马太福音 4 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

马太福音 4:1-25

耶稣受试探

1后来,耶稣被圣灵带到旷野,去受魔鬼的试探。 2耶稣禁食了四十昼夜后,很饥饿。 3试探者前来对祂说:“如果你是上帝的儿子,可以叫这些石头变成食物。”

4耶稣回答说:“圣经上说,‘人活着不是单靠食物,乃是靠上帝口中的每一句话。’”

5魔鬼又带祂进圣城,让祂站在圣殿的最高处, 6说:“如果你是上帝的儿子,就跳下去吧!因为圣经上说,‘上帝会差遣祂的天使用手托住你,不让你的脚碰在石头上。’”

7耶稣回答说:“圣经上也说,‘不可试探主——你的上帝。’”

8魔鬼再带耶稣到一座极高的山上,把世上万国及其荣华富贵展示给祂看, 9说:“如果你俯伏敬拜我,我就把这一切都给你。”

10耶稣说:“撒旦,走开!圣经上说,‘要敬拜主——你的上帝,单单事奉祂。’”

11于是魔鬼离开了耶稣,这时有天使前来伺候祂。

开始传道

12耶稣听见约翰被捕入狱,就回到加利利13后来,祂离开拿撒勒迦百农住。迦百农靠近湖边,在西布伦拿弗他利地区。 14这就应验了以赛亚先知的话:

15西布伦拿弗他利

沿海一带及约旦河东、外族人居住的加利利啊!

16你们住在黑暗中的人看见了大光,

活在死亡阴影下的人被光照亮了!”

17从那时起,耶稣开始传道:“悔改吧,因为天国临近了!”

呼召门徒

18耶稣沿着加利利湖边行走的时候,看见被称为彼得西门安得烈两兄弟正在撒网打鱼,他们是渔夫。 19耶稣对他们说:“来跟从我!我要使你们成为得人的渔夫。” 20他们立刻撇下渔网,跟从了耶稣。 21耶稣再往前走,又看见雅各约翰两兄弟正和父亲西庇太一起在船上补渔网。耶稣呼召他们, 22他们马上离开渔船,辞别父亲,跟从了耶稣。

教导和医治

23耶稣走遍加利利,在各个会堂里教导人,宣讲天国的福音,医治人们各样的疾病。 24祂的名声传遍了整个叙利亚。人们把一切患病的,就是患各种疾病的、疼痛的、癫痫的、瘫痪的,以及被鬼附身的都带到祂面前,祂都医治了他们。 25因此,有大群的人跟从了祂,他们来自加利利低加坡里耶路撒冷犹太约旦河东。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mateyu 4:1-25

Yesu Ayesedwa Mʼchipululu

1Pambuyo pake Yesu anatsogozedwa ndi Mzimu Woyera kupita ku chipululu kukayesedwa ndi mdierekezi. 2Ndipo atasala kudya masiku makumi anayi usana ndi usiku, anamva njala. 3Woyesayo anadza kwa Iye nati, “Ngati ndinu mwana wa Mulungu, sandutsani miyala iyi kuti ikhale buledi.”

4Yesu anayankha kuti, “Zalembedwa, ‘Munthu sadzakhala ndi moyo ndi chakudya chokha, koma ndi mawu aliwonse ochokera mʼkamwa mwa Mulungu.’ ”

5Pamenepo mdierekezi anapita naye ku mzinda woyera namuyimiritsa pamwamba penipeni pa Nyumba ya Mulungu. 6Ndipo anati, “Ngati ndinu Mwana wa Mulungu, dziponyeni nokha pansi. Pakuti kwalembedwa:

“ ‘Adzalamulira angelo ake za iwe,

ndipo adzakunyamula ndi manja awo

kuti phazi lako lisagunde pa mwala.’ ”

7Yesu anamuyankha kuti, “Kwalembedwanso: ‘Musamuyese Yehova Mulungu wanu.’ ”

8Kenaka mdierekezi anamutengera Yesu ku phiri lalitali kwambiri namuonetsa maufumu onse a dziko lapansi ndi ulemerero wawo. 9Ndipo anati kwa Iye, “Zonsezi ndidzakupatsani ngati mutandiweramira ndi kundipembedza ine.”

10Yesu anati kwa iye, “Choka Satana! Zalembedwa, ‘Pembedza Yehova Mulungu wako ndi kumutumikira Iye yekha.’ ”

11Pamenepo mdierekezi anamusiya ndipo angelo anamutumikira Iye.

Yesu Ayamba Kulalikira

12Yesu atamva kuti Yohane anamutsekera mʼndende, anabwerera ku Galileya. 13Ndipo atachoka ku Nazareti anapita ku Kaperenawo ndi kukhala mʼmbali mwa nyanja, mʼdera la Zebuloni ndi Nafutali; 14pokwaniritsa zimene zinanenedwa kudzera mwa mneneri Yesaya kuti,

15“Dziko la Zebuloni ndi dziko la Nafutali,

njira ya ku nyanja, kutsidya lija la Yorodani,

Galileya wa anthu a mitundu ina,

16anthu okhala mu mdima

awona kuwala kwakukulu;

ndi kwa iwo okhala mʼdziko la mthunzi wa imfa

kuwunika kwawafikira.”

17Kuyambira nthawi imeneyo, Yesu anayamba kulalikira nati, “Tembenukani mtima ufumu wakumwamba wayandikira.”

Yesu Ayitana Ophunzira ake Oyamba

18Pamene Yesu ankayenda mʼmbali mwa nyanja ya Galileya, anaona abale awiri, Simoni wotchedwa Petro ndi mʼbale wake Andreya akuponya khoka mʼnyanja popeza anali asodzi. 19Yesu anati, “Bwerani, tsateni Ine ndipo ndidzakusandutsani asodzi a anthu.” 20Nthawi yomweyo anasiya makoka awo namutsata Iye.

21Atapita patsogolo, anaona abale ena awiri, Yakobo ndi mʼbale wake Yohane ana a Zebedayo. Iwowa anali mʼbwato ndi abambo awo, Zebedayo, akukonza makoka awo ndipo Yesu anawayitana. 22Nthawi yomweyo anasiya bwato ndi abambo awo namutsata Iye.

Yesu Achiritsa Odwala

23Yesu anayendayenda mu Galileya kuphunzitsa mʼmasunagoge awo, nalalikira Uthenga Wabwino wa ufumu ndi kuchiritsa matenda onse pakati pa anthu. 24Mbiri yake yonse inawanda ku Siriya konse ndipo anthu anabweretsa kwa Iye onse amene anali odwala nthenda zosiyanasiyana, womva maululu aakulu, ogwidwa ndi ziwanda, odwala matenda akugwa ndi olumala ndipo Iye anawachiritsa. 25Magulu ambiri a anthu anachokera ku Galileya, Dekapoli, Yerusalemu, Yudeya ndi ku madera a kutsidya la mtsinje wa Yorodani namutsata Iye.