列王紀下 14 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

列王紀下 14:1-29

亞瑪謝做猶大王

1以色列約哈斯的兒子約阿施執政第二年,猶大約阿施的兒子亞瑪謝登基。 2他二十五歲登基,在耶路撒冷執政二十九年。他母親叫約耶但,是耶路撒冷人。 3亞瑪謝做耶和華視為正的事,雖不如他祖先大衛,但事事效法他父親約阿施4然而,他沒有拆毀邱壇,人們仍在那裡獻祭燒香。 5他鞏固了王位後,立即處死了殺他父王的臣僕, 6但沒有處死他們的孩子,遵照了耶和華在摩西律法書中的吩咐:「不可因孩子犯罪而處死父親,也不可因父親犯罪而處死孩子。各人要自負罪責。」 7亞瑪謝曾在鹽谷殺了一萬以東人,攻佔了西拉,把西拉改名為約帖,沿用至今。

8後來,亞瑪謝差遣使者對耶戶的孫子、約哈斯的兒子、以色列約阿施說:「來,我們戰場上見。」 9以色列約阿施派人對猶大亞瑪謝說:「黎巴嫩的蒺藜派使者去對黎巴嫩的香柏樹說,『將你女兒嫁給我兒子吧。』後來黎巴嫩的一隻野獸經過,把那蒺藜踐踏在腳下。 10你打敗了以東人就趾高氣揚,還是待在家裡慶祝勝利吧,何必惹禍上身,使你和猶大一同滅亡呢?」

11亞瑪謝不理會他的勸告。於是,以色列約阿施起兵攻打猶大亞瑪謝,兩王會戰於猶大伯·示麥12猶大人被以色列人打敗,兵將都各自逃回家去了。 13約阿施伯·示麥擒獲亞瑪謝,然後前往耶路撒冷,拆毀從以法蓮門到角門約一百八十米長的耶路撒冷城牆, 14搶走耶和華殿裡和王宮庫房裡的所有金銀和器皿,並帶著人質返回撒瑪利亞15約阿施其他的事,包括他怎樣英勇對抗猶大亞瑪謝,都記在以色列的列王史上。 16約阿施與祖先同眠後,葬在撒瑪利亞的色列王陵。他兒子耶羅波安繼位。

17以色列約哈斯的兒子約阿施死後,猶大約阿施的兒子亞瑪謝又活了十五年。 18亞瑪謝其他的事都記在猶大的列王史上。 19耶路撒冷有人謀反,亞瑪謝就逃到拉吉,叛黨派人追到那裡殺了他。 20有人用馬將他的屍體馱回耶路撒冷,葬在大衛城他的祖墳裡。 21猶大民眾擁立亞瑪謝十六歲的兒子亞撒利雅14·21 「亞撒利雅」即烏西雅。為王。 22亞瑪謝與祖先同眠後,亞撒利雅猶大收回了以拉他,並重新修建。

耶羅波安二世

23猶大亞瑪謝執政第十五年,以色列約阿施的兒子耶羅波安撒瑪利亞登基,執政四十一年。 24他做耶和華視為惡的事,沒有離開尼八的兒子耶羅波安使以色列人犯的那些罪。 25他收復了從哈馬口到死海14·25 「死海」希伯來文是「亞拉巴海」。一帶的以色列邊境,正如以色列的上帝耶和華藉祂僕人迦特希弗亞米太的兒子約拿先知所言。 26因為耶和華看見以色列人,無論自由人還是奴隸都十分痛苦,沒有人幫助他們。 27耶和華沒有說要從世上抹去以色列的名,因此他藉著約阿施的兒子耶羅波安拯救他們。 28耶羅波安其他的事及其一切所作所為,包括他怎樣英勇收復大馬士革和一度屬猶大國的哈馬,都記在以色列的列王史上。 29耶羅波安與祖先——以色列的先王們同眠後,他兒子撒迦利雅繼位。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mafumu 14:1-29

Amaziya Mfumu ya Yuda

1Mʼchaka chachiwiri cha Yehowasi mwana wa Yowahazi mfumu ya Israeli, Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anayamba kulamulira. 2Iye anali ndi zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 29. Amayi ake anali Yehoyadini wa ku Yerusalemu. 3Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, koma osafanana ndi zomwe anachita Davide kholo lake. Iye anatsatira zochita zonse za Yowasi abambo ake. 4Komabe sanachotse malo opembedzerapo mafano. Anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.

5Atakhazikika mu ufumu wake, Amaziya anapha atumiki ake amene anapha abambo ake, mfumu ija. 6Komatu iye sanaphe ana a anthu amene anapha abambo ake potsatira zomwe zinalembedwa mʼbuku la Malamulo a Mose. Mʼmenemo Yehova analamula kuti, “Makolo asaphedwe chifukwa cha ana awo, ndipo ana asaphedwe chifukwa cha makolo awo, koma aliyense ayenera kufa chifukwa cha zolakwa zake.”

