創世記 45 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

創世記 45:1-28

約瑟與弟兄相認

1約瑟再也控制不住自己,於是令所有的隨從都出去。這樣,約瑟跟弟兄們相認時,沒有外人在場。 2約瑟放聲大哭,埃及人聽見了他的哭聲,法老家也聽到了這個消息。 3約瑟對他的弟兄們說:「我是約瑟!我的父親還健在嗎?」他的弟兄們嚇得一句話也說不出來。

4約瑟叫他們走近一點,等他們靠近了,便說:「我是你們賣到埃及的弟弟約瑟5現在,你們不要因為把我賣到這裡而自怨自責。上帝差我先來這裡,是為了保住大家的性命。 6地上的饑荒已經兩年了,我們還有五年不能種、不能收。 7上帝差我先來,是要為你們保留後代,又要大施拯救,保住你們的性命。 8這樣看來,不是你們,是上帝把我送到這裡的。祂使我成為法老的宰相,管理他的家和整個埃及9你們快回去告訴父親,他兒子約瑟說,『上帝已經使我管理整個埃及,請他立刻來這裡。 10他可以帶著他的子孫、牛羊及一切所有住在歌珊。那裡離我很近, 11我可以奉養他,以免他和全家老少及僕婢牲畜都陷入絕境,因為還有五年的饑荒。』 12你們和我弟弟便雅憫都看見了,這是我親口對你們說的。 13你們要把我在埃及享有的尊榮和你們見到的一切都告訴父親,儘快把他接來。」 14約瑟和弟弟便雅憫抱頭痛哭, 15然後又親吻其他弟兄,抱著他們痛哭,弟兄們跟他交談起來。

16約瑟弟兄們到來的消息傳到法老的王宮,法老和他的臣僕都為約瑟感到高興。 17法老對約瑟說:「你去吩咐你的弟兄備好驢回迦南18把你們的父親和家眷都接到我這裡。我要把埃及最好的土地賜給他們,讓他們享受這裡肥美的物產。 19吩咐你的弟兄從埃及帶著車去把他們的妻子、兒女和你們的父親接來。 20不要擔心你們在迦南的產業,因為埃及全國的美物都是你們的。」

21以色列的兒子們答應了。約瑟遵照法老的吩咐,為他的弟兄們預備好車輛和路上需用的糧食, 22又給他們每人一套新衣服,但給了便雅憫五套新衣服和三百塊銀子。 23約瑟送給父親十頭公驢,馱著埃及的美物,還送了十頭母驢,馱著糧食、餅和其他食物,讓父親路上用。 24約瑟送弟兄們回去,囑咐他們路上不要爭吵。

25於是,他們離開埃及回到在迦南的父親雅各那裡, 26對父親說:「約瑟還活著,並且做了埃及的宰相。」雅各驚呆了,不敢相信他們的話。 27雅各聽了他們轉述約瑟的話,又看見約瑟派來接他的車,才回過神來。 28以色列說:「我信了!我兒約瑟還活著,我要在死之前去見他。」

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 45:1-28

Yosefe Adziwulula kwa Abale Ake

1Tsono Yosefe sanathenso kuwugwira mtima kuti asalire pamaso pa antchito ake ndipo anafuwula kuti, “Aliyense achoke pamaso panga!” Motero panalibe wina aliyense pamene Yosefe anadziwulula kwa abale ake. 2Ndipo analira mokweza mwakuti Aigupto anamva. Onse a ku nyumba kwa Farao anamvanso za zimenezi.

3Yosefe anati kwa abale ake, “Ine ndine Yosefe! Kodi abambo anga akanali ndi moyo?” Koma abale ake sanathe kumuyankha chifukwa anali ndi mantha kwambiri pamaso pake.

4Ndipo Yosefe anati kwa abale ake, “Senderani pafupi nane.” Atasendera iye anati, “Ine ndine mʼbale wanu Yosefe amene munamugulitsa ku Igupto! 5Ndipo tsopano, musawawidwe mtima kapena kudzipsera mtima chifukwa choti munandigulitsa ine kuno, popeza Mulungu ananditsogoza ine kuti adzapulumutse miyoyo yanu. 6Kwa zaka ziwiri tsopano, kwakhala kuli njala mʼdziko muno, ndipo kwa zaka zisanu zikubwerazi, anthu sadzalima kapena kukolola. 7Koma Mulungu ananditsogoza kuti adzakusungeni ndi moyo ndi kuti mudzakhale ndi zidzukulu pa dziko lapansi.

