哈巴谷書 3 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

哈巴谷書 3:1-19

哈巴谷的禱告

1以下是哈巴谷先知的禱告,採用流離調3·1 流離調是希伯來詩歌的一種曲調。

2耶和華啊,我聽過你的威名;

耶和華啊,我對你的作為充滿敬畏。

求你如今再次彰顯你的作為,

求你發怒的時候仍以憐憫為念。

3上帝從提幔來,

聖者從巴蘭山來。(細拉)

祂的榮耀遮蔽諸天,

頌讚祂的聲音響徹大地。

4祂的榮光猶如太陽的光輝,

祂的手射出光芒,

其中蘊藏著大能。

5瘟疫行在祂前面,

災病跟在祂腳後。

6祂停下,大地就震動;

祂觀看,萬民就戰慄。

古老的山嶽崩裂,

遠古的丘陵塌陷,

但祂的作為永遠不變。

7我看見古珊的帳篷遭難,

米甸人的幔子顫抖。

8耶和華啊,你是向江河發怒嗎?

你乘著得勝的戰車而來,

是向江河生氣嗎?

是向海洋發怒嗎?

9你拿出弓,要射出許多箭羽。(細拉)

你以江河分開大地。

10群山看見你就戰慄,

大雨傾盆,

深淵翻騰,波浪滔天。

11你射出的箭閃閃發光,

你的槍熠熠生輝,

以致日月都停在天上。

12你懷著烈怒走遍大地,

踐踏萬國。

13你出來是為了拯救你的子民,

拯救你膏立的王。

你打垮邪惡之人的首領,

從頭到腳徹底毀滅他們。(細拉)

14他們的軍隊如旋風而至,

要驅散我們,

他們以暗中吞噬貧民為樂,

但你用他們的矛刺透他們的頭顱。

15你騎馬踐踏洶湧的大海。

16我聽到這些,

就膽戰心驚,嘴唇哆嗦,

四肢無力,雙腿發抖。

但我仍要靜候災難臨到入侵者的日子。

17即使無花果樹不發芽,

葡萄樹不結果,

橄欖樹無收成,

田地不產糧,

圈裡沒有羊,

棚裡沒有牛,

18我仍要因耶和華而歡欣,

因拯救我的上帝而喜樂。

19主耶和華是我的力量,

祂使我的腳如母鹿的蹄,

穩行在高處。

這首歌交給樂長,用弦樂器伴奏。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Habakuku 3:1-19

Pemphero la Habakuku

1Pemphero la mneneri Habakuku potsata mayimbidwe a Sigionoti.

2Inu Yehova, ndamva za kutchuka kwanu;

Inu Yehova, ntchito zanu zandiopsa.

Muzichitenso masiku athu ano,

masiku athu ano zidziwike;

mu ukali wanu mukumbukire kuchita chifundo.

3Mulungu anabwera kuchokera ku Temani,

Woyerayo kuchokera ku Phiri la Parani.

Sela

Ulemerero wake unaphimba mlengalenga

ndipo dziko lapansi linadzaza ndi matamando ake.

4Kuwala kwa ulemerero wake kunali ngati kutuluka kwa dzuwa;

kunyezimira kunkatuluka mʼdzanja lake,

mʼmene anabisamo mphamvu zake.

5Patsogolo pake pankagwa mliri;

nthenda yoopsa inkagwa kumbuyo kwake.

6Iye anayimirira ndi kugwedeza dziko lapansi;

anayangʼana ndipo mitundu ya anthu inanjenjemera.

Mapiri okhazikika anagumuka

ndipo zitunda zakalekale zinatitimira.

Njira zake ndi zachikhalire.

7Ndinaona matenti a ku Kusani ali pa mavuto,

mokhala a ku Midiyani muli ululu waukulu.

8Inu Yehova, kodi munakwiyira mitsinje?

Kodi munakalipira timitsinje?

Kodi munapsera mtima nyanja

pamene munakwera pa akavalo anu

ndiponso magaleta anu achipulumutso?

9Munasolola uta wanu mʼchimake,

munayitanitsa mivi yambiri.

Sela

Munagawa dziko lapansi ndi mitsinje;

10mapiri anakuonani ndipo anagwedezeka.

Madzi amphamvu anasefukira;

nyanja yozama inakokoma

ndipo mafunde ake anakwera kwambiri.

11Dzuwa ndi mwezi zinayima chilili mlengalenga,

pa kungʼanima kwa mivi yanu yowulukayo,

pa kunyezimira kwa mkondo wanu.

12Munayendayenda mʼdziko lapansi muli ndi ukali,

ndipo munapondereza mitundu ya anthu muli ndi mkwiyo.

13Munapita kukalanditsa anthu anu,

kukapulumutsa wodzozedwa wanu.

Munakantha mtsogoleri wa dziko la anthu oyipa,

munawononga anthu ake onse.

Sela

14Ndi mkondo wake womwe munalasa mtsogoleri wake

pamene ankhondo ake anabwera mwamphamvu kudzatibalalitsa,

ankasangalala ngati kuti akudzawononga

osauka amene akubisala.

15Munapondaponda pa nyanja ndi akavalo anu,

kuvundula madzi amphamvu.

16Ndinamva ndipo mtima wanga unagunda kwambiri,

milomo yanga inanjenjemera pakumva phokosolo;

mafupa anga anaguluka,

ndipo mawondo anga anawombana.

Komabe ndikuyembekezera mofatsa,

tsiku la masautso limene lidzafike pa mtundu wa anthu umene ukutithira nkhondo.

17Ngakhale mtengo wa mkuyu usachite maluwa,

ndipo mipesa ikhale yopanda mphesa.

Ngakhale mitengo ya olivi isabereke zipatso,

ndipo mʼminda musatuluke kanthu.

Ngakhale nkhosa

ndi ngʼombe zithe mʼkhola,

18komabe ine ndidzakondwera mwa Yehova,

ndidzasangalala mwa Mulungu Mpulumutsi wanga.

19Ambuye Yehova ndiye mphamvu yanga;

amalimbitsa miyendo yanga ngati ya mbawala yayikazi,

amandithandiza kukafika pamwamba pa phiri.

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za nsambo.