7Iye ndiye amene anapha Aedomu 10,000 mʼchigwa cha Mchere nalanda mzinda wa Sela pa nkhondo ndipo anawutcha Yokiteeli, dzina lake ndi lomwelo mpaka lero lino.

8Tsono Amaziya anatuma amithenga kwa Yehowasi mwana wa Yehowahazi, mwana wa Yehu mfumu ya Israeli ndi kumuopseza kuti, “Bwera tidzaonane maso ndi maso.”

9Koma Yehowasi mfumu ya Israeli anabweza mawu kwa Amaziya mfumu ya Yuda kuti, “Mtengo wa minga wa ku Lebanoni unatumiza uthenga kwa mkungudza wa ku Lebanoni. ‘Patse mwana wako wamkazi kuti ndimukwatire.’ Kenaka chirombo cha ku Lebanoni chinabwera ndi kupondaponda mtengo wa mingawo. 10Inde iwe wagonjetsa Edomu ndipo tsopano wayamba kudzikuza. Dzitamandire chifukwa cha kupambana kwako, koma khala kwanu konko! Nʼchifukwa chiyani ukuyamba dala mavuto amene adzakuwononga pamodzi ndi Yuda?”

11Koma Amaziya sanamvere zimenezi. Choncho Yehowasi mfumu ya Israeli anakamuthira nkhondo. Yehowasi ndi Amaziya anakumana maso ndi maso ku Beti-Semesi mʼdziko la Yuda. 12Israeli anagonjetsa Yuda ndipo munthu aliyense anathawira kwawo. 13Yehowasi mfumu ya Israeli anagwira Amaziya mfumu ya Yuda, mwana wa Yowasi, mwana wa Ahaziya ku Beti-Semesi. Ndipo anapita ku Yerusalemu nakagwetsa khoma la Yerusalemu kuyambira ku Chipata cha Efereimu mpaka ku Chipata Chapangodya, gawo lotalika mamita 180. 14Iye anatenga golide ndi siliva yense pamodzi ndi ziwiya zonse zimene zinali mʼNyumba ya Yehova ndi zimene zinali mosungira chuma cha nyumba ya mfumu. Iye anagwiranso anthu nabwerera ku Samariya.

15Ntchito zina za Yehowasi ndi zonse zimene anachita, kuwonjezera za nkhondo yake ndi Amaziya mfumu ya Yuda, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli? 16Yehowasi anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu Samariya pamodzi ndi mafumu a Israeli. Ndipo mwana wake Yeroboamu analowa ufumu mʼmalo mwake.

17Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anakhala zaka khumi ndi zisanu atamwalira Yehowasi mwana wa Yehowahazi mfumu ya Israeli. 18Ntchito zina za Amaziya, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?

19Anthu anapangana zomuchita chiwembu mu Yerusalemu ndipo Amaziya anathawira ku Lakisi, koma anatumiza anthu ku Lakisiko nakamuphera komweko. 20Anabwera naye ku pa kavalo ku Yerusalemu ndi kumuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide.

21Ndipo anthu onse a ku Yuda anatenga Azariya, amene anali ndi zaka 16 namulonga ufumu mʼmalo mwa abambo ake Amaziya. 22Azariya anamanga mzinda wa Elati ndi kuwubwezeretsa ku Yuda, Amaziya atamwalira.

Mfumu Yeroboamu Wachiwiri wa ku Israeli

23Mʼchaka cha khumi ndi chisanu cha Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda, Yeroboamu mwana wa Yehowasi mfumu ya Israeli analowa ufumu ku Samariya ndipo analamulira za 41. 24Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova ndipo sanasiye machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli. 25Iye ndi amene anabwezeretsanso malire a Israeli kuyambira ku Lebo Hamati mpaka ku Nyanja ya Araba, molingana ndi zimene ananena Yehova Mulungu wa Israeli, kudzera mwa mtumiki wake Yona mwana wa Amitai, mneneri wochokera ku Gati-Heferi.

26Pakuti Yehova anaona masautso a Israeli amene anali owawa kwambiri, panalibe kapolo kapena mfulu ngakhale wina aliyense amene akanathandiza Israeli. 27Pakuti Yehova anali asananene zofafaniza ufumu wa Israeli pa dziko lapansi, Iye anawapulumutsa kudzera mʼdzanja la Yeroboamu mwana wa Yowasi.

28Ntchito zina za Yeroboamu ndi zonse zimene anachita, za kupambana kwake pa nkhondo, za mmene anagonjetsera Damasiko ndi Hamati, imene inali mizinda ya Yuda, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli? 29Yeroboamu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi mafumu a Israeli. Ndipo Zekariya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.