以賽亞書 44 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

以賽亞書 44:1-28

以色列蒙揀選

1「我的僕人雅各

我所揀選的以色列啊,

現在你要留心聽。

2造你、使你在母胎中成形、

幫助你的耶和華說,

『我的僕人雅各

我所揀選的耶書崙44·2 耶書崙」是以色列的暱稱。啊,

不要害怕。

3我要用水澆灌乾渴之地,

使河流滋潤乾旱之土。

我要用我的靈澆灌你的後裔,

使我的福澤臨到你的子孫。

4他們要滋長如青草,

又如溪旁楊柳。』

5這個說,『我屬於耶和華』,

那個說,『我是雅各的子孫』,

還有人手上寫著,『耶和華之民』,

稱自己屬於以色列

6「耶和華,以色列的君王和救贖主,

萬軍之耶和華說,

『我是首先的,我是末後的,

除我以外再沒有真神。

7誰能與我相比?讓他告訴我。

自從我設立這古老的民族以來所發生的事和將要發生的事,

讓他告訴我。

8不要恐懼,不要害怕,

我不是早已告訴過你們嗎?

你們是我的證人。

除我以外還有真神嗎?

沒有,沒有別的磐石,

一個也沒有。』」

9製造偶像的真是無用,他們珍愛的偶像毫無價值。拜神像的人目盲眼瞎,愚昧無知,自找羞辱。 10製造神像、雕刻無益偶像的是誰? 11看啊,製造神像的工匠不過是人,他們必羞愧。讓他們一起來對質吧,他們必恐懼、羞愧。 12鐵匠把鐵塊放在炭火裡燒,用他強壯的臂膀揮動鐵錘把它打成偶像。他饑餓時就會無力,口渴時就會疲乏。 13木匠拉線測量木料,用筆勾出形狀,用圓規畫出模樣,仿照人的樣子用鑿子做成逼真的神像,放在廟宇裡。 14他砍伐香柏木,或從林中選取柏木和橡木。他栽種松樹,雨水使它長大。 15這樹可以用來作燃料,他取一些木料生火取暖、烤餅,又製成神像來祭拜,雕成偶像來叩拜。 16他用一半木頭烤肉,飽餐一頓,並用火取暖,說:「啊!我這裡有火,真暖和。」 17他用另一半木頭造了一個神,一個偶像,向它俯伏叩拜、禱告說:「你是我的神明,求你拯救我。」 18他們愚昧無知,因為眼睛被封住以致看不見,心竅被塞住以致不明白。 19他們無人思想,無人明白,無人醒悟說:「我用一半木頭當柴烤餅、烤肉吃,我豈能用另一半木頭造可憎的神像?我豈能向一塊木頭叩拜?」 20他們以灰為食,心智迷糊,走入歧途,不能自救,也不會說:「我右手拿的神像不是假的嗎?」

耶和華救贖以色列

21雅各啊,以色列啊,

要記住這些事,

因為你是我的僕人。

我造了你,你是我的僕人;

以色列啊,我不會忘記你。

22我除去了你的過犯和罪惡,

使它們如雲霧消散。

歸向我吧,因為我救贖了你。」

23諸天啊,歌唱吧!

因為耶和華成就了這事。

地的深處啊,歡呼吧!

眾山嶺和林中的樹木啊,

你們都要歌唱!

因為耶和華救贖了雅各

以色列彰顯了祂的榮耀。

24在母腹中造你、救贖你的耶和華說:

「我是創造萬物的耶和華,

我獨自鋪展穹蒼,開闢大地。

25我使假先知的預兆無法應驗,

使占卜者醜態百出;

我顛覆智者的知識,

使之愚不可及。

26我使我僕人的話應驗,

使我使者的計劃成就。

我說耶路撒冷必有人居住,

我說猶大的城邑必重建起來,

從廢墟中重建起來。

27我對深海說,『枯乾吧!

