出埃及記 2 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

出埃及記 2:1-25

摩西出生

1有一個利未族人跟他同族的女子結婚。 2那女子懷孕,生了一個男嬰。她看見孩子可愛,就把他藏了三個月。 3後來無法再藏下去,她就拿來一個蒲草籃子,外面塗上防水的瀝青和柏油,然後把嬰兒放在裡面,又把籃子放在尼羅河邊的蘆葦叢中。 4嬰兒的姐姐遠遠地站著,要看看她的弟弟究竟會怎樣。

5這時,法老的女兒來到河邊沐浴,宮女們在河邊行走。公主發現了蘆葦叢中的籃子,便吩咐一個婢女去把它取來。 6公主打開一看,原來是一個男嬰。公主看見孩子在哭,就可憐他,說:「他是希伯來人的孩子。」 7嬰兒的姐姐對公主說:「我去找一個希伯來婦女當奶媽,為你哺養他好嗎?」 8公主回答說:「好!」那女孩就跑去把嬰孩的母親帶來。 9公主對那婦女說:「你把孩子抱去,替我哺養他,我會給你工錢。」她便把孩子抱去哺養。 10孩子漸漸長大,她便把他帶到公主那裡,孩子就做了公主的兒子。公主給孩子取名叫摩西,意思是「我把他從水中拉了上來」。

11後來,摩西長大了,他去看望做苦工的希伯來同胞,看見一個埃及人在毆打他的一個希伯來同胞。 12他左右觀望,見四下無人,便下手殺了那埃及人,把屍體埋藏在沙地裡。 13第二天,他又出去,看見兩個希伯來人在打架,便過去對理虧的人說:「你為什麼打自己的同胞呢?」 14那人說:「你以為你是誰啊?誰立你做我們的首領和審判官?難道你要殺我,像殺那個埃及人一樣嗎?」摩西聽了,害怕起來,心想:「我做的事一定被人知道了。」 15法老聽說這件事後,便想殺死摩西摩西為了躲避法老,就逃到米甸居住。一天他坐在一口井旁, 16米甸祭司的七個女兒來打水,要把水倒進槽裡飲她們父親的羊。 17這時,來了另外一群牧人要把她們趕走。摩西便起來幫助她們,打水飲她們的羊群。 18她們回到父親流珥2·18 流珥」又名「葉忒羅」。那裡,父親問她們:「你們今天怎麼這麼快就回來了?」 19她們答道:「有一個埃及人救我們免遭牧人的欺負,還幫我們打水飲羊群。」 20他又問女兒們:「現在那人在哪裡?你們怎麼可以丟下他不管呢?去請他來吃點東西。」 21後來,摩西同意住在那人家裡。那人把女兒西坡拉許配給他。 22後來,西坡拉生了一個兒子,摩西給他取名叫革舜,意思是「我成了在異鄉寄居的人」。

23過了多年,埃及王死了。以色列人受盡奴役,就哀歎呼求,聲音傳到上帝那裡。 24上帝聽見他們的哀聲,顧念從前跟亞伯拉罕以撒雅各所立的約, 25就垂顧他們,體恤他們。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 2:1-25

Kubadwa kwa Mose

1Ndipo munthu wina wa fuko la Levi anakwatira mkazi wa fuko lomwelo. 2Mkaziyo anatenga pathupi ndipo anabereka mwana wamwamuna. Ataona kuti mwanayo anali wokongola, anamubisa kwa miyezi itatu. 3Koma mwanayo atafika pa msinkhu woti sakanathanso kubisidwa, amayi ake anatenga kadengu kopangidwa ndi bango nakamata phula. Kenaka anayika mwanayo mʼmenemo ndi kukamuyika pa mabango mu mtsinje wa Nailo. 4Mlongo wake wa mwanayo anayima pataliko kuti aone chimene chidzamuchitikira mwanayo.

