但以理書 6 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

但以理書 6:1-28

但以理在獅子坑

1大流士決定設立一百二十個總督治理全國。 2總督之上,設三個總長,以維護王的統治,但以理是其中之一。 3因為但以理有非凡的心智,遠超過其他總長和總督,王便考慮讓他治理全國。 4於是,其他總長和總督想在但以理的政務中找把柄控告他,卻找不到任何把柄或過失,因為他誠實可靠,毫無過失。 5最後他們說:「除非我們從但以理上帝的律法下手,否則找不到指控他的把柄。」

6於是,這些總長和總督齊來見王,說:「願大流士王萬歲! 7所有總長、行政官、總督、謀士和省長都認為王應該下一道禁令,三十天內,任何人不得向王以外的神明或人禱告,違者必被扔進獅子坑。 8王啊,求你頒佈、簽署這道禁令,使之不可更改,正如瑪代人和波斯人的律令是不可更改的。」 9於是大流士王簽署了這道禁令。

10但以理知道王簽署禁令後,就回到家裡。他樓上的窗戶朝向耶路撒冷,他像往常一樣每日三次跪下向上帝禱告、感恩。 11那些官員一同來了,發現但以理向他的上帝禱告、祈求, 12便去見王,提及王的禁令,說:「王啊,你不是簽署禁令,三十天內,任何人不得向王以外的神明或人禱告,違者必被扔進獅子坑嗎?」王說:「確有此事,按照瑪代人和波斯人的律,這禁令不可更改。」 13他們對王說:「王啊,被擄來的猶大但以理不理會你和你的禁令,仍一日三次向他的上帝祈禱。」 14王聽了這些話,十分愁煩,一心想救但以理,直到日落都在籌畫解救之道。 15那些人齊來見王,說:「王啊,按照瑪代人和波斯人的律,王頒佈的禁令和律例是不可更改的。」

16王便下令把但以理帶來扔進獅子坑。他對但以理說:「願你忠心事奉的上帝拯救你!」 17坑口用大石封住,並加上王和大臣的封印,使懲辦但以理的事不可更改。 18王回宮後,整夜禁食,拒絕娛樂,無法入睡。

19次日黎明,王起來匆忙趕往獅子坑, 20到了坑邊,淒聲呼喊但以理:「永活上帝的僕人但以理啊,你忠心事奉的上帝有沒有救你脫離獅子的口?」 21但以理對王說:「願王萬歲! 22我的上帝差遣天使封住了獅子的口,不讓牠們傷害我,因為我在上帝面前是清白的。王啊,我在你面前也沒有過錯。」 23王非常高興,便命人把但以理從坑中拉上來。於是,但以理從坑中被拉了上來,他因為信靠他的上帝,身上毫無損傷。 24王下令把那些惡意控告但以理的人及其兒女妻子都帶來,扔進獅子坑。他們還沒到坑底,獅子便撲上去,咬碎了他們的骨頭。

25後來,大流士王傳諭境內的各族、各邦、各語種的人,說:「願你們大享平安! 26我下令,我統治的國民都要敬畏但以理的上帝,

「因為祂是永活長存的上帝,

祂的國度永不滅亡,

祂的統治直到永遠。

27祂庇護、拯救,

在天上地下行神蹟奇事,

但以理脫離獅子的口。」

28因此,在大流士波斯塞魯士執政期間,但以理凡事亨通。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Danieli 6:1-28

Danieli Mʼdzenje la Mikango

1Kunamukomera Dariyo kusankha akalonga 120 kuti alamulire mu ufumu wonse, 2ndikusankha nduna zazikulu zitatu kuti ziwayangʼanire ndipo imodzi mwa ndunazo anali Danieli. Akalongawo amayangʼaniridwa ndi nduna zazikuluzo kuti zinthu za mfumu zisawonongeke. 3Tsono Danieli anadzionetsa kuti akhoza kugwira ntchito bwino kopambana nduna zinzake chifukwa anali wanzeru kwambiri. Ndiye mfumu inaganiza zomuyika kuti akhale woyangʼanira ufumu wonse. 4Chifukwa cha ichi, anzake ndi akalonga anayesa kupeza zifukwa zomutsutsira Danieli pa kayendetsedwe ka ntchito za dzikolo, koma sanapeze cholakwa chilichonse. Iwo sanapeze chinyengo mwa iye, chifukwa anali wokhulupirika ndipo sankachita chinyengo kapena kutayirira ntchito. 5Pomaliza, anthu awa ananena kuti, “Sitidzapeza cholakwa chilichonse chomutsutsira Danieli kupatula chokhacho chimene chikhudza chipembedzo cha Mulungu wake.”

6Choncho akalonga ndi nduna pamodzi anapita kwa mfumu ndipo anati: “Inu mfumu Dariyo, mukhale ndi moyo wautali! 7Nduna zoyendetsa ufumu wanu, aphungu, akalonga ndi abwanamkubwa tonse tagwirizana kuti inu mfumu mukhazikitse lamulo ndi kulisindikiza kuti aliyense amene apemphera kwa mulungu wina kapena kwa munthu kupatula kwa inu mfumu, pa masiku makumi atatu otsatirawa, adzaponyedwa mʼdzenje la mikango. 8Tsopano inu mfumu khazikitsani lamulo limeneli ndipo musindikizepo dzina lanu kuti lisasinthike monga mwa malamulo a Amedi ndi Aperezi, amene sasinthidwa.” 9Choncho mfumu Dariyo anasindikizapo dzina lake pa lamuloli.

