以賽亞書 56 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

以賽亞書 56:1-12

外族人蒙拯救

1耶和華說:

「你們當堅持正義,

秉行公義,

因為我的救恩快要來臨,

我的公義快要彰顯。

2謹守而不褻瀆安息日、

不做惡事的人有福了!」

3皈依耶和華的外族人啊,

不要以為耶和華會把你和祂的子民分開,

太監也不要覺得自己只是一棵枯樹。

4因為耶和華說:

「如果太監遵守我的安息日、

做我喜悅的事、

持守我的約,

5我必在我的殿中、

牆內賜給他們紀念碑和名號,

使他們勝過有兒女的人。

我必賜給他們永遠不會被除去的名號。

6至於那些皈依耶和華、

事奉祂、愛祂的名、

做祂的僕人、

謹守而不褻瀆安息日、

持守祂的約的外族人,

7我必領他們到我的聖山,

到向我禱告的殿內,

使他們歡欣。

他們獻上的燔祭和其他祭物必蒙悅納,

因為我的殿必被稱為萬民禱告的殿。」

8招聚以色列流亡者的主耶和華說:

「除了這些被招聚回來的人以外,

我還要招聚其他人。」

以色列昏庸的首領

9田野和林中的走獸啊,

來吞吃吧!

10以色列的守望者瞎眼無知,

是不會叫的啞巴狗,

只喜歡躺下睡覺做夢。

11這些人就像貪吃的狗,

不知飽足,

又像什麼都不懂的牧人,

人人各行其是,

追求自己的利益。

12他們說:「來吧,我去拿酒,

讓我們喝個痛快!

明天會跟今天一樣,

甚至更豐盛。」

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 56:1-12

Chipulumutso kwa Anthu Ena Onse

1Yehova akuti,

“Chitani chilungamo

ndi zinthu zabwino,

chifukwa chipulumutso changa chili pafupi

ndipo ndidzakuwombolani posachedwapa.

2Ndi wodala munthu amene amachita zimenezi,

munthu amene amalimbika kuzichita,

amene amasunga Sabata osaliyipitsa,

ndipo amadziletsa kuchita zoyipa.”

3Mlendo amene waphatikana ndi Yehova asanene kuti,

“Ndithu Yehova wandichotsa pakati pa anthu ake.”

Ndipo munthu wofulidwa asanene kuti,

“Ine ndine mtengo wowuma basi.”

4Popeza Yehova akuti,

“Wofulidwa amene amasunga masabata anga,

nachita zokomera Ine

ndi kusunga pangano langa,

5ndidzawapatsa dzina ndi mbiri yabwino

mʼkati mwa Nyumba yanga ndi makoma ake,

kuposa kukhala ndi ana aamuna ndi aakazi.

Ndidzawapatsa dzina labwino,

losatha ndi losayiwalika.”

6Yehova akuti, “Alendo amene amadziphatika kwa Yehova,

motero kuti amamutumikira Iye,

amakonda dzina la Yehova,

amamugwirira ntchito,

komanso kusunga Sabata osaliyipitsa

ndi kusunga bwino pangano langa,

7amenewa Ine ndidzawafikitsa ku phiri langa lopatulika,

ndidzawapatsa chimwemwe mʼnyumba yanga ya mapemphero.

Zopereka zawo zopsereza ndi nsembe zawo

ndidzazilandira pa guwa langa la nsembe.

Paja nyumba yanga idzatchedwa

nyumba ya mapemphero ya anthu a mitundu yonse.”

8Ambuye Yehova, amene amasonkhanitsa

Aisraeli onse ali ku ukapolo akunena kuti,

“Ndidzasonkhanitsano anthu ena

kuwonjezera amene anasonkhana kale.”

Mulungu Adzazula Anthu Oyipa

9Bwerani, inu zirombo zonse zakuthengo,

inu nonse zirombo zamʼnkhalango bwerani mudzadye!

10Atsogoleri onse a Israeli ndi akhungu,

onse ndi opanda nzeru;

onse ndi agalu opanda mawu,

samatha kuwuwa:

amagona pansi nʼkumalota

amakonda kugona tulo.

11Ali ngati agalu amene ali ndi njala yayikulu;

sakhuta konse.

Abusa nawonso samvetsa zinthu;

onse amachita monga akufunira,

aliyense amafunafuna zomupindulitsa iye mwini.

12Aliyense amafuwulira mnzake kuti, “Bwera, tiye timwe vinyo!

Tiyeni timwe mowa mpaka kukhuta!

Mawa lidzakhala ngati leroli,

kapena kuposa lero lino.”