马太福音 21 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

马太福音 21:1-46

光荣进圣城

1耶稣和门徒离耶路撒冷越来越近了,他们来到橄榄山旁的伯法其2耶稣派两个门徒进村,并对他们说:“你们到前面的村庄去,就会看见一头母驴拴在那里,旁边还有一头驴驹。你们把它们解开,牵到我这里。 3要是有人问起,你们就说,‘主要用它们’,那人会立刻让你们牵来。” 4这件事是要应验先知的话:

5“要对锡安21:5 ”希伯来文是“女子”,可能是对锡安的昵称。说,‘看啊,你的君王来了!祂谦卑地骑着驴,骑着一头驴驹。’”

6两个门徒照着耶稣的吩咐去了, 7把母驴和驴驹带了回来。他们把自己的衣服盖在驴背上,让耶稣骑上去。 8许多人把衣服铺在路上,也有些人砍下树枝铺在路上。 9众人前呼后拥,欢呼着说:

“和散那21:9 和散那”原意是“拯救我们”,此处有“赞美”的意思。归于大卫的后裔!

奉主名来的当受称颂!

和散那归于至高之处的上帝!”

10耶稣进耶路撒冷时,全城轰动,说:“这是谁?”

11众人说:“祂是先知耶稣,来自加利利拿撒勒。”

洁净圣殿

12耶稣进入圣殿,赶走里面做买卖的人,又推翻兑换钱币之人的桌子和卖鸽子之人的凳子。

13耶稣斥责他们说:“圣经上说,‘我的殿必称为祷告的殿。’你们竟把它变成了贼窝。”

14殿中的瞎子和瘸子都来到耶稣面前,祂便医好了他们。 15祭司长和律法教师看见祂所行的奇事,又听见小孩子在圣殿里高声喊着:“和散那归于大卫的后裔!”便十分恼怒。 16他们责问耶稣说:“你听见这些人说的了吗?”

耶稣说:“我听见了。圣经上说,‘你使孩童和婴儿口中发出颂赞’,你们没有读过吗?” 17然后,祂便离开他们,出城前往伯大尼,在那里住宿。

咒诅无花果树

18清早,耶稣在回城的途中饿了。 19祂看见路旁有一棵无花果树,便走过去,却发现除了叶子外什么也没有。

祂对那棵树说:“你将再不会结果子!”那棵树立刻枯萎了。

20门徒见了就惊奇地问:“这棵树怎么一下子枯萎了?”

21耶稣回答说:“我实在告诉你们,如果你们有信心、不怀疑,不但能使无花果树枯萎,就算对这座山说,‘从这里挪开,投进大海里!’也照样可以实现。 22所以,你们祷告时无论求什么,只要有信心,就必定得到。”

质问耶稣的权柄

23耶稣进了圣殿,正在教导人的时候,祭司长和民间的长老来质问祂:“你凭什么权柄做这些事?谁授权给你了?”

24耶稣说:“我也要问你们一个问题,你们回答了,我就告诉你们我凭什么权柄做这些事。 25约翰的洗礼是从哪里来的?从天上来的,还是从人来的?”

他们便彼此议论说:“如果我们说‘是从天上来的’,祂一定会问我们,‘那你们为什么不信他?’ 26但如果我们说‘是从人来的’,又怕触怒百姓,因为他们相信约翰是个先知。” 27于是,他们回答耶稣说:“我们不知道。”

耶稣说:“我也不告诉你们我凭什么权柄做这些事。”

两个儿子的比喻

28耶稣又说:“你们怎样看这件事?某人有两个儿子。他对大儿子说,‘孩子,你今天到葡萄园工作吧!’

29“大儿子回答说,‘我不去!’但后来他改变了主意,就去了。

30“那父亲又对小儿子说,‘你今天到葡萄园工作吧!’小儿子回答说,‘好的,父亲。’他答应了,却没有去。

31“你们认为这两个儿子,到底哪一个服从父亲呢?”

他们回答道:“大儿子。”

耶稣说:“我实在告诉你们,税吏和娼妓要比你们先进上帝的国。 32因为约翰来指示你们当行的正路,你们不信他,但税吏和娼妓信了。你们亲眼看见了这些事,竟然还是执迷不悟,不肯信他。

恶毒的佃户

33“你们再听一个比喻。有个园主栽种了一个葡萄园,在园子的四周建造围墙,又在园中挖了一个榨酒池,建了一座瞭望台,然后把葡萄园租给佃户,就出远门了。 34到了收获的季节,园主派奴仆到佃户那里收果子。 35但那些佃户却抓住他的奴仆,打伤一个,杀死一个,又用石头打死了一个。 36于是,园主又派更多的奴仆去,结果也遭到同样的对待。 37最后,园主派了自己的儿子去,心想,‘他们肯定会尊重我的儿子。’ 38然而,那些佃户看见园主的儿子来了,就商量说,‘这是园主的继承人。来吧!我们杀掉他,占了他的产业!’ 39于是,他们抓住他,把他推出园外杀了。 40那么,当园主回来的时候,他会怎样处置那些佃户呢?”

