以賽亞書 42 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

以賽亞書 42:1-25

主的僕人

1「看啊,我所扶持、所揀選、所喜悅的僕人,

我已將我的靈賜給祂,

祂必將正義帶給萬邦。

2祂不喧嚷,不呼喊,

不在街上高聲說話。

3壓傷的蘆葦,祂不折斷;

將殘的燈火,祂不吹滅。

祂必信實地帶來正義。

4祂不灰心也不沮喪,

直到祂在地上設立正義。

四海都渴望祂的訓誨。」

5創造諸天、鋪展穹蒼、

設立大地和地上的一切、

賜給世人生命氣息和靈性的耶和華上帝說:

6「我耶和華憑公義呼召你,

我必扶持你,保護你,

使你做我與眾民立約的中保、

成為列國的光,

7使你開瞎子的眼睛、

從監牢中釋放囚犯、

領出陷在黑暗中的人。

8我是耶和華,這就是我的名字。

我不會把我的榮耀給假神,

也不會把我當受的讚美給雕刻的偶像。

9看啊,以前的預言都已應驗,

我現在要宣告新的預言,

把還未發生的事告訴你們。」

讚美主的歌

10航海的和海中的一切、

眾海島和島上的居民啊,

你們要向耶和華高唱新歌,

從地極讚美祂。

11曠野和其中的城邑以及基達人居住的村莊,

要一同揚聲頌讚。

西拉的居民要歌唱,

在山頂歡呼。

12願他們把榮耀歸給耶和華,

在眾海島上頌讚祂。

13耶和華像出征的勇士,

像鬥志激昂的戰士。

祂必高呼吶喊,戰勝仇敵。

上帝應許幫助以色列人

14「我已沉默多時,我克制不語,

現在我要發出急促的呐喊,

像分娩的婦人。

15我要使大山小丘一片荒涼,

上面的草木都枯萎。

我要使河川變成島嶼,

池塘乾涸。

16我要帶領瞎子走他們不認識的路,

引導他們走陌生的道。

我要把他們面前的黑暗變為光明,

坎坷之地變得平坦。

我必行這些事,我必不離棄他們。

17但那些信靠雕刻的偶像、

供奉金屬鑄像的必遭唾棄,

羞愧難當。

以色列眼瞎耳聾

18「耳聾的人啊,聽吧!

眼瞎的人啊,看吧!

19有誰比我的僕人更瞎,

比我差遣的使者更聾呢?

有誰像那些與我立約的人那樣瞎呢?

有誰像耶和華的僕人那樣瞎呢?

20你們看見許多事卻不領會,

耳朵開著卻聽不見。」

21耶和華樂意使祂的律法尊大而榮耀,

因為祂行事公義。

22但這些百姓飽受劫掠,

都被困在坑中,囚在監內。

他們淪為俘虜,無人搭救;

被當作戰利品擄走,無人追回。

23你們當中誰肯專心聽呢?

以後誰肯留心傾聽呢?

24誰把雅各交給了擄掠者,

使以色列任人劫掠?

難道不是被我們得罪的耶和華嗎?

他們不肯遵行祂的道,

也不聽從祂的訓誨。

25所以,祂把烈怒和戰火傾倒在他們身上。

他們被火包圍,卻不明白;

被烈火焚身,卻不在乎。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 42:1-25

Mtumiki wa Yehova

1“Nayu mtumiki wanga, amene ndimamuchirikiza,

amene ndamusankha, amenenso ndimakondwera naye.

Ndayika Mzimu wanga mwa Iyeyo,

ndipo adzaweruza anthu a mitundu yonse mwachilungamo.

2Iye sadzafuwula, sadzamveka mawu,

kapena mawu ake kumveka mʼmisewu.

3Bango lophwanyika sadzalithyola,

ndipo moto wozilala sadzawuzimitsa.

Motero adzaonetsa kuti chilungamo ndicho choonadi;

4sadzafowoka kapena kukhumudwa

mpaka atakhazikitsa chilungamo pa dziko lapansi,

ndi mpaka mayiko a mʼmbali mwa nyanja atafika poyembekezera malangizo ake.”

5Yehova Mulungu

amene analenga zamlengalenga ndi kuziyalika,

amene analenga dziko lapansi ndi zonse zimene zimabereka,

amenenso amapereka mpweya kwa anthu ake okhala mʼdzikomo,

ndi moyo kwa onse oyendamo, akuti,

6“Ine Yehova, ndakuyitana chifukwa Ine ndine wolungama;

ndikugwira dzanja ndipo

ndidzakuteteza.

