創世記 25 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

創世記 25:1-34

亞伯拉罕的其他後代

1亞伯拉罕又娶了基土拉2基土拉亞伯拉罕生了心蘭約珊米但米甸伊施巴書亞3約珊生了示巴底但底但的子孫是亞書利族、利都示族和利烏米族。 4米甸的兒子是以法以弗哈諾亞比大以勒大。這些都是基土拉的子孫。 5亞伯拉罕把所有的財產都給了以撒6他趁自己還在世的時候,把一些禮物送給他的妾所生的兒子們,讓他們離開他的兒子以撒到東方去。

7亞伯拉罕活了一百七十五歲, 8享盡天年,壽終正寢,歸到他祖先那裡。 9他的兩個兒子以撒以實瑪利把他安葬在麥比拉洞,那山洞在幔利附近、瑣轄的兒子以弗崙的地裡。 10那塊地是亞伯拉罕人買的,他和妻子撒拉葬在一起。 11亞伯拉罕去世以後,上帝賜福給他的兒子以撒以撒住在庇耳·拉海·萊附近。

12以實瑪利亞伯拉罕撒拉的婢女埃及夏甲所生的兒子。 13以下是以實瑪利的兒子,按出生的次序是:尼拜約基達亞德別米比衫14米施瑪度瑪瑪撒15哈大提瑪伊突拿非施基底瑪16他這十二個兒子後來分別成了十二個族的族長,各有自己的村莊和營寨。 17以實瑪利活了一百三十七歲,壽終正寢,歸到他祖先那裡。 18他子孫居住的地方從哈腓拉一直延伸到埃及東面、通往亞述方向的書珥,他們與其他親屬作對25·18 與其他親屬作對」或譯「住在其他親屬的東面」。

利百加生以掃和雅各

19以下是關於亞伯拉罕的兒子以撒的記載。

亞伯拉罕以撒20以撒四十歲娶利百加利百加巴旦·亞蘭的亞蘭人彼土利的女兒、拉班的妹妹。 21以撒因為利百加沒有生育,就為她祈求耶和華。耶和華應允了他的祈求,利百加就懷了孕。 22兩個胎兒在她腹中彼此相爭,她說:「怎麼會這樣?」於是,她去求問耶和華。 23耶和華對她說:

「你腹中有兩個國家,

你要生出兩個敵對的民族,

一族要比另一族強大,

將來大的要服侍小的。」

24到了生產的時候,利百加果然生下雙胞胎。 25先出生的嬰兒遍體通紅,渾身長毛,好像穿了皮衣,因此給他取名叫以掃25·25 以掃」意思是「有毛」。26隨後出生的弟弟緊緊抓著以掃的腳跟,因此給他取名叫雅各25·26 雅各」意思是「抓住」。。那時以撒六十歲。

以掃出賣長子名分

27孩子們漸漸長大,以掃擅長狩獵,常在田野活動;雅各生來安靜,喜歡待在家裡。 28以撒疼愛以掃,因為他喜歡吃以掃帶回來的獵物,利百加卻疼愛雅各

29一天,雅各正在熬湯,以掃精疲力盡地從田野回來。 30以掃雅各說:「我要餓死了,給我一些紅豆湯喝吧!」因此,以掃又叫以東25·30 以東」意思是「紅色」。31雅各回答說:「好,你今天把長子的名分賣給我吧!」 32以掃說:「我都快餓死了,長子的名分對我有什麼用呢?」 33雅各說:「好,你現在向我起誓保證吧!」於是,以掃就起誓把長子的名分賣給了雅各34雅各把餅和紅豆湯給以掃以掃吃完喝完便走了。以掃輕看自己長子的名分。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 25:1-34

Abrahamu Amwalira

1Abrahamu anakwatira mkazi wina dzina lake Ketura. 2Iyeyu anamubalira Zimurani, Yokisani, Medani, Midiyani, Isibaki ndi Suwa. 3Yokisani anabereka Seba ndi Dedani ndipo zidzukulu za Dedani ndiwo Aasuri, Aletusi, ndi Aleumi. 4Ana aamuna a Midiyani anali, Efai, Eferi, Hanoki, Abida ndi Elida. Onsewa anali zidzukulu za Ketura.

5Abrahamu anasiyira Isake chilichonse anali nacho. 6Koma pamene anali ndi moyo, Abrahamu anapereka mphatso kwa ana aakazi ake ena onse. Kenaka anawatumiza ku dziko la kummawa kuti akhale kutali ndi mwana wake Isake.