41他们说:“他会毫不留情地除掉那些恶人,然后把葡萄园租给其他按时交果子的佃户。”

42耶稣说:

“‘工匠丢弃的石头已成了房角石。

这是主的作为,在我们看来奇妙莫测。’

你们难道没有读过这段经文吗? 43所以,我告诉你们,将把上帝的国从你们那里夺去,赐给结果子的人。 44凡跌在这石头上的人,一定粉身碎骨;这石头落在谁身上,就会把谁砸烂。”

45祭司长和法利赛人听了耶稣的比喻,明白是针对他们讲的。 46他们试图逮捕耶稣,但又害怕百姓,因为百姓都认为耶稣是先知。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mateyu 21:1-46

Yesu Alowa mu Yerusalemu

1Akuyandikira ku Yerusalemu anafika ku Betifage pa phiri la Olivi, Yesu anatumiza ophunzira awiri, 2nawawuza kuti, “Pitani ku mudzi uli patsogolo panu, ndipo mukakangolowa mʼmenemo mukapeza bulu womangidwa ali ndi mwana pa mbali pake. Mukawamasule ndipo mubwere nawo kwa Ine. 3Wina akakayankhula, mukamuwuze kuti Ambuye akuwafuna, ndipo adzawatumiza nthawi yomweyo.”

4Izi zinachitika kukwaniritsa zimene zinayankhulidwa ndi mneneri:

5“Uza mwana wamkazi wa Ziyoni,

taona, mfumu yako ikubwera kwa iwe,

yofatsa ndi yokwera pa bulu,

pa kamwana ka bulu, mwana wa nyama yonyamula katundu.”

6Ophunzirawo anapita nachita monga Yesu anawalamulira. 7Anabweretsa bulu ndi mwana wake, nayala zovala zawo pa abuluwo, ndipo Yesu anakwerapo. 8Gulu lalikulu la anthu linayala zovala zawo mu msewu pamene ena anadula nthambi zamitengo ndi kuziyala mu msewumo. 9Magulu amene anali patsogolo pake ndi amene amamutsatira anafuwula kuti,

“Hosana Mwana wa Davide!”

“Wodala Iye amene abwera mʼdzina la Ambuye!”

“Hosana mmwambamwamba!”

10Yesu atalowa mu Yerusalemu, mzinda wonse unatekeseka ndipo anthu anafunsa kuti, “Ndani ameneyu?”

11Magulu a anthu anayankha kuti, “Uyu ndi Yesu, mneneri wochokera ku Nazareti.”

Yesu mʼNyumba ya Mulungu

12Yesu analowa mʼdera lina la Nyumba ya Mulungu ndipo anatulutsa kunja anthu onse amene ankachita malonda. Anagubuduza matebulo a osinthira ndalama ndi mipando ya ogulitsa nkhunda. 13Iye anawawuza kuti, “Zinalembedwa kuti Nyumba yanga idzatchedwa Nyumba ya mapemphero koma inu mwayisandutsa phanga la anthu achifwamba.”

14Anthu osaona ndi olumala anabwera kwa Iye mʼNyumba ya Mulungu ndipo anawachiritsa. 15Koma akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo ataona zodabwitsa zimene anachita, komanso ana akufuwula mʼNyumbayo kuti, “Hosana kwa Mwana wa Davide,” anapsa mtima.

16Anamufunsa kuti, “Kodi mukumva zimene anawa akunena?”

Yesu anayankha nati, “Inde. Kodi simunawerenge kuti,

“Kuchokera mʼkamwa mwa ana ndi makanda

mwatuluka mayamiko?”

17Ndipo anawasiya natuluka mu mzindawo ndi kupita ku Betaniya, kumene anakagona.

Yesu Atemberera Mtengo wa Mkuyu

18Mmamawa, pamene amabwera ku mzinda, anamva njala. 19Ataona mtengo wamkuyu mʼmbali mwa msewu, anapitapo koma sanapeze kanthu koma masamba okhaokha. Pamenepo anati kwa mtengowo, “Usadzabalