使徒行傳 14 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

使徒行傳 14:1-28

在以哥念傳道

1保羅巴拿巴一同進入以哥念猶太會堂講道,許多猶太人和希臘人信了耶穌。 2但那些頑梗不信的猶太人卻慫恿外族人敵視信徒。 3二人在那裡逗留了好些日子,靠著主勇敢地傳道。主賜給他們行神蹟奇事的能力,為祂的恩典之道做見證。 4城裡的居民分成了兩派,有些附和猶太人,有些支持使徒。

5當時,有些外族人、猶太人及其官長企圖惡待使徒,用石頭打他們。 6保羅巴拿巴得知後,就逃往呂高尼路司得特庇二城並周圍的地區, 7在那裡繼續傳揚福音。

在路司得和特庇傳福音

8路司得城裡坐著一個天生雙腳無力、不能走路的瘸子。 9他也聽保羅講道。保羅定睛看他,見這個人有信心,可以得醫治, 10就高聲對他說:「起來,兩腳站直!」那人就跳了起來,開始行走。 11周圍的人看見保羅所行的,就用呂高尼話大聲說:「神明化成人形下凡了!」 12於是,他們稱巴拿巴希臘天神宙斯,又因為保羅是主要的發言人,就稱他為希耳米14·12 希臘神話中天神宙斯是最大的神,希耳米則是為眾神傳遞信息的使者——「傳諭之神」。13城外宙斯廟的祭司也牽著牛、拿著花環來到城門口,要和眾人一同向使徒獻祭。

14巴拿巴保羅見此情形,就撕裂衣服,衝進人群中,大聲喊著說: 15「各位,你們為什麼這樣做?我們和你們一樣只是凡人!我們來這裡是要向你們傳福音,叫你們離棄這些虛妄的事,轉向那創造天、地、海和其中萬物的永活上帝。 16在以往的世代,祂雖然容許萬國各行其道, 17卻從未停止用美善的事證實自己的存在。祂常施恩惠,降下甘霖,賞賜豐年,又叫你們衣食飽足,滿心喜樂。」

18保羅巴拿巴說了這些話,才勉強制止住向他們獻祭的人群。 19有些猶太人從安提阿以哥念來煽動民眾,他們用石頭打保羅,以為他死了,就把他拖到城外。 20當門徒圍過來看他的時候,他站了起來,走回城裡。第二天,保羅巴拿巴前往特庇

返回安提阿

21他們向那裡的人傳福音,有很多人作了門徒。然後,他們又回到路司得以哥念安提阿22堅固各地門徒的信心,鼓勵他們要持守信仰,並且說:「我們在進入上帝國的道路上必經歷許多苦難。」 23二人又為每個教會選立長老,禁食禱告,把他們交託給所信靠的主。

24後來,二人又經過彼西底,來到旁非利亞25別加講道,然後下到亞大利26從那裡乘船回安提阿。當初就是在安提阿,他們被交託在上帝的恩手中去傳道,如今工作已經完成了。

27他們到達之後,就召集教會的人,報告上帝藉著他們所做的一切事,以及上帝如何給外族人開了信仰之門。 28之後,二人和門徒同住了很久。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Machitidwe a Atumwi 14:1-28

Ku Ikoniya

1Ku Ikoniya, Paulo ndi Barnaba analowanso mʼsunagoge ya Ayuda. Kumeneko iwo anaphunzitsa momveka bwino kotero kuti anthu ambiri Achiyuda ndi anthu a mitundu ina anakhulupirira. 2Koma Ayuda amene anakana kukhulupirira anawutsa anthu a mitundu ina nawononga maganizo awo kutsutsana ndi abale. 3Ndipo Paulo ndi Barnaba anakhala kumeneko nthawi yayitali, nalalikira molimba mtima za Ambuye amene anawapatsa mphamvu yochitira zozizwitsa ndi zizindikiro zodabwitsa pochitira umboni mawu a chisomo. 4Anthu a mu mzindamo anagawikana; ena anali mbali ya Ayuda, ena mbali ya atumwi. 5Pamenepo anthu a mitundu ina ndi Ayuda, pamodzi ndi atsogoleri awo anakonza chiwembu choti azunze atumwiwo ndi kuwagenda ndi miyala. 6Koma atazindikira zimenezi, anathawira ku Lusitra ndi Derbe, mizinda ya ku Lukaoniya, ndiponso ku dziko lozungulira mizindayo, 7kumene anapitiriza kulalikira Uthenga Wabwino.

