以斯拉記 3 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

以斯拉記 3:1-13

重建祭壇

1到了七月,以色列人已安居各城,他們萬眾一心地聚集在耶路撒冷2約薩達的兒子耶書亞及其他祭司、撒拉鐵的兒子所羅巴伯及其親屬,一起重新築造以色列上帝的祭壇,為要照上帝的僕人摩西在律法書上的記載在壇上獻燔祭。 3他們雖然懼怕當地的居民,還是在原來的根基上重建祭壇,並早晚在上面向耶和華獻燔祭。 4他們照律法書的記載守住棚節,每天按規定的數目獻上燔祭。 5之後,他們獻上日常的燔祭,並在朔日3·5 朔日」即每月初一。和耶和華所定的一切節期獻祭,又向耶和華獻上自願獻的祭。 6儘管耶和華殿的根基還沒有立好,從七月一日起,他們就開始向耶和華獻燔祭。 7他們付給石匠和木匠銀子,並經波斯塞魯士批准,供給泰爾人和西頓人食物、酒和油,換取他們把香柏木從黎巴嫩經海路運到約帕

開始重建聖殿

8在回到耶路撒冷上帝殿的第二年二月,撒拉鐵的兒子所羅巴伯約薩達的兒子耶書亞及其祭司和利未親族,以及所有從流亡之地回到耶路撒冷的人,開始重建耶和華的殿,並派二十歲以上的利未人做督工。 9何達威雅3·9 何達威雅」希伯來文是「猶大」,參考2·40的後裔,即耶書亞及其子孫和弟兄、甲篾及其子孫,與利未希拿達的子孫及其弟兄同心協力地監督在上帝殿裡做工的人。

10工人立耶和華殿的根基時,祭司身穿禮服拿著號角,利未亞薩的子孫拿著鈸各就各位,照以色列大衛所定的規矩讚美耶和華。 11他們彼此唱和,讚美、稱謝耶和華,說:

「祂是美善的,

因為祂向以色列人永施慈愛!」

所有人都高聲歡呼讚美耶和華,因為耶和華殿的根基已經立好。 12許多曾見過舊殿的年長的祭司、利未人和族長看見這殿的根基,不禁放聲大哭,也有很多人高聲歡呼。 13人們無法分辨是痛哭聲還是歡呼聲,因為眾人都大聲呼喊,聲音傳到遠處。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezara 3:1-13

Kumangidwanso kwa Guwa la Nsembe

1Utafika mwezi wa chisanu ndi chiwiri Aisraeli atakhala kale mʼmidzi yawo, anthu anasonkhana ku Yerusalemu ndi cholinga chimodzi. 2Kenaka Yesuwa mwana wa Yozadaki ndi ansembe anzake pamodzi ndi Zerubabeli mwana wa Sealatieli ndi abale ake anayamba kumanga guwa lansembe la Mulungu wa Israeli. Anatero pofuna kuti aziperekapo nsembe zopsereza monga analembera mʼbuku la Mose, munthu wa Mulungu uja. 3Ndi mantha ndi mantha chifukwa cha anthu a mʼmayikomo, iwo anamanga guwalo pa maziko ake akale, ndipo anapereka nsembe zopsereza kwa Mulungu pa guwapo mmawa ndi madzulo. 4Ankasunga tsiku la chikondwerero cha misasa monga momwe zinalembedwera. Ankaperekanso nsembe za tsiku ndi tsiku monga mwa chiwerengero chake potsata mwambo wake wa tsiku ndi tsiku monga zinalembedwa. 5Pambuyo pake, ankapereka nsembe zopsereza, nsembe zopereka pa nthawi ya mwezi watsopano ndi za pa masiku onse a chikondwerero oyikidwa kutamandira Yehova, kudzanso nsembe zaufulu zopereka kwa Yehova. 6Kuyambira pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri, iwo anayambanso kupereka nsembe zopsereza kwa Yehova, ngakhale kuti maziko a Nyumba ya Yehova anali asanamangidwe.

Kumangidwanso kwa Nyumba ya Mulungu

7Ndipo anapereka ndalama kwa amisiri a miyala ndi kwa amisiri a matabwa, ndi chakudya, chakumwa ndi mafuta kwa anthu a ku Sidoni ndi a ku Turo, kuti abweretse mitengo ya mkungudza pa nyanja kuchokera ku Lebanoni mpaka ku Yopa. Zonsezi anachita malinga ndi chilolezo chimene analandira kuchokera kwa Koresi, mfumu ya Peresiya.

8Tsono mu chaka chachiwiri atabwera ku Yerusalemu, ku malo akale a Nyumba ya Yehova, mwezi wachiwiri Zerubabeli mwana wa Sealatieli, Yesuwa mwana wa Yozadaki pamodzi ndi abale awo onse, ansembe, Alevi ndi onse amene anabwera ku Yerusalemu kuchokera ku ukapolo, anayamba kugwira ntchito. Iwo anasankha Alevi a zaka zoyambira makumi awiri kuti aziyangʼanira ntchito ya kumanga Nyumba ya Yehova. 9Yesuwa ndi ana ake aamuna kudzanso abale ake, Kadimieli ndi ana ake (ana a Yuda) onse pamodzi anasenza udindo woyangʼanira antchito ku Nyumba ya Mulungu, kuphatikizanso ana a Henadadi komanso Alevi, ana awo ndi abale awo.

10Amisiri omanga nyumba atamanga maziko a Nyumba ya Yehova, ansembe anabwera akuyimba malipenga, atavala zovala zaunsembe. Ndipo Alevi, zidzukulu za Asafu, anadza akuyimba matambolini ndi kutenga udindo wawo wotamanda Yehova, potsata malangizo a Davide mfumu ya Aisraeli. 11Iwo ankayimba motamanda ndi mothokoza Yehova nyimbo iyi:

“Yehova ndi wabwino;

chikondi chake pa Israeli ndi chamuyaya.”

Ndipo anthu onse ankafuwula kwambiri kumutamanda Yehova, chifukwa maziko a Nyumba ya Yehova anali kumangidwa. 12Koma ambiri mwa ansembe, Alevi ndiponso atsogoleri amabanja, akuluakulu amene anaona Nyumba ya Yehova yakale, analira mokweza pamene anaona maziko a nyumbayi akumangidwa. Komanso ena ambiri ankafuwula mosangalala. 13Choncho panalibe amene ankatha kusiyanitsa liwu lofuwula mokondwerera ndi liwu la anthu olira, chifukwa anthuwo ankafuwula kwambiri. Ndipo liwu lofuwulalo limamveka kutali.