7Abrahamu anakhala ndi moyo zaka 175. 8Abrahamu anamwalira atakalamba kwambiri ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake. 9Ana ake, Isake ndi Ismaeli anamuyika mʼphanga la Makipela pafupi ndi Mamre, mʼmunda umene kale unali wa Efroni mwana wa Zohari Mhiti, 10uwu ndi munda umene Abrahamu anagula kwa Ahiti. Kumeneko Abrahamu anakayikidwa pamodzi ndi mkazi wake Sara. 11Atamwalira Abrahamu, Mulungu anadalitsa mwana wake Isake, amene ankakhala pafupi ndi Beeri-lahai-roi (chitsime cha Wamoyo Wondipenya).

Ana Aamuna a Ismaeli

12Nazi zidzukulu za Ismaeli, mwana wa Abrahamu amene wantchito wa Sara, Hagara Mwigupto uja, anaberekera Abrahamu.

13Awa ndi mayina a ana a Ismaeli monga mwa mndandanda wa mabadwidwe awo: Nebayoti ndiye anali mwana woyamba wa Ismaeli; kenaka Kedara, Adibeeli, Mibisamu, 14Misima, Duma, Masa, 15Hadadi, Tema, Yeturi, Nafisi ndi Kedema; 16Amenewa ndi ana a Ismaeli ndi mayina awo monga mwa midzi ndi misasa yawo. Anali olamulira mafuko khumi ndi awiri. 17Ismaeli anakhala ndi moyo zaka 137. Iye anamwalira ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake. 18Zidzukulu za Ismaeli zinkakhala mʼdera la pakati pa Havila ndi Suri, kummwera kwa Igupto, mukamapita cha ku Asuri. Choncho anakhala kummawa kwa abale awo.

Yakobo ndi Esau

19Iyi ndi mbiri ya Isake mwana wa Abrahamu.

Abrahamu anabereka Isake 20ndipo Isake anali ndi zaka makumi anayi pamene anakwatira Rebeka mwana wa Betueli Mwaramu wa ku Padanaramu mlongo wa Labani Mwaramu.

21Isake anapempherera mkazi wake kwa Yehova popeza iye anali wosabereka. Yehova anayankha pemphero lake ndipo mkazi wake Rebeka anatenga pathupi. 22Koma pamene anawo amalimbana mʼmimba mwake, iye anati, “Bwanji zikundichitikira zoterezi?” Choncho anapita kukafunsa kwa Yehova.

23Yehova anati kwa iye,

“Udzabala mafuko awiri a anthu olimbana,

ndipo magulu awiri a anthu ochokera mwa iwe adzasiyana;

fuko limodzi lidzakhala la mphamvu kuposa linzake,

ndipo wamkulu adzatumikira wamngʼono.”

24Pamene nthawi inakwana yakuti abeleke, Rebeka anaberekadi mapasa. 25Woyamba kubadwa anali wofiira, ndipo thupi lake lonse linali ngati chovala cha ubweya; choncho anamutcha Esau. 26Kenaka mʼbale wake anabadwa atagwira chidendene cha Esau; choncho anamutcha Yakobo. Isake anali ndi zaka 60 pamene Rebeka anabereka mapasawa.

27Anyamatawo anakula ndipo Esau anakhala katswiri wosaka, munthu wamʼthengo, pamene Yakobo anali munthu wofatsa, wokonda kukhala pa nyumba. 28Isake ankakonda Esau chifukwa cha nyama za kutchire zomwe ankakonda kudya, koma Rebeka ankakonda Yakobo.

29Tsiku lina pamene Yakobo ankaphika chakudya, Esau anabwera kuchokera kuthengo ali wolefuka ndi njala. 30Iye anati kwa Yakobo, “Tandipatsako phala lofiiralo, ndimwe! Ndalefuka ndi njala.” (Nʼchifukwa chake amatchedwanso Edomu).

31Yakobo anayankha, “Choyamba undigulitse ukulu wako.”

32Esau anati, “Chabwino, ine ndatsala pangʼono kufa, ukulu undithandiza chiyani?”

33Koma Yakobo anati, “Lumbira kwa ine choyamba.” Kotero Esau analumbiradi, ndipo anagulitsa ukulu wake kwa Yakobo.

34Choncho Yakobo anamupatsa Esau buledi ndi phala lofiira lija. Iye anadya ndi kumwa, nanyamuka kumapita.

Motero Esau anapeputsa ukulu wake wachisamba uja.