Ndakupereka kukhala pangano langa kwa anthu

ndi kuwunika kwa anthu a mitundu ina.

7Udzatsekula maso a anthu osaona,

udzamasula anthu a mʼndende

ndi kutulutsa mʼndende anthu okhala mu mdima.

8“Ine ndine Yehova: dzina langa ndi limenelo!

Sindidzapereka ulemerero wanga kwa wina aliyense

kapena matamando anga kwa mafano.

9Taonani, zinthu zimene ndinalosera kale zachitikadi,

ndipo ndikuwuzani zinthu zatsopano;

zinthuzo zisanaonekere

Ine ndakudziwitsani.”

Nyimbo Yotamanda Yehova

10Imbirani Yehova nyimbo yatsopano,

mutamandeni inu okhala mʼdziko lonse lapansi,

inu amene mumayenda pa nyanja, nyanja ikokome ndi zonse zili mʼmenemo.

Inu okhala pa zilumba tamandani Yehova.

11Chipululu ndi mizinda yake zikweze mawu awo;

midzi ya Akedara ikondwere.

Anthu a ku Sela ayimbe mwachimwemwe;

afuwule kuchokera pamwamba pa mapiri.

12Atamande Yehova

ndipo alalike matamando ake kwa anthu apazilumba zonse.

13Yehova adzapita ku nkhondo ngati munthu wamphamvu,

adzawutsa ukali wake ngati munthu wankhondo;

akukuwa ndiponso akufuwula mfuwu wankhondo

ndipo adzagonjetsa adani ake.

14Yehova akuti, “Ndakhala ndili chete kwa nthawi yayitali,

ndakhala ndili phee osachita kanthu.

Koma tsopano, ngati mayi pa nthawi yochira,

ndi kubuwula ndi kupuma modukizadukiza ndipo ndili wefuwefu.

15Ndidzawononga mapiri ndi zitunda

ndipo ndidzawumitsa zomera zawo zonse;

ndidzasandutsa mitsinje kukhala zilumba

ndipo ndidzawumitsa maiwe.

16Ndidzatsogolera anthu osaona mʼmisewu imene sanayidziwe,

ndidzawatsogolera mʼnjira zimene sanayendepo;

ndidzasandutsa mdima wa kutsogolo kwawo kuti ukhale kuwala

ndipo ndidzasalaza malo osalala.

Zimenezi ndizo ndidzachite;

sindidzawataya.

17Koma onse amene amadalira mafano

amene amanena kwa mafanowo kuti, ‘ndinu milungu yathu,’

ndidzawachititsa manyazi kotheratu.

Aisraeli Alephera Kuphunzira

18“Imvani, agonthi inu;

yangʼanani osaona inu, kuti muone! 19Ali wosaona ndani, si mtumiki wanga kodi?

Ndipo ndani ali wosamva ngati mthenga amene ndamutuma?

Kodi ndani ali wosaona ngati uja ndinachita naye pangano,

kapena wosaona ndani ngati mtumiki wa Yehova?

20Iwe waona zinthu zambiri, koma sunazisamale;

makutu ako ndi otsekuka koma sumva kanthu.”

21Chinamukomera Yehova

chifukwa cha chilungamo chake,

kapena lamulo lake kukhala lalikulu ndi lopambana.

22Koma awa ndi anthu amene afunkhidwa ndi kuwalanda zinthu zawo,

onsewa anawakola mʼmaenje

kapena akuwabisa mʼndende.

Tsono asanduka chofunkha

popanda wina wowapulumutsa

kapena kunena kuti,

“Abwezeni kwawo.”

23Kodi ndani wa inu amene adzamvetsera zimenezi

kapena kutchera khutu ndi kumva za mʼtsogolomo?

24Ndani anapereka Yakobo kwa ofunkha,

ndi Israeli kwa anthu akuba?

Kodi si Yehova,

amene ife tamuchimwirayu?

Pakuti sanathe kutsatira njira zake;

ndipo sanamvere malangizo ake.

25Motero anawakwiyira kwambiri,

nawavutitsa ndi nkhondo.

Anayatsa moto ponseponse mowazungulira komabe iwo sanamvetse;

motowo unawapsereza, koma iwo sanatengepo phunziro ayi.