以賽亞書 61 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

以賽亞書 61:1-11

大喜的訊息

1主耶和華的靈在我身上,因為耶和華膏立了我,

讓我傳福音給貧窮的人,

差遣我醫治傷心的人,

宣告被擄的人得釋放、

被囚的人得自由;

2宣告我們上帝耶和華的恩年和祂報仇的日子,

安慰一切悲哀的人;

3以華冠取代錫安哀傷者頭上的灰塵,

以喜樂的膏油取代他們的哀傷,

以頌讚的外袍取代他們的沮喪。

他們將被稱為耶和華所栽種的公義橡樹,

以彰顯祂的榮耀。

4他們必重修古老的荒場,

在久已毀壞之地重建荒廢的城邑。

5異鄉人要為你們牧放羊群,

外族人要為你們耕種田地、

照料葡萄園。

6你們要被稱為耶和華的祭司,

我們上帝的臣僕。

你們必享用各國的財寶,

誇耀自己擁有他們的財富。

7你們曾經蒙受恥辱,

如今將得到雙倍的福分;

你們曾經遭受屈辱,

如今將因得到產業而快樂。

你們將在自己的土地上得到雙倍的福分,

享受永遠的快樂。

8「因為我耶和華喜愛公正,

憎惡搶劫之罪。

我必憑信實賞賜我的子民,

與他們立永遠的約。

9他們的後代必享譽列國,

子孫必名聞萬邦,

看見的人都承認他們是蒙上帝賜福之民。」

10我因耶和華而無比喜樂,

因我的上帝而心裡快樂,

因為祂給我穿上救恩的衣服、

披上公義的袍子,

使我像戴上華冠的新郎,

又像戴上飾物的新娘。

11大地怎樣使嫩苗長出,

園子怎樣使種子發芽,

主耶和華必照樣使公義與頌讚在萬民中滋長。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 61:1-11

Uthenga Wabwino wa Yehova

1Mzimu wa Ambuye Yehova uli pa ine,

chifukwa Yehova wandidzoza

kuti ndilalikire uthenga wabwino kwa anthu osauka.

Wandituma kuti ndikatonthoze anthu osweka mtima,

ndikalengeze kwa akapolo kuti alandire ufulu

ndiponso kuti ndikamasule a mʼndende.

2Wandituma kuti ndikalengeze nthawi imene Yehova adzapulumutsa anthu ake;

za tsiku limene Yehova adzalanga adani a anthu ake.

Wandituma kuti ndikatonthoze olira.

3Wandituma kuti ndiwakonzere olira a ku Ziyoni,

nkhata ya maluwa yokongola

mʼmalo mwa phulusa,

ndiwapatse mafuta achikondwerero

mʼmalo mwa kulira.

Ndiwapatse chovala cha matamando

mʼmalo mwa mtima wopsinjika.

Ndipo iwo adzatchedwa mitengo ya thundu yamphamvu yachilungamo,

yoyidzala Yehova

kuti Iye mwini apezemo ulemerero wake.

4Adzamanganso mabwinja akale a mzinda

ndipo malo amene anawonongeka kalekale aja adzakonzanso.

Adzakonzanso mizinda imene inapasuka,

imene yakhala yowonongeka kwa nthawi yayitali kwambiri.

5Anthu achilendo adzakutumikirani; adzazidyetsa ziweto zanu;

iwo adzagwira ntchito mʼminda yanu ya mpesa.

6Ndipo inu mudzatchedwa ansembe a Yehova,

adzakutchulani kuti ndinu atumiki a Mulungu wathu.

Mudzadyerera chuma cha mitundu ya anthu,

ndipo mudzanyadira ulemu umene mwalandira.

7Chifukwa manyazi awo anali owirikiza;

ndi kuti munalandira

chitonzo ndi kutukwana,

adzakondwera ndi cholowa chawo,

tsono adzalandira cholowa chawo cha chigawo cha dziko mowirikiza,

ndipo chimwemwe chamuyaya chidzakhala chawo.

8“Pakuti Ine Yehova, ndimakonda chilungamo;

ndimadana ndi zakuba ndi zoyipa.

Anthu anga ndidzawapatsa mphotho mokhulupirika

ndikupangana nawo pangano losatha.

9Ana awo adzakhala odziwika pakati pa mitundu ya anthu

ndipo adzukulu awo adzakhala otchuka pakati pa anthu a mitundu ina.

Aliyense wowaona adzazindikira

kuti ndi anthu amene Yehova wawadalitsa.”

10Ine ndikusangalala kwambiri chifukwa cha Yehova;

moyo wanga ukukondwera chifukwa cha Mulungu wanga.

Pakuti Iye wandiveka zovala zachipulumutso,

ndipo wandiveka mkanjo wachilungamo.

Zili ngati mkwati wovala nkhata ya maluwa mʼkhosi mwake,

ndiponso ngati mkwatibwi wovala mikanda yamtengowapatali.

11Monga momwe nthaka imameretsa mbewu

ndiponso monga munda umakulitsa mbewu zimene anadzala,

momwemonso Ambuye Yehova adzaonetsa chilungamo ndi matamando

pamaso pa mitundu yonse ya anthu.