Ku Lusitra ndi ku Derbe

8Ku Lusitra kunali munthu wolumala miyendo, amene sanayendepo chibadwire chake. 9Iyeyu, amamvetsera pamene Paulo amayankhula. Paulo anamuyangʼanitsitsa ndipo anaona kuti anali ndi chikhulupiriro choti achiritsidwe nacho. 10Ndipo Paulo anamuyitana mofuwula nati, “Imirira!” Atamva zimenezi, munthuyo anayimirira, nayamba kuyenda.

11Gulu la anthu litaona zimene Paulo anachitazi, linafuwula mʼChilukaoniya kuti, “Milungu yatitsikira yooneka ngati anthu!” 12Barnaba anamutcha Zeusi ndipo Paulo anamutcha Herimesi chifukwa ndiye amatsogolera kuyankhula. 13Wansembe wa Zeusi amene nyumba yopembedzera Zeusiyo inali kunja pafupi ndi mzindawo, anabweretsa ngʼombe yayimuna yovekedwa nkhata za maluwa pa chipata cha mzindawo chifukwa iyeyo pamodzi ndi anthu ena onse aja amafuna kudzipereka nsembe kwa Paulo ndi Barnaba.

14Koma Barnaba ndi Paulo atamva zimenezi, anangʼamba zovala zawo, nathamangira pakati pa gulu la anthuwo, akufuwula kuti, 15“Anthu inu, bwanji mukuchita zimenezi? Ifenso ndife anthu monga inu nomwe. Ife takubweretserani Uthenga Wabwino, kuti musiye zinthu zachabezi ndi kutsata Mulungu wamoyo, amene analenga kumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zimene zili mʼmenemo. 16Kale Iye analola anthu a mitundu ina yonse kutsata njira zawozawo. 17Komabe wakhala akudzichitira yekha umboni: Iye amaonetsa kukoma mtima kwake pogwetsa mvula kuchokera kumwamba ndi zipatso pa nyengo yake. Amakupatsani chakudya chambiri ndipo amadzaza mitima yanu ndi chimwemwe.” 18Ngakhale ndi mawu awa, anavutika kuletsa gulu la anthu kuti asapereke nsembe kwa iwo.

19Kenaka kunabwera Ayuda ena kuchokera ku Antiokeya ndi Ikoniya nakopa gulu la anthu lija. Iwo anamugenda miyala Paulo namukokera kunja kwa mzindawo, kuganiza kuti wafa. 20Koma ophunzira atamuzungulira, Pauloyo anayimirira nalowanso mu mzindawo. Mmawa mwake iye ndi Barnaba anachoka ndi kupita ku Derbe.

Paulo ndi Barnaba Abwerera ku Antiokeya wa ku Siriya

21Iwo analalikira Uthenga Wabwino mu mzindawo ndipo anthu ambiri anatembenuka mtima ndi kukhala ophunzira. Kenaka anabwerera ku Lusitra, ku Ikoniya ndi ku Antiokeya. 22Kumeneko analimbikitsa mitima ya ophunzira ndi kuwapatsa mphamvu kuti akhalebe woona mʼchikhulupiriro. Iwo anati, “Ife tiyenera kudutsa mʼmasautso ambiri kuti tikalowe mu ufumu wa Mulungu.” 23Paulo ndi Barnaba anasankha akulu ampingo pa mpingo uliwonse, ndipo atapemphera ndi kusala kudya anawapereka kwa Ambuye amene anamukhulupirira. 24Atadutsa Pisidiya, anafika ku Pamfiliya. 25Atalalikira Mawu ku Perga, anapita ku Ataliya.

26Ku Ataliyako, anakwera sitima ya pamadzi kubwerera ku Antiokeya kumene anayitanidwa mwachisomo cha Mulungu kuti agwire ntchito imene tsopano anali atayitsiriza. 27Atangofika ku Antiokeya, anasonkhanitsa pamodzi mpingo ndipo anafotokoza zonse zimene Mulungu anachita kudzera mwa iwo ndiponso mmene Iye anatsekulira a mitundu ina njira ya chikhulupiriro. 28Ndipo anakhala kumeneko ndi ophunzira nthawi yayitali.