列王紀上 11 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

列王紀上 11:1-43

所羅門背棄上帝

1除了埃及公主以外,所羅門王還寵愛許多外邦女子,有摩押人、亞捫人、以東人、西頓人和人。 2耶和華曾告訴以色列人不可跟這些外族人通婚,免得受引誘去隨從他們的神明,所羅門卻迷戀這些女子。 3他有七百個妻子,都是外國的公主,還有三百個妃嬪。這些女子使他的心背棄耶和華。 4所羅門年老的時候,他的嬪妃誘惑他的心去追隨別的神明。他沒有像他父親大衛那樣忠心順服他的上帝耶和華。 5所羅門西頓人的女神亞斯她錄亞捫人的可憎神明米勒公6他做了耶和華視為惡的事,沒有像他父親大衛那樣忠心順服耶和華。 7耶路撒冷東面的山上,所羅門摩押人可憎的神明基抹亞捫人可憎的神明摩洛修建邱壇。 8他又為所有的外邦妃嬪修建邱壇,供她們向自己的神明燒香獻祭。

9-10所羅門背棄了曾兩次向他顯現的以色列的上帝耶和華,違背耶和華的命令去隨從別的神明。所以,耶和華向他發怒, 11說:「你既然違背我的命令,不遵守我的約和律例,我必奪走你的國,將它賜給你的一個臣僕。 12然而,因你父大衛的緣故,我不會在你有生之年這樣做,我要從你兒子手中把國奪走。 13但我不會全部奪走,為了我僕人大衛和我揀選的耶路撒冷,我會留下一個支派給你兒子。」

所羅門的敵人

14耶和華使以東王的後裔哈達興起,與所羅門為敵。 15從前大衛征討以東,元帥約押前去埋葬陣亡的人,將以東的男子都殺了。 16他率領以色列人在那裡住了六個月,直到殺光了以東的男子。 17那時,哈達年紀還小,他和他父親的幾個以東臣僕一起逃往埃及18他們從米甸逃到巴蘭,在那裡招聚了一些人,然後又逃到埃及去見埃及王法老。法老賜他糧食、房屋和田地。 19法老非常喜歡哈達,將王后答比妮的妹妹許配給他。 20他們生了一個兒子,取名基努拔,由王后在宮中撫養,跟王子們在一起。 21後來,哈達知道大衛已與祖先同眠,約押元帥也死了,就求法老准他回國。 22法老問他:「你為什麼要回國呢?你在我這裡還缺什麼嗎?」哈達答道:「什麼都不缺,但還是求王准我回國。」 23上帝又使以利亞大的兒子利遜興起,與所羅門為敵。這人從他主人瑣巴哈大底謝身邊逃走後, 24招聚了一群匪徒,自己做頭目。大衛征服瑣巴人後,他又前往大馬士革,在那裡做王。 25所羅門活著的時候,哈達利遜不斷為患。利遜統治亞蘭,他憎恨以色列人。

耶羅波安叛變

26所羅門的一個臣僕耶羅波安也叛變了。他是以法蓮支派洗利達尼八的兒子,母親洗魯阿是個寡婦。 27以下是他反叛所羅門的緣由:

當年所羅門建造米羅堡,修補大衛城的城牆時, 28發現年輕的耶羅波安勤奮能幹,就提拔他監管約瑟家族的一切工程。

29有一次,耶羅波安出了耶路撒冷,在路上遇見身披新衣的示羅亞希雅先知。當時野外只有他們二人。 30亞希雅將身上的新衣撕作十二片, 31耶羅波安說:「你可以拿十片。以色列的上帝耶和華說,『我必奪走所羅門的國,把十個支派賜給你。 32然而,為了我僕人大衛和我在以色列眾支派中揀選的耶路撒冷城,我會留下一個支派給所羅門33所羅門背棄了我,去祭拜西頓人的女神亞斯她錄摩押的神明基抹亞捫人的神明米勒公。他沒有遵行我的道,沒有做我視為正的事,也不像他父親大衛那樣遵守我的律例和典章。 34然而,我不會奪走他整個國,我會讓所羅門終生為王,因為我所揀選的僕人大衛遵守我的誡命和律法。 35我必從他兒子手中把國奪走,將十個支派賜給你, 36只給他兒子留下一個支派,好使我僕人大衛有後裔留在我選為居所的耶路撒冷城。 37我要讓你做王,使你如願地統治以色列38若你像我僕人大衛一樣聽從我的一切吩咐,遵行我的道,做我視為正的事,遵守我的律例誡命,我就與你同在,鞏固你的王朝,像鞏固大衛的王朝一樣,使你統治以色列39所羅門的所作所為,我必讓大衛的後裔遭難,但不會永遠如此。』」

