出埃及記 5 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

出埃及記 5:1-23

摩西和亞倫見法老

1之後,摩西亞倫去見法老,對他說:「以色列的上帝耶和華說,『放我的子民走,讓他們到曠野去為我守節期。』」 2法老說:「耶和華是誰?我憑什麼要聽從祂,放走以色列人?我不認識祂,也不會讓以色列人離開!」 3摩西亞倫說:「希伯來人的上帝向我們顯現了。求你容我們走三天的路程,到曠野去向我們的上帝耶和華獻祭,請你讓我們去吧,免得祂用刀劍、瘟疫來攻擊我們。」 4埃及王說:「摩西亞倫,你們竟敢煽動百姓曠工!快回去工作!」 5法老又說:「這地方的以色列人如此眾多,你竟叫他們停止工作!」 6當天,法老就對埃及監工和以色列人的工頭下令: 7「從今天開始,不許再供應草給他們製磚,叫他們自己去撿, 8但上交的磚的數量要和往常一樣,一塊也不可少。因為他們懶惰,所以才嚷著要去給他們的上帝獻祭。 9你們要加重他們的工作,他們就無暇再聽那些蠱惑人心的話了!」

10於是,那些監工和工頭就出來向百姓宣佈:「法老下令不再供應草給你們製磚。 11你們要自己設法去找,但上交的磚一塊也不能少。」 12百姓只好在埃及全國收集碎禾稭當草用。 13監工催逼他們說:「你們要完成每天規定的數目,像從前有草時一樣。」 14他們又鞭打以色列人的工頭,說:「你們這兩天為什麼沒有像從前一樣完成規定的磚數?」

15以色列人的工頭來見法老,向他哀求說:「你為什麼要這樣對待僕人們? 16監工不給僕人們草,卻命令我們做磚,還打我們,其實是你百姓的錯。」 17法老說:「你們是懶惰的人,懶惰的人!所以才嚷著要去給耶和華獻祭。 18回去繼續工作!我不再供應草給你們,但磚要如數交齊。」 19以色列人的工頭聽見每天做的磚數不可減少,就知道情況不妙。 20他們從法老那裡出來的時候,遇見摩西亞倫站在外面等候, 21便埋怨二人說:「願耶和華鑒察、懲罰你們!你們使我們在法老和他的臣僕面前有了臭名,使他們有藉口來殺我們。」

22摩西回到耶和華那裡說:「主啊!你為什麼這樣苦待你的子民呢?為什麼要派我去呢? 23自從我去法老那裡奉你的名發言後,他更加虐待你的子民,你並沒有拯救他們。」

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 5:1-23

Mose Akumana ndi Farao

1Zitachitika izi, Mose ndi Aaroni anapita kwa Farao ndipo anati, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Aloleni anthu anga apite, kuti akachite chikondwerero cha Ine mʼchipululu.’ ”

2Koma Farao anati, “Yehova ndani kuti ine ndimumvere ndi kulola Aisraeli kuti apite? Ine Yehova sindikumudziwa ndipo sindilola kuti Aisraeli apite.”

3Ndipo iwo anati, “Mulungu wa Ahebri anakumana nafe. Chonde tiloleni tipite ulendo wa masiku atatu ku chipululu kuti tikapereke nsembe kwa Yehova Mulungu wathu, ngati sititero iye adzatipweteka ndi miliri kapena lupanga.”

4Koma mfumu ya Igupto inati, “Mose ndi Aaroni, chifukwa chiyani mukuchititsa anthuwa kuti asagwire ntchito zawo? Bwererani ku ntchito zanu!” 5Ndiponso Farao anati, “Taonani, anthuwa mʼdziko muno alipo ochuluka, ndipo inu mukuwaletsa kugwira ntchito.”

Njerwa Zopanda Udzu

6Pa tsiku lomwelo Farao analamulira akapitawo a thangata ndi anzawo a Chiisraeli amene ankayangʼanira anthu kuti 7“Inu musawapatsenso udzu wopangira njerwa monga mumachitira kale, iwo azipita ndi kukatenga udzu wawo. 8Koma musawachepetsere chiwerengero cha njerwa chomwe munawalamulira kale kuti aziwumba. Iwowa ndi aulesi. Nʼchifukwa chake akulira kuti, ‘Tiloleni tipite tikapereke nsembe kwa Mulungu wathu.’ 9Muwakhawulitse ndi ntchito anthu amenewa kuti azitanganidwa, asakhale ndi mpata omvera zabodza.”

10Choncho akapitawo a thangata ndi anzawo a Chiisraeli amene ankayangʼanira anthu anapita kwa anthu aja nati, “ ‘Farao akuti sadzakupatsaninso udzu. 11Mʼmalo mwake mupite mukadzimwetere udzu kulikonse kumene mungawupeze. Komabe ntchito yanu sichepetsedwa.’ ” 12Kotero anthuwo anamwazikana mʼdziko lonse la Igupto kukamweta udzu. 13Akapitawo a thangata aja anawafulumiza anthu aja nati, “Malizani kugwira ntchito yanu ya tsiku ndi tsiku monga mmene zinalili pamene munkapatsidwa udzu.” 14Akapitawo a thangata a Farao ankawamenya oyangʼanira anzawo a Chiisraeli aja nawapanikiza kuti, “Chifukwa chiyani lero simunawumbe chiwerengero chovomerezeka cha njerwa monga chakale chija?”

15Pamenepo oyangʼanira anzawo a Chiisraeli aja anapita kukadandaula kwa Farao kuti, “Chifukwa chiyani mwachitira antchito anu zotere? 16Antchito anu sakupatsidwa udzu, komabe akutiwuza kuti, ‘Umbani njerwa!’ Antchito anu akumenyedwa, koma cholakwa sichili ndi anthu anu.”

17Farao anati, “Ulesi, inu ndinu alesi! Nʼchifukwa chake mukumanena kuti, ‘Mutilole tipite kukapereka nsembe kwa Yehova.’ 18Pitani tsopano kuntchito. Simudzapatsidwanso udzu komabe muyenera kuwumba muyeso wanu wovomerezeka wa njerwa.”

19Oyangʼanira anzawo a Chiisraeli anazindikira kuti ali pa mavuto pamene anawuzidwa kuti, “Musachepetse chiwerengero cha njerwa chimene muyenera kuwumba tsiku lililonse.” 20Atachoka pamaso pa Farao, anakumana ndi Mose ndi Aaroni akuwadikira, 21ndipo iwo anati, “Yehova akupenyeni ndi kukuweruzani popeza mwachititsa Farao ndi nduna zake kuti anyansidwe nafe ndipo mwayika lupanga mʼmanja mwawo kuti atiphe.”

Mulungu Alonjeza Chipulumutso

22Mose anabwerera kwa Yehova ndipo anati, “Chonde Ambuye, chifukwa chiyani mukuzunza anthu anu? Kodi munanditumira zimenezi? 23Chipitireni changa kwa Farao kukamuyankhula mʼdzina lanu, iye wakhala akuzunza anthuwa, ndipo inu simunawapulumutse konse anthu anu.”