何西阿書 13 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

何西阿書 13:1-16

對以色列的最後審判

1以法蓮支派在以色列地位崇高,

他們一開口,人都恐懼顫抖。

但他們卻祭拜巴力,自招滅亡。

2如今他們作惡日甚,

憑藉自己的聰明用銀子鑄造神像,

但這不過是匠人之作。

人們議論他們說:

「那些獻祭的人竟親吻牛犢偶像!」

3他們像晨霧,如轉瞬即逝的朝露,

像麥場上飛旋而去的糠秕,

又像窗口冒出的輕煙。

4耶和華說:

「自從你們離開埃及以來,

我就是你們的上帝耶和華。

除我以外,你們不可有別的神明;

在我以外,你們也沒有別的救主。

5我曾在乾旱的曠野照顧你們,

6但你們吃得飽足以後,

就心高氣傲,忘記了我。

7因此,我要像獅子攻擊你們,

如豹子潛伏在路旁;

8我要像一頭失了幼崽的母熊衝向你們,

撕裂你們的胸膛;

我要像母獅吞噬你們,

像兇猛的野獸撕碎你們。

9以色列啊,你要滅亡了,

因為你抵擋我,抵擋你的幫助者。

10你曾求我為你設立君王和首領,

現在拯救你的君王在哪裡呢?

在各城管理你的首領在哪裡呢?

11我在憤怒中賜給你君王,

也在憤怒中廢黜他們。

12以法蓮的過犯已被記錄在冊,

他的罪惡已被儲存入庫。

13臨產的陣痛要臨到他,

但他是毫無智慧的孩子,

分娩之時卻不離開母腹。

14我要把他們從陰間的權勢下贖回嗎?

我要救他們脫離死亡嗎?

死亡啊,你去降災給他們吧!

陰間啊,你去毀滅他們吧!

我不會再憐憫他們。

15儘管以法蓮在眾弟兄中最強盛,

但炙熱的東風——耶和華的風要從沙漠颳來,

使清泉枯竭,水井乾涸。

他儲藏的一切珍寶都要被擄去。

16撒瑪利亞人背叛了他們的上帝,

要擔當自己的罪過。

他們將喪身刀下,

他們的孩子要被摔死,

孕婦要被剖腹。」

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hoseya 13:1-16

Mkwiyo wa Yehova pa Israeli

1Kale Efereimu ankati akayankhula, anthu ankanjenjemera;

anali wolemekezeka mu Israeli.

Koma analakwa popembedza Baala, motero anafa.

2Tsopano akunka nachimwirachimwirabe;

akudzipangira mafano pogwiritsa ntchito siliva wawo,

zifanizo zopangidwa mwaluso,

zonsezo zopangidwa ndi amisiri.

Amanena za anthu awa kuti,

“Amatenga munthu ndi kumupereka nsembe

ndipo amapsompsona fano la mwana wangʼombe.”

3Choncho adzakhala ngati nkhungu yammawa,

ngati mame amene amakamuka msanga,

ngati mungu wowuluka kuchokera pa malo opunthira tirigu,

ngati utsi umene ukutulukira pa zenera.

4Koma Ine ndine Yehova Mulungu wanu,

amene ndinakutulutsani mu Igupto.

Simuyenera kudziwa Mulungu wina, koma Ine ndekha,

palibe Mpulumutsi wina kupatula Ine.

5Ndinakusamalira mʼchipululu,

mʼdziko lotentha kwambiri.

6Pamene ndinawadyetsa, iwo anakhuta;

iwo atakhuta anayamba kunyada;

ndipo anandiyiwala Ine.

7Motero ndidzawalumphira ngati mkango,

ndidzawabisalira mu msewu ngati kambuku.

8Ngati chimbalangondo cholandidwa ana ake,

ndidzawambwandira ndi kuwathyolathyola.

Ndidzawapwepweta ngati mkango;

chirombo chakuthengo chidzawakhadzula.

9“Iwe Israeli, wawonongedwa,

chifukwa ukutsutsana ndi Ine, ukutsutsana ndi mthandizi wako.

10Kodi mfumu yako ili kuti, kuti ikupulumutse?

Olamulira ako a mʼmizinda yonse ali kuti,

amene iwe unanena za iwo kuti,

‘Patseni mfumu ndi akalonga?’

11Choncho Ine ndinakupatsani mfumu mwachipseramtima,

ndipo ndinayichotsa mwaukali.

12Kulakwa kwa Efereimu kwasungidwa,

machimo ake alembedwa mʼbuku.

13Zowawa zonga za mayi pa nthawi yobala mwana zamugwera,

koma iye ndi mwana wopanda nzeru,

pamene nthawi yake yobadwa yafika

iyeyo safuna kutuluka mʼmimba mwa amayi ake.

14“Ndidzawapulumutsa ku mphamvu ya manda;

ndidzawawombola ku imfa.

Kodi iwe imfa, miliri yako ili kuti?

Kodi iwe manda, kuwononga kwako kuli kuti?

“Sindidzachitanso chifundo,

15ngakhale Efereimu akondwe pakati pa abale ake,

mphepo ya kummawa yochokera kwa Yehova idzabwera,

ikuwomba kuchokera ku chipululu.

Kasupe wake adzaphwa

ndipo chitsime chake chidzawuma.

Chuma chake chonse chamtengowapatali

chidzafunkhidwa ndipo chidzatengedwa.

16Anthu a ku Samariya adzalangidwa chifukwa cha zolakwa zawo,

chifukwa anawukira Mulungu wawo.

Adzaphedwa ndi lupanga;

ana awo adzaphedwa mowamenyetsa pansi,

akazi awo oyembekezera adzatumbulidwa pa mimba.”