8“Motero, si inu amene munanditumiza kuno koma Mulungu. Iye anandisandutsa kukhala nduna yayikulu ya Farao, ndipo zonse za mʼnyumba mwake zili mʼmanja mwangamu. Komanso amene akulamulira dziko lonse la Igupto ndi ine. 9Tsono fulumirani mubwerere kwa abambo anga ndi kuwawuza kuti, ‘Mwana wanu Yosefe akuti, Mulungu anandisandutsa kukhala mbuye wa dziko lonse la Igupto. Ndiye bwerani kuno musachedwe. 10Ndipo inu, ana anu, zidzukulu zanu, pamodzi ndi nkhosa ndi ngʼombe zanu ndi antchito anu amene muli nawo muzidzakhala mʼdziko la Goseni pafupi ndi ine. 11Ine ndizidzakupatsani zakudya kumeneko chifukwa zaka zisanu za njala zikubwera ndithu. Kupanda kutero, inu ndi mabanja anu pamodzi ndi anthu anu onse mudzasowa chakudya.’

12“Tsono inu nonse pamodzi ndi mʼbale wangayu Benjamini, mukuona kuti ndi inedi amene ndikuyankhula nanu. 13Mukawawuze abambo anga kuti ndili pa ulemerero ku dziko la Igupto kuno ndi zonse zimene mwaziona. Tsopano fulumirani kuti mukabwere nawo kuno abambo anga.”

14Kenaka Yosefe anakhumbatira Benjamini, mngʼono wake uja nayamba kulira. Nayenso Benjamini anayamba kulira atamukumbatira. 15Atatero, Yosefe anapsompsona abale ake onse aja, akulira. Pambuyo pake abale ake aja anacheza ndi Yosefe.

16Akunyumba kwa Farao atamva kuti abale ake a Yosefe abwera, Farao pamodzi ndi nduna zake zonse anakondwera. 17Farao anati kwa Yosefe, “Uwawuze abale ako kuti, ‘Senzetsani nyama zanu katundu ndi kubwerera ku dziko la Kanaani. 18Mukabwere nawo abambo anu ndi mabanja anu kuno, ndipo ine ndidzakupatsani dera lachonde kwambiri mʼdziko la Igupto. Mudzadya zokoma za mʼdzikoli.’ ”

19“Uwawuzenso kuti, ‘Tengani ngolo zingapo za kuno ku Igupto kuti mukakwezepo ana anu, akazi anu pamodzi ndi abambo ako ndi kubwera nawo kuno. 20Musadandaule zosiya katundu komweko chifukwa dziko lachonde la kuno ku Igupto lidzakhala lanu.’ ”

21Choncho ana a Israeli anachita zimenezo. Yosefe anawapatsa ngolo monga Farao analamulira, ndipo anawapatsanso chakudya cha paulendo wawo. 22Anaperekanso kwa aliyense zovala zatsopano, koma kwa Benjamini anapereka siliva wolemera pafupifupi makilogalamu anayi ndi zovala zisanu. 23Ndipo abambo ake anawatumizira izi: abulu khumi osenza zinthu zabwino kwambiri za ku Igupto, ndi abulu aakazi khumi osenza tirigu, buledi ndi zakudya zina za pa ulendo wake. 24Kenaka anawalola abale ake aja kuti azipita, ndipo akunyamuka, iye anawawuza kuti, “Osakangana mʼnjira!”

25Ndipo anachoka ku Igupto nafika kwa abambo awo Yakobo mʼdziko la Kanaani. 26Iwo anawuza abambo awo kuti, “Yosefe akanali ndi moyo! Ndiponsotu, ndiye akulamulira dziko la Igupto.” Yakobo anangoti kakasi osankhulupirira. 27Komabe atamufotokozera zonse zimene Yosefe anawawuza ndipo ataona ngolo zimene Yosefe anatumiza kuti adzakweremo popita ku Igupto, mtima wa Yakobo, abambo awo unatsitsimuka. 28Ndipo Israeli anati, “Ndatsimikizadi! Mwana wanga Yosefe akanali ndi moyodi. Ndipita ndikamuone ndisanafe.”