posowa chakudya; 6pokhala moyo woyera mtima, pomvetsa zinthu, wokoma mtima ndi wachifundo mwa Mzimu Woyera ndi mwachikondi choonadi 7ndi poyankhula choonadi mwamphamvu ya Mulungu. Zida zimene zili mʼdzanja lamanja ndi lamanzere ndizo chilungamo. 8Timatumikira Mulungu ngakhale ena amatinyoza ndi ena amatilemekeza, ena amatinenera chipongwe, enanso amatiyamikira. Ena amatitenga kukhala ngati onena zoona, ndipo enanso amatitenga kukhala ngati onena zabodza. 9Amatiyesa osadziwika komatu ndife odziwika kwambiri. Amatiyesa wooneka ngati tikufa, koma tikupitirirabe ndi moyo, okanthidwa, koma osaphedwa. 10Amatiyesa achisoni, koma ndife achimwemwe nthawi zonse, aumphawi, koma olemeretsa ambiri; wopanda kanthu, koma tili ndi zonse.

11Tayankhula momasuka kwa inu, Akorinto, ndipo tanena zonse za kumtima kwathu. 12Ife sitikukubisirani chikondi chathu pa inu, koma inu mukubisa chikondi chanu pa ife. 13Pofuna kufanana zochita ndi kuyankhula monga kwa ana anga, nanunso muzinena za kukhosi kwanu.

Kukhala Pamodzi ndi Osakhulupirira

14Musamasenze goli pamodzi ndi osakhulupirira. Kodi pali mgwirizano wanji pakati pa kulungama ndi kusalungama? Kapena kodi pali mgwirizano wanji pakati pa kuwala ndi mdima? 15Pali mgwirizano wanji pakati pa Khristu ndi Beliyali? Kapena munthu wokhulupirira angayanjane bwanji ndi munthu wosakhulupirira? 16Pali mgwirizano wanji pakati pa Nyumba ya Mulungu ndi nyumba ya mafano? Popezatu ndife Nyumba ya Mulungu wamoyo. Monga Mulungu wanena kuti,

“Ndidzakhala mwa iwo

ndipo ndidzayendayenda pakati pawo,

ndipo ndidzakhala Mulungu wawo,

ndipo adzakhala anthu anga.”

17Nʼchifukwa chake

“Tulukani pakati pawo

ndi kudzipatula,

akutero Ambuye.

Musakhudze chodetsedwa chilichonse,

ndipo ndidzakulandirani.”

18Ndipo

“Ndidzakhala Atate anu,

ndipo inu mudzakhala ana anga aamuna ndi aakazi,

akutero Ambuye, Wamphamvuzonse.”