我要使你的河流乾涸』;

28我說塞魯士是我的牧人,

他必完成我的旨意,

他會下令重建耶路撒冷

降旨奠定聖殿的根基。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 44:1-28

Israeli Wosankhidwa wa Yehova

1Yehova akuti, “Mvera tsopano, iwe Yakobo, mtumiki wanga,

Israeli, amene ndinakusankha.

2Yehova

amene anakupanga iwe, anakuwumba iwe mʼmimba ya amayi ako,

ndi amene adzakuthandiza iwe. Iye akuti,

Usachite mantha, iwe Yakobo, mtumiki wanga,

Yesuruni, amene ndinakusankha.

3Pakuti ndidzathira madzi pa nthaka yowuma,

ndi kuyendetsa mitsinje mʼdziko lowuma;

ndidzatumiza Mzimu wanga pa ana anu,

ndi kutsitsa madalitso anga pa zidzukulu zanu.

4Iwo adzakula ngati udzu wothirira bwino

ndi ngati bango lomera mʼmbali mwa mitsinje ya madzi oyenda.

5Wina adzanena kuti, ‘Ine ndine wa Yehova;’

wina adzadzitcha yekha wa banja la Yakobo;

winanso adzalemba pa dzanja lake, ‘Wa Yehova’

ndipo adzadzitcha wa banja la Israeli.

Yehova, Osati Mafano

6“Yehova Mfumu

ndi Mpulumutsi wa Israeli, Yehova Wamphamvuzonse akuti:

Ine ndine woyamba ndi wotsiriza;

palibenso Mulungu wina koma Ine ndekha.

7Ndani nanga angafanane ndi Ine? Muloleni kuti ayankhule.

Muloleni andifotokozere ndi kundiyalira bwino lomwe

zimene zinachitika kuyambira pamene ndinkakhazikitsa anthu anga akalekale,

ndi ziti zimene zidzachitike;

inde, muloleni alosere zimene zikubwera.

8Musanjenjemere, musachite mantha.

Kodi sindinakuwuzeni zimenezi ndi kuzilosera kalekale lomwe?

Inu ndinu mboni zanga. Kodi aliponso Mulungu wina kupatula Ine?

Ayi, palibe Thanthwe linanso limene sindikulidziwa.”

9Onse amene amapanga mafano ngachabe,

ndipo milungu imene amayilemekeza ndi yopanda phindu.

Iwo amene amapembedza mafano ndi wosaona;

ndipo sazindikira kanthu. Choncho adzawachititsa manyazi.

10Ndani amasema mulungu ndi kuwumba fano,

limene silingamupindulire?

11Iye pamodzi ndi anzake onse adzawachititsa manyazi;

amisiri a mafano ndi anthu chabe.

Aloleni onse asonkhane ndi kuyima pabwalo la milandu;

onse adzaopsedwa ndipo adzachita manyazi.

12Mmisiri wa zitsulo amatenga chitsulo

ndipo amachiyika pa makala amoto;

ndi dzanja lake lamphamvu

amachisula pochimenya ndi nyundo.

Pambuyo pake mʼmisiri uja amamva njala natha mphamvu;

iye samwa madzi, ndipo amalefuka.

13Mmisiri wa matabwa nayenso amayeza mtengo ndi chingwe

ndipo amajambula chithunzi ndi cholembera;

amasema bwinobwino ndi chipangizo chake

ndipo amachiwongola bwino ndi chida chake.

Amachipanga ngati munthu,

munthu wake wokongola

kuti aliyike mʼnyumba yake yachipembedzo.

14Amagwetsa mitengo ya mkungudza,

mwinanso amatenga mtengo wa payini kapena wa thundu

nʼkudzisankhira mtengo wabwino pakati pa mitengo ya mʼnkhalango,

ndipo amadzala mtengo wa payini ndi kuwuleka kuti ukule ndi mvula.

15Mitengoyo munthu amachitako nkhuni;

nthambi zina amasonkhera moto wowotha,

amakolezera moto wophikira buledi

ndi mbali ina ya mtengowo amapangira mulungu ndipo amapembedza;

iye amapanga fano ndi kumaligwadira.

16Chigawo china cha mtengowo amasonkhera moto

wowotcherapo nyama imene

amadya, nakhuta.

Iye amawotha motowo ndipo amanena kuti,

“Aa! Ndikumva kutentha; pano pali moto.”

17Chigawo chotsala amapanga kamulungu, fano lake limenelo;

amaligwadira ndi kulipembedza.

Amapemphera kwa fanolo ndipo amanena kuti,

“Iwe ndiwe mulungu wanga, ndipulumutse.”

18Anthu otere sadziwa kanthu, samvetsa kanthu kalikonse;

maso awo ndi omatirira ndipo sangathe kuona,

ndipo mitu yawo ndi yogontha kotero sangathe kumvetsa.

19Palibe amene amayima nʼkulingalira.

Palibe wanzeru kapena womvetsa zinthu bwino woti nʼkunena kuti,

chigawo china cha mtengowo ndinasonkhera moto;

pa makala ake ndinaphikira buledi,

ndinawotchapo nyama ndipo ndinadya.

Chigawo chotsalachi ndipangire chinthu chonyansachi.

Kodi ndidzagwadira mtengo?

20Munthu wotere ali ngati wodya phulusa, maganizo ake opusa amusocheretsa;

motero kuti sangathe kudzipulumutsa yekha kapena kudzifunsa kuti,

“Kodi chinthu chili mʼmanja mwangachi si chabodza?”

21Yehova akuti, “Iwe Yakobo, kumbukira zinthu izi

popeza kuti ndiwe mtumiki wanga, iwe Israeli.

Ine ndinakupanga iwe, ndiwe mtumiki wanga;

iwe Israeli, sindidzakuyiwala.

22Ndachotsa zolakwa zako ngati mitambo,

ndi machimo ako ngati nkhungu ya mmawa.

Bwerera kwa Ine,

popeza ndakupulumutsa.”

23Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga, pakuti Yehova wachita zimenezi;

fuwula, iwe dziko lapansi.

Imbani nyimbo, inu mapiri,

inu nkhalango ndi mitengo yonse,

chifukwa Yehova wawombola Yakobo,

waonetsa ulemerero wake mwa Israeli.

Anthu Adzakhalanso mu Yerusalemu

24Yehova Mpulumutsi wanu, amene

anakuwumbani mʼmimba ya amayi anu akuti:

“Ine ndine Yehova,

amene anapanga zinthu zonse,

ndinatambasula ndekha zinthu zakuthambo,

ndinayala ndekha dziko lapansi.

25Ndine amene ndinalepheretsa mipingo ya anthu onyenga,

ndipo ndimapusitsa owombeza mawula.

Ndimasokoneza anthu a nzeru,

ndi kuonetsa kuti nzeru zawo nʼzopusa.

26Ndine amene ndimatsimikiza mawu a atumiki ake

ndi kukwaniritsa zimene analosera amithenga ake.

“Ndine amene ndinanena za Yerusalemu kuti mudzakhalanso anthu.

Ndinanenanso za mizinda ya Yuda kuti idzamangidwanso.

Za mabwinja awo ndinanena kuti ndidzawawutsanso.

27Ndine amene ndinawuza nyanga yayikulu kuti, ‘Uma’

ndipo ndidzawumitsa mitsinje yako.

28Ndine amene ndinanena kwa Koresi kuti, ‘Iye ndiye mʼbusa wanga,’

ndipo adzachita zonse zimene ndikufuna;

iye adzalamula kuti, ‘Yerusalemu amangidwenso’

ndi kuti, ‘Maziko a Nyumba ya Mulungu ayikidwenso.’ ”