5Mwana wamkazi wa Farao anapita ku mtsinje wa Nailo kukasamba ndipo adzakazi ake ankayenda mʼmbali mwa mtsinjewo. Tsono mwana wa Farao uja anaona kadenguko pakati pa mabango ndipo anatuma mdzakazi wake kuti akakatenge. 6Iye atavundukula anaona mwana wamwamuna akungolira. Iye anamva naye chisoni mwana uja, nati, “Ameneyu ndi mmodzi mwa ana a Chihebri.”

7Kenaka mlongo wake wa mwanayo anafunsa mwana wa Farao kuti, “Ndingapite kukakupezerani mmodzi mwa amayi a Chihebri kuti azikakulererani mwanayu?”

8Iye anayankha kuti, “Inde, pita.” Ndipo mtsikanayo anapita nakayitana amayi a mwanayo. 9Mwana wa Farao anati, “Tengani mwanayu mukandilerere, ndidzakulipirani.” Mayiyo anatenga mwanayo kukamulera. 10Mwanayo atakula anakamupereka kwa mwana wa Farao ndipo anakhala mwana wake. Iye anamutcha dzina lake Mose, popeza anati, “Ndinamuvuwula mʼmadzi.”

Mose Athawira ku Midiyani

11Tsiku lina, Mose atakula, anapita kumene kunali anthu a mtundu wake ndipo anawaona akugwira ntchito yowawa. Iye anaona Mwigupto akumenya Mhebri, mmodzi mwa anthu a mtundu wake. 12Atayangʼana uku ndi uku, naona kuti panalibe wina aliyense, Mose anamupha Mwiguptoyo ndipo anamukwirira mu mchenga. 13Mmawa mwake Mose anapita ndipo anaona anthu awiri a Chihebri akumenyana. Iye anafunsa amene anali wolakwa kuti, “Chifukwa chiyani ukumenya Mhebri mnzako?”

14Munthu uja anati, “Kodi ndani anakuyika kuti ukhale wotilamulira ndi wotiweruza? Kodi ukufuna kundipha monga momwe unaphera Mwigupto uja?” Mose anachita mantha ndipo anati mu mtima mwake, “Chimene ndinachita chija chadziwika.”

15Farao atamva zimenezi anafuna kuti aphe Mose, koma Mose anathawa ndipo anapita kukakhala ku Midiyani. Ali kumeneko, tsiku lina anakhala pansi pafupi ndi chitsime. 16Wansembe wa ku Midiyaniko anali ndi ana aakazi asanu ndi awiri. Iwowa anabwera kudzatunga madzi ndi kudzaza mu zomwera kuti amwetse nkhosa za abambo awo. 17Koma kunabwera abusa ena amene anathamangitsa atsikana aja. Ndiye Mose anayimirira nawathandiza atsikana aja ndi kumwetsa nkhosa zawo.

18Atsikana aja atabwerera kwa abambo awo Reueli, iye anawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani lero mwabwera msanga?”

19Atsikanawo anayankha kuti, “Mwigupto wina ndiye watilanditsa kwa abusa. Ndiponso anatitungira madzi ndi kumwetsa ziweto zathu.”

20Tsono Reueli anafunsa ana ake kuti, “Ndiye ali kuti munthuyo? Chifukwa chiyani mwamusiya? Kamuyitaneni kuti adzadye.”

21Mose anavomera kukhala ndi Reueli, ndipo anamupatsa Zipora kuti akhale mkazi wake. 22Zipora anabereka mwana wa mwamuna amene Mose anamutcha Geresomu, popeza anati, “Ndakhala mlendo mʼdziko la eni.”

23Nthawi yonseyo nʼkuti ana a Israeli akulira chifukwa cha ukapolo wawo uja. Iwo anafuwula kupempha thandizo, ndipo kulira kwawoko kunafika kwa Mulungu. 24Mulungu anamva kubuwula kwawo ndipo anakumbukira pangano lake ndi Abrahamu, Isake ndi Yakobo. 25Mulungu ataona Aisraeli aja ndi masautso awo, Iye anawamvera chifundo.