但以理書 8 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

但以理書 8:1-27

公綿羊和公山羊的異象

1在看見先前的異象之後,我但以理伯沙撒王執政第三年又看見一個異象。 2我在異象中看見自己在以攔省的書珊城,又看見自己站在烏萊河畔。 3我舉目觀看,見一隻長著長角的公綿羊站在河邊,其中一角比另一角長,較長的角是後長出來的。 4我看見這公綿羊向西方、北方和南方頂撞,沒有獸能抵擋牠,或逃脫牠的威力。牠隨心所欲,狂妄自大。

5我正沉思的時候,忽然從西面出現一隻公山羊,穿越大地,腳不沾地。牠雙眼之間有一個大角。 6這公山羊來到我之前看見的那隻站在河邊的雙角公綿羊那裡,憤怒地向牠頂去。 7我看見公山羊憤怒地頂向公綿羊,攻擊牠,折斷了牠的雙角。公綿羊無力抵擋,被撞倒在地,踐踏在腳下,無人能救牠脫離公山羊的威力。 8公山羊極其狂妄自大。但正值鼎盛之時,牠的大角突然折斷,在原處又長出四個奇特的角,朝著天的四方。 9其中一個角又長出一個小角,向南方、東方和佳美之地8·9 佳美之地」指以色列,下同11·1641擴張勢力。 10它逐漸強大,高及天軍,將一些天軍和星宿拋到地上,用腳踐踏。 11它狂妄自大,要與天軍的統帥比高,它廢除日常獻給祂的祭,毀壞祂的聖所。 12因為反叛的緣故,天軍和日常所獻的祭都交給了它。它將真理拋在地上,它所行的無不順利。

13接著,我聽見一位聖者在說話,另一位聖者問他:「異象中出現的有關日常所獻的祭,毀滅性的反叛和踐踏聖所及天軍的事要持續多久呢?」 14他對我說:「兩千三百個晝夜。之後,聖所才會潔淨。」

解釋異象

15但以理看見這異象,正想明白它的意思,忽然有一個外貌像人的站在我面前。 16我聽見有人聲從烏萊河兩岸之間呼喊:「加百列啊,要讓此人明白這異象。」 17於是,他朝我站的地方走來,當他走來的時候,我嚇得俯伏在地。他對我說:「人子啊,你要明白,這異象是關於末後的時期。」 18他和我說話的時候,我伏在地上昏睡過去,他便輕拍我,扶我起來, 19對我說:「我要告訴你將來上帝發烈怒時所發生的事,因為這異象是關於那定好的末後時期。 20你看見的那隻有兩角的公綿羊指瑪代波斯的諸王。 21公山羊指希臘王,在牠雙眼之間的大角指第一個王。 22大角折斷後,從原處長出四個角表示四個國必從這國興起,但都不及這國強大。 23在四國的末期,人們惡貫滿盈的時候,必有一個面貌兇惡、詭計多端的王興起。 24他勢力強大,卻不是靠自己的力量。他必帶來可怕的毀滅,而且凡事亨通,他必毀滅強者和聖民。 25他利用詭計和騙術得逞,心高氣傲,乘人不備突然毀滅許多人,甚至要攻擊萬君之君,然而他終必被擊垮,但並非被人的手擊垮。 26異象中所說的兩千三百個晝夜是真的。但你要保密,不可告訴別人,因為這指的是遙遠的將來。」

27但以理精疲力盡,病了幾天。後來我起來照常辦理王的事務,但我對這異象感到驚奇不已,不明白它的意思。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Danieli 8:1-27

Masomphenya a Danieli a Nkhosa Yayimuna ndi Mbuzi Yayimuna

1Chaka chachitatu cha ulamuliro wa mfumu Belisazara, Ine Danieli, ndinaonanso masomphenya, ena atatha amene anandionekera poyamba. 2Ndinaona mʼmasomphenya kuti ndinali mu mzinda wotetezedwa wa Susa mʼchigawo cha Elamu. Mʼmasomphenyawo ndinaona nditayima pafupi ndi mtsinje wa Ulai. 3Nditakweza maso ndinaona nkhosa yayimuna ya nyanga ziwiri, itayima pafupi ndi mtsinje. Nyanga zakezo zinali zazitali. Nyanga imodzi inali yotalika kuposa inzake, ndipo iyi inaphuka inzakeyo itamera kale. 4Ndinaona nkhosa yayimunayo ikuthamanga mwaukali kupita kumadzulo, kumpoto ndi kummwera. Palibe chirombo chimene chikanatha kulimbana nayo, ndipo palibe akanatha kulanditsa kanthu kwa iyo. Iyo inachita monga inafunira ndipo inali ndi mphamvu zambiri.

5Pamene ndinali kulingalira za zinthu zimenezi, mwadzidzidzi mbuzi yayimuna inatulukira cha kumadzulo, kudutsa dziko lonse lapansi mwaliwiro ikuyenda mʼmalele mokhamokha. Mbuzi yayimunayo inali ndi nyanga yayikulu pakati pa maso ake. 6Inabwera molunjika nkhosa yayimuna ya nyanga ziwiri ija imene ndinaona itayima pafupi ndi mtsinje. Ndipo inayithamangira mwaukali. 7Inafika pafupi ndipo inalimbana nayo mwaukali nkhosa yayimuna ija nʼkuthyola nyanga zake ziwiri. Nkhosa yayimunayo inalibenso mphamvu zogonjetsera mbuziyo; choncho mbuzi ija inagwetsa nkhosayo pansi nʼkuyipondaponda, ndipo palibe akanatha kulanditsa nkhosayo kwa mbuziyo. 8Mbuziyo inayamba kudzikuza kwambiri chifukwa cha mphamvu zake koma pamene mphamvuzo zinakula kwambiri nyanga yake yayikulu inathyoka, ndipo mʼmalo mwake panamera nyanga zinayi moloza mbali zonse zinayi.

9Pa imodzi mwa nyangazo panatuluka nyanga imene inali yocheperapo koma inakula kwambiri kuloza kummwera ndi kummawa ndi kuloza dziko lokongola. 10Inakula mpaka inafikira gulu lankhondo la kumwamba, ndipo inagwetsera ena a gulu lankhondolo ndi ena a gulu la nyenyezi ku dziko lapansi ndi kuwapondaponda. 11Inadzikuza yokha mpaka kufikira kwa mfumu ya gululo: inathetsa nsembe zimene zinkaperekedwa tsiku ndi tsiku, ndipo inagwetsa nyumba yake yopatulika. 12Gulu lake la nkhondo linathetsa nsembe zoperekera machimo za tsiku ndi tsiku; chipembedzo choonadi chinaponderezedwa pansi. Nyangayi inapambana mu zonse zimene inachita.

13Kenaka ndinamva wina akuyankhula; ndipo woyera winanso anamufunsa kuti, “Kodi zimene ndikuziona mʼmasomphenyazi zidzatha liti? Nsembe zoperekera machimo za tsiku ndi tsiku zidzakhala zoletsedwa mpaka liti? Nanga chonyansa chosokoneza chidzakhalapo mpaka liti? Kodi gulu la ankhondo lidzapondereza malo opatulika mpaka liti?”

14Iye anandiyankha kuti, “Zidzachitika patapita masiku 2,300; pambuyo pake malo opatulika adzabwezeretsedwa monga kale.”

Kumasulira kwa Masomphenya

15Ine Danieli ndikuyangʼanitsitsa masomphenyawa ndi kuyesa kuwazindikira, kuwamvetsa, ndinangoona wina wooneka ngati munthu atayima patsogolo panga. 16Ndipo ndinamva mawu a munthu kuchokera mʼmbali mwa mtsinje wa Ulai akuyitana kuti, “Gabrieli, muwuze munthuyu tanthauzo la masomphenyawo.”

17Atayandikira kumene ndinayima, ndinachita mantha ndi kugwa chafufumimba. Iye anati, “Mwana wa munthu, zindikira kuti masomphenyawa akunena za nthawi yachimaliziro.”

18Pamene ankandiyankhula ndinadzigwetsa pansi chafufumimba, nʼkugona tulo tofa nato. Kenaka anandikhudza ndi kundiyimiritsa.

19Iye anati, “Ine ndikuwuza zimene zidzachitike ukadzatha mkwiyo, chifukwa masomphenyawa ndi a nthawi ya chimaliziro.” 20Nkhosa yayimuna ya nyanga ziwiri imene unayiona, ikuyimira mafumu a Amedi ndi Aperezi. 21Mbuzi yayimuna ija ndi mfumu ya Agriki, ndipo nyanga yayikulu pakati pa maso ake aja ndi mfumu yoyamba. 22Kunena za nyanga inathyoka ija ndi nyanga zinayi zimene zinaphuka mʼmalo mwake zikutanthauza maufumu anayi amene adzatuluka mʼdziko lake; koma sizidzafanana mphamvu ndi ufumu woyambawo.

23“Pa masiku otsiriza a maufumuwa, machimo awo atachulukitsa, padzadzuka mfumu yaukali ndi yochenjera kwambiri. 24Idzakhala yamphamvu kwambiri koma osati mphamvu za iyo yokha. Idzawononga koopsa ndipo idzapambana mu chilichonse chimene idzachite. Mfumuyi idzawononga anthu amphamvu ndi anthu oyera omwe. 25Chifukwa cha kuchenjera kwake chinyengo chidzachuluka pa nthawi ya ulamuliro wake, ndipo idzadzikuza kuposa onse. Pamene oyera mtima adzaona ngati kuti ali otetezedwa, iyo idzawononga ambiri ndi kuwukira ngakhale Mfumu ya mafumu. Komabe idzawonongedwa, koma osati ndi mphamvu za munthu.

26“Masomphenya okhudza madzulo ndi mmawa amene unawaona aja ndi woona, koma uwasunge masomphenyawa mwachinsinsi popeza ndi onena za masiku a mʼtsogolo kwambiri.”

27Ine Danieli ndinafowoka ndipo ndinadwala masiku angapo. Kenaka ndinadzuka ndi kupitiriza ntchito za mfumu. Ndinada nkhawa ndi masomphenyawo; ndipo sindinathe kuwamvetsa.