但以理書 7 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

但以理書 7:1-28

但以理夢見四獸

1巴比倫伯沙撒元年,但以理在床上做了一個夢,腦中出現了異象,便把夢記錄下來,講述其中的大意。 2但以理說:「我在夜間的異象中看見天風四面吹來,攪動大海。 3接著,四隻巨獸從海中上來,各有不同的形狀。 4第一隻獸像獅子,但有鷹的翅膀。我觀看時,見牠的翅膀被拔掉。牠被扶起來,像人一樣雙腳站在地上,並被賦予人的頭腦。 5第二隻獸像熊,用兩隻後腿站立,牙齒間叼著三根肋骨,有聲音對牠說,『起來,多吞吃肉吧!』

6「此後,我繼續觀看,見還有一隻獸像豹,背上有四個如鳥翼般的翅膀。這獸有四個頭,並被賦予權柄。 7此後,我在夜間的異象中看見第四隻獸,恐怖可怕,極其強壯,用大鐵牙吞吃、咬碎獵物,用腳踐踏所剩的。這獸與前三隻獸不同,牠有十個角。 8我觀看這些角時,見其中長出一個小角,先前的角中有三個被連根拔出,讓它取而代之。這小角有人的眼睛和說狂言的口。

9「我看見寶座已設立,

上面坐著亙古長存者,

祂的衣服潔白如雪,

頭髮如純淨的羊毛。

祂的寶座是火焰,

寶座的輪子是烈火。

10從祂面前流出火河,

事奉祂的有千千,

侍立在祂面前的有萬萬。

祂坐下要審判,

案卷已經展開。

11「我繼續觀看,見那獸被殺,身體被毀並被扔進火中,因為牠的小角口出狂言。 12至於其餘的獸,牠們的權柄都被奪去,但獲准再存活一段時間。

13「我在夜間的異象中看見一位像人子的,駕著天雲而來,到亙古長存者那裡,被引到祂面前。 14他得到權柄、榮耀和國度,各族、各邦、各語種的人都要事奉他。他的統治直到永遠、沒有窮盡,他的國度永不滅亡。

解釋異象

15「我但以理心中不安,腦中出現的異象令我恐懼, 16便走近一位侍立一旁的,問他這些事的意思。他就向我解釋這些事的意思,說, 17『這四隻巨獸是指四個將要在世上興起的國。 18但至高者的聖民必承受國度,並永永遠遠擁有國度。』

19「那時,我想知道關於第四獸的事,牠與其餘三獸不同,極其可怕,有鐵牙銅爪,吞吃、咬碎獵物,用腳踐踏所剩的。 20我也想知道有關牠頭上的十角及後來長出的小角的事。這小角取代了三角,它有眼和說狂言的口,比其他的角更強大。 21我看見這小角與聖民爭戰,並佔了上風。 22後來亙古長存的至高者來為祂的聖民伸冤。聖民擁有國度的時候到了。

23「那位侍立一旁的說,『第四隻獸是指世上將興起的第四個國,與其他各國不同,牠將吞吃、踐踏、咬碎天下。 24十角是指這國中將興起十個王,後來又興起一王,與先前的王不同,他將制伏三個王。 25他必褻瀆至高者,迫害至高者的聖民,試圖改變節期和律法。聖民將被交在他手中三年半。 26然而,審判者將坐下來審判,奪去並永遠廢除他的權柄。 27那時,國度、權柄和天下萬國的尊榮必賜給至高者的聖民。祂的國度直到永遠,一切掌權者都要事奉祂,順服祂。』

28「這就是我的夢。我但以理心中十分害怕,臉色蒼白,但我沒有把這事告訴別人。」

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Danieli 7:1-28

Maloto a Danieli a Zirombo Zinayi

1Chaka choyamba cha ufumu wa Belisazara wa ku Babuloni, Danieli akugona pa bedi lake analota maloto ndipo anaona masomphenya. Iye analemba malotowo mwachidule.

2Danieli anati, “Mʼmasomphenya anga usiku, ndinaona nyanga yayikulu ikuvunduka ndi mphepo zochokera mbali zonse zinayi za mlengalenga. 3Ndipo mʼnyangayo munatuluka zirombo zazikulu zinayi, chilichonse chosiyana ndi chinzake.

4“Choyamba chinali ngati mkango, ndipo chinali ndi mapiko ngati a chiwombankhanga. Ndinayangʼanitsitsa, kenaka mapiko ake anakhadzuka ndipo chinanyamulidwa ndi kuyimirira ndi miyendo yake iwiri ngati munthu, ndipo anachipatsa mtima wa munthu.

5“Ndipo ndinaona chirombo chachiwiri, chimene chimaoneka ngati chimbalangondo. Chinali chonyamuka mbali imodzi, ndipo chinapana nthiti zitatu mʼkamwa mwake pakati pa mano ake. Anachilamula kuti, ‘Nyamuka, idya nyama yambiri!’

6“Pambuyo pake, ndinaona chirombo china, chimene chinkaoneka ngati kambuku. Pa msana pake chinali ndi mapiko anayi onga a mbalame. Chirombo ichi chinali ndi mitu inayi, ndipo chinapatsidwa mphamvu kuti chilamulire.

7“Zitatha izi, mʼmasomphenya anga usiku, ndinaonanso chirombo chachinayi chitayima patsogolo panga. Chinali choopsa, chochititsa mantha ndi champhamvu kwambiri. Chinali ndi mano akuluakulu a chitsulo. Chimati chikatekedza ndi kumeza adani ake kenaka chinapondereza chilichonse chotsala. Ichi chinali chosiyana ndi zirombo zoyambirira zija, ndipo chinali ndi nyanga khumi.

8“Ndikulingalira za nyangazo, ndinaona nyanga ina, yocheperapo, imene inkatuluka pakati pa zinzake. Zitatu mwa nyanga zoyamba zija zinazulidwa mwa icho. Nyanga iyi inali ndi maso a munthu ndi pakamwa pamene pankayankhula zodzitama.

9“Ine ndikuyangʼanabe ndinaona

“mipando yaufumu ikukhazikitsidwa,

ndipo Mkulu Wachikhalire anakhala pa mpando wake.

Zovala zake zinali zoyera ngati chisanu chowundana;

tsitsi la kumutu kwake linali loyera ngati thonje.

Mpando wake waufumu unali wonga malawi a moto,

ndipo mikombero yake yonse inkayaka moto.

10Mtsinje wa moto unkayenda,

kuchokera patsogolo pake.

Anthu miyandamiyanda ankamutumikira;

ndipo anthu osawerengeka anayima pamaso pake.

Abwalo anakhala malo awo,

ndipo mabuku anatsekulidwa.

11“Ndinapitiriza kuyangʼanitsitsa chifukwa cha mawu odzitamandira amene nyanga ija inkayankhula. Ndili chiyangʼanire choncho chirombo chachinayi chija chinaphedwa ndipo thupi lake linawonongedwa ndi kuponyedwa mʼngʼanjo ya moto. 12Zirombo zina zija zinalandidwa ulamuliro wawo, koma zinaloledwa kukhala ndi moyo kwa kanthawi.

13“Ndikuyangʼanabe zinthu mʼmasomphenya usiku, ndinaona wina ngati mwana wa munthu, akubwera ndi mitambo ya kumwamba. Anayandikira Mkulu Wachikhalire uja. Ena anamuperekeza kwa Iye. 14Anapatsidwa ulamuliro, ulemerero ndi mphamvu za ufumu kuti anthu a mitundu ina yonse, mayiko ndi anthu aziyankhulo zosiyanasiyana apembedze iye. Mphamvu zake ndi mphamvu zamuyaya zimene sizidzatha, ndipo ufumu wake sudzawonongeka konse.

Tanthauzo la Maloto

15“Ine Danieli ndinavutika mu mzimu, ndipo zimene ndinaziona mʼmasomphenya zinandisautsa mʼmaganizo. 16Ndinayandikira mmodzi mwa amene anayima pamenepo ndi kumufunsa tanthauzo lenileni la zonsezi.

“Kotero anandiwuza ndi kundipatsa tanthauzo la zinthu zonse izi: 17‘Zirombo zikuluzikulu zinayi zija ndi maufumu anayi amene adzaoneka pa dziko lapansi. 18Koma oyera mtima a Wammwambamwamba adzalandira ufumu ndipo udzakhala nawo mpaka muyaya, inde ku nthawi zonse.’

19“Kenaka ndinafuna kudziwa tanthauzo lenileni la chirombo chachinayi chija, chimene chinali chosiyana ndi zinzake zonse ndi choopsa kwambiri, cha mano ake achitsulo ndi zikhadabo zamkuwa; chirombo chimene chinapweteka ndi kumeza zinazo ndi kupondaponda chilichonse chimene chinatsala. 20Ndinafunanso kudziwa za nyanga khumi za pa mutu pake ndiponso ina ija, nyanga imene inaphuka pambuyo pake ndi kugwetsa zitatu zija. Imeneyi ndi nyanga ija yokhala ndi maso ndi pakamwa poyankhula modzitamandira, ndipo inkaoneka yayikulu kupambana zina zonse. 21Ndikuyangʼanitsitsa, nyanga imeneyi inathira nkhondo anthu oyera mtima ndi kuwagonjetsa, 22mpaka pamene Mkulu Wachikhalire uja anafika ndi kuweruza mokomera oyera mtima a Wammwambamwamba. Tsono nthawi inafika imene anthu oyera mtimawo analandira ufumu.

23“Tsono anandifotokozera kuti, ‘Chirombo chachinayi chija ndi ufumu wachinayi umene udzaoneka pa dziko lapansi. Udzakhala wosiyana ndi maufumu anzake onse ndipo udzawononga dziko lonse lapansi. Udzalipondaponda ndi kuliphwasula. 24Nyanga khumi zija ndiwo mafumu khumi amene adzatuluka mu ufumu umenewu. Pambuyo pake mfumu ina idzadzuka, yosiyana ndi mafumu a mʼmbuyomu; iyo idzagonjetsa mafumu atatu. 25Idzayankhula motsutsana ndi Wammwambamwamba ndipo adzazunza oyera mtima ndi kusintha masiku azikondwerero ndi malamulo. Oyera mtimawo adzalamulidwa ndi mfumuyi kwa zaka zitatu ndi theka.

26“ ‘Koma bwalo lidzapereka chiweruzo, ndipo mphamvu zake zidzalandidwa ndi kuwonongedwa kotheratu mpaka muyaya. 27Kenaka ulamuliro, mphamvu ndi ukulu wa maufumu pa dziko lonse lapansi zidzaperekedwa kwa oyera mtima, a Wammwambamwamba. Ufumu wawo udzakhala ufumu wosatha, ndipo olamulira onse adzawalamulira ndi kuwamvera.’ ”

28“Apa ndiye pa mapeto pa nkhaniyi. Ine Danieli, ndinasautsidwa kwambiri mʼmaganizo anga, ndipo nkhope yanga inasandulika, koma ndinasunga nkhaniyi mu mtima mwanga.”