40所羅門想殺耶羅波安,他就逃到埃及投奔埃及示撒,在那裡一直住到所羅門過世。

41所羅門的其他事蹟、作為和智慧都記在所羅門記上了。 42所羅門耶路撒冷統治以色列四十年, 43他與祖先同眠後葬在他父親大衛的城裡。他兒子羅波安繼位。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mafumu 11:1-43

Akazi a Solomoni

1Komatu Mfumu Solomoni anakonda akazi ambiri achilendo ndipo kuwonjezera pa mwana wamkazi wa Farao, analinso ndi akazi a mitundu iyi: Amowabu, Aamoni, Aedomu, Asidoni, ndi Ahiti. 2Akazi amenewa anali ochokera ku mitundu ija imene Yehova anawuza Aisraeli kuti, “Simuyenera kudzakwatirana nawo amenewa, chifukwa ndithu, amenewa adzatembenuza mitima yanu kuti mutsatire milungu yawo.” Komabe Solomoni anawakonda kwambiri akazi amenewa. 3Iye anali ndi akazi 700 ochokera ku mabanja achifumu ndi azikazi 300 ndipo akaziwo anamusocheretsa. 4Solomoni atakalamba, akazi akewo anakopa mtima wake kuti atsatire milungu ina, ndipo sanatsatire Yehova Mulungu wake ndi mtima wodzipereka, monga unalili mtima wa Davide abambo ake. 5Pakuti iye ankapembedza Asitoreti, mulungu wamkazi wa Asidoni, ndiponso Moleki mulungu wonyansa wa Aamoni. 6Kotero Solomoni anachita zoyipa pamaso pa Yehova. Sanatsatire Yehova kwathunthu monga anachitira Davide abambo ake.

7Pa phiri la kummawa kwa Yerusalemu, anamanga malo opembedzerapo Kemosi, mulungu wonyansa wa Mowabu, ndiponso malo a Moleki, mulungu wonyansa wa Aamoni. 8Iye anamangiranso malo oterewa akazi ake onse achilendo, amene amafukiza lubani ndi kumapereka nsembe kwa milungu yawo.

9Choncho Yehova anakwiyira Solomoni chifukwa mtima wake unatembenuka kuchoka kwa Yehova Mulungu wa Israeli, amene anamuonekera kawiri konse. 10Ngakhale kuti Yehova anamuletsa Solomoni kutsatira milungu ina, iyeyo sanamvere lamulo la Yehova. 11Pamenepo Yehova anati kwa Solomoni, “Popeza mtima wako ndi wotere ndipo sunasunge pangano langa ndi malamulo anga amene ndinakuwuza, ndithudi, Ine ndidzawugawa ufumuwu kuwuchotsa kwa iwe ndi kuwupereka kwa mmodzi mwa atumiki ako. 12Koma chifukwa cha Davide abambo ako, sindidzachita zimenezi iwe uli moyo. Ndidzawugawa mʼdzanja la mwana wako. 13Komabe sindidzamulanda ufumu wonse, koma ndidzamusiyira fuko limodzi chifukwa cha mtumiki wanga Davide ndiponso chifukwa cha Yerusalemu, mzinda umene ndinawusankha.”

Adani a Solomoni

14Ndipo Yehova anamuutsira Solomoni mdani, Hadadi Mwedomu, wochokera ku banja laufumu ku Edomu. 15Kale pamene Davide ankachita nkhondo ndi Aedomu, Yowabu mkulu wa ankhondo, amene anapita kukakwirira Aisraeli akufa, anakantha amuna onse ku Edomu. 16Yowabu ndi Aisraeli onse anakhala kumeneko miyezi isanu ndi umodzi mpaka anawononga amuna onse a ku Edomu. 17Koma Hadadi akanali mwana anathawira ku Igupto pamodzi ndi akuluakulu ena a ku Edomu amene ankatumikira abambo ake. 18Iwo ananyamuka ku Midiya ndi kupita ku Parani. Ndipo anatenga amuna ena ku Paraniko, napita nawo ku Igupto, kwa Farao mfumu ya Igupto, amene anamupatsa nyumba, malo ndiponso chakudya.

19Farao anamukomera mtima Hadadi ndipo anamupatsa mkazi amene anali mngʼono wake wa Mfumukazi Tahipenesi. 20Mngʼono wake wa Tahipenesi anabereka mwana wamwamuna ndipo anamutcha Genubati, amene analeredwa mʼnyumba yaufumu ndi Tahipenesi. Genubatiyo ankakhala limodzi ndi ana a Farao.

21Ali ku Iguptoko, Hadadi anamva kuti Davide ndi Yowabu anamwalira. Pamenepo Hadadi anati kwa Farao, “Loleni ndichoke kuti ndibwerere ku dziko la kwathu.”

22Farao anafunsa kuti, “Kodi ukusowa chiyani kuno kuti ufune kubwerera ku dziko la kwanu?”