10Danieli atamva kuti lamulo lasindikizidwa, anapita ku nyumba kwake nalowa mʼchipinda chapamwamba chimene mazenera ake anali otsekula kuloza ku Yerusalemu. Katatu pa tsiku iye ankagwada pansi pa mawondo ndipo amapemphera, kuyamika Mulungu wake, monga momwe ankachitira kale. 11Ndipo anthu awa anapita pamodzi ndi kukapeza Danieli akupemphera ndi kupempha Mulungu wake kuti amuthandize. 12Kotero iwo anapita kwa mfumu ndipo anayankhula naye za lamulo lake kuti, “Kodi simunasindikize lamulo lakuti pa masiku makumi atatu otsatirawa aliyense amene apemphera kwa mulungu wina aliyense kapena kwa munthu kupatula kwa inu mfumu, adzaponyedwa mʼdzenje la mikango?”

Mfumu inayankha kuti, “Lamulo lilipobe monga mwa malamulo a Amedi ndi Aperezi, amene sangathe kusinthika.”

13Kenaka iwo anati kwa mfumu, “Danieli, amene ndi mmodzi mwa akapolo ochokera ku Yuda, sakulabadira inu mfumu, kapena lamulo limene munasindikizapo dzina lanu lija. Iye akupempherabe katatu pa tsiku.” 14Mfumu itamva izi, inavutika kwambiri mu mtima mwake. Iyo inayesa kupeza njira yopulumutsira Danieli. Iyo inachita chotheka chilichonse kufikira kulowa kwa dzuwa kuti imupulumutse.

15Ndipo anthuwo anapita pamodzi kwa mfumu ndipo anati kwa iye, “Kumbukirani, inu mfumu kuti monga mwa lamulo la Amedi ndi Aperezi, palibe chimene mfumu inalamulira kapena kukhazikitsa chimasinthidwa.”

16Choncho mfumu inalamula, ndipo anabwera naye Danieli ndi kukamuponya mʼdzenje la mikango. Mfumu inati kwa Danieli, “Mulungu wako amene umutumikira nthawi zonse, akupulumutse!”

17Anatenga mwala natseka pa khoma pa dzenje la mikango, ndipo mfumu inadindapo chizindikiro chake ndi cha nduna zake kuti wina asasinthepo kanthu pa za Danieli. 18Kenaka mfumu inabwerera ku nyumba yake ndipo inakhala usiku wonse osadya kanthu, osalola chosangalatsa chilichonse. Ndipo sinagone tulo.

19Mʼbandakucha, mfumu inanyamuka ndi kufulumira kupita ku dzenje la mikango lija. 20Itayandikira pa dzenjelo, inayitana Danieli moonetsa nkhawa, “Danieli, mtumiki wa Mulungu wa moyo! Kodi Mulungu wako, amene umutumikira nthawi zonse, wakulanditsa ku mikango?”

21Danieli anayankha kuti, “Inu mfumu mukhale ndi moyo wautali! 22Mulungu wanga anatumiza mngelo wake, ndipo anatseka pakamwa pa mikango. Iyo sinandivulaze chifukwa Mulungu anaona kuti ndine wosalakwa ndi kutinso sindinakulakwireni inu mfumu.”

23Mfumu inali ndi chimwemwe chopambana ndipo inalamulira kuti amutulutse Danieli mʼdzenjemo. Ndipo atamutulutsa Danieli mʼdzenjemo, sanapezeke ndi chilonda chilichonse pa thupi lake, chifukwa iye anadalira Mulungu wake.

24Mwa lamulo la mfumu, anthu onse amene ananeneza Danieli aja anagwidwa ndi kukaponyedwa mʼdzenje la mikango, pamodzi ndi akazi awo ndi ana awo. Ndipo asanafike pansi pa dzenjelo, mikango inawawakha ndi mphamvu ndi kuteketa mafupa awo onse.

25Kenaka mfumu Dariyo inalembera anthu a mitundu yonse, ndi anthu a ziyankhulo zosiyanasiyana a mʼdziko lonse kuti,

“Mtendere uchuluke pakati panu!

26“Ndikukhazikitsa lamulo kuti paliponse mʼdziko langa anthu ayenera kuopa ndi kuchitira ulemu Mulungu wa Danieli.

“Popeza Iye ndi Mulungu wamoyo

ndi wamuyaya;

ufumu wake sudzawonongeka,

ulamuliro wake sudzatha.

27Iye amalanditsa ndipo amapulumutsa,

amachita zizindikiro ndi zozizwitsa

kumwamba ndi pa dziko lapansi.

Iye walanditsa Danieli

ku mphamvu ya mikango.”

28Choncho Danieli anapeza ufulu pa nthawi ya ulamuliro wa Dariyo ndi ulamuliro wa Koresi wa ku Perisiya.