Hadadi anayankha kuti, “Palibe chimene ndikusowa, koma loleni kuti ndichoke!”

23Ndipo Mulungu anawutsira Solomoni mdani wina, Rezoni mwana wa Eliada, amene anali atathawa mbuye wake, Hadadezeri mfumu ya ku Zoba. 24Iye anasonkhanitsa anthu ndipo anali mtsogoleri wa anthu owukira pamene Davide anapha ankhondo a ku Zoba. Anthu owukirawa anapita ku Damasiko, nakakhala kumeneko ndi kuyamba kulamulira. 25Rezoni anali mdani wa Israeli pa masiku onse a Solomoni, kuwonjezera pa mavuto amene ankabweretsa Hadadi. Kotero Rezoni ankalamulira ku Aramu ndipo ankadana ndi Israeli.

Yeroboamu Awukira Solomoni

26Yeroboamu, mwana wa Nebati anawukiranso mfumu. Iye anali mmodzi mwa akuluakulu a Solomoni wa fuko la Efereimu, wa ku Zeredi, ndipo amayi ake anali Zeruya, mkazi wamasiye.

27Nkhani ya kuwukira kwa Yeroboamu inali yotere: Solomoni anamanga malo a chitetezo a Milo ndipo anakonza khoma logumuka la mzinda wa Davide, abambo ake. 28Tsono Yeroboamu anali munthu wamphamvu kwambiri ndipo Solomoni ataona kuti mnyamatayo amadziwa kugwira ntchito bwino, anamuyika kukhala woyangʼanira anthu a ntchito onse a nyumba ya Yosefe.

29Tsiku lina Yeroboamu ali pa ulendo kuchokera ku Yerusalemu, anakumana ndi mneneri Ahiya pa msewu, ndipo Ahiyayo anali atavala mwinjiro watsopano. Awiriwo anali okha kuthengoko, 30ndipo Ahiya anagwira mwinjiro watsopano umene anavala ndi kuwungʼamba zidutswa 12. 31Tsono iye anati kwa Yeroboamu, “Tenga zidutswa khumi, pakuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Taona, Ine ndidzachotsa ufumu mʼdzanja la Solomoni ndipo ndidzakupatsa iwe mafuko khumi. 32Koma chifukwa cha mtumiki wanga Davide ndiponso mzinda wa Yerusalemu, umene ndinawusankha pakati pa mafuko a Israeli, iye adzakhala ndi fuko limodzi lokha. 33Ndidzachita zimenezi chifukwa wandisiya Ine ndi kupembedza Asitoreti mulungu wamkazi wa Asidoni, Kemosi mulungu wa Amowabu ndiponso Moleki mulungu wa Aamoni, ndipo sanayende mʼnjira yanga, kapena kusunga mawu anga ndi malamulo anga monga anachitira Davide abambo ake.

34“ ‘Koma sindidzalanda ufumu wonse mʼdzanja la Solomoni. Ine ndamuyika kukhala wolamulira masiku onse a moyo wake chifukwa cha mtumiki wanga Davide, amene ndinamusankha ndiponso amene anamvera malamulo anga ndi mawu anga. 35Ndidzalanda ufumu mʼdzanja la mwana wake ndipo ndidzakupatsa iwe mafuko khumi. 36Ndidzapereka fuko limodzi kwa mwana wake ndi cholinga choti Davide mtumiki wanga adzakhale nyale nthawi zonse pamaso panga mu Yerusalemu, mzinda umene ndinawusankha kuyikamo Dzina langa. 37Koma kunena za iwe, ndidzakutenga ndipo udzalamulira chilichonse chimene mtima wako ukukhumba; udzakhala mfumu ya Israeli. 38Ngati udzamvera zonse zimene ndidzakulamula ndi kuyenda mʼnjira yanga ndi kuchita zabwino pamaso panga, posunga malamulo anga ndi mawu anga monga anachitira Davide mtumiki wanga, Ine ndidzakhala nawe. Ndidzakupatsa ufumu umene udzakhala wokhazikika monga ndinamupatsira Davide, ndipo Ine ndidzakupatsa Israeli. 39Ine ndidzalanga zidzukulu za Davide chifukwa cha zimenezi, koma osati kwamuyaya.’ ”

40Solomoni anafunitsitsa kupha Yeroboamu, koma Yeroboamu anathawira ku Igupto, kwa Sisaki mfumu ya Igupto ndipo anakhala kumeneko mpaka Solomoni atamwalira.

Kumwalira kwa Solomoni

41Ntchito zina za Solomoni, zonse zomwe anachita komanso za nzeru zake, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya Solomoni? 42Solomoni analamulira Aisraeli onse mu Yerusalemu kwa zaka makumi anayi. 43Ndipo anagona ndi makolo ake nayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide abambo ake. Ndipo Rehobowamu mwana wake analowa ufumu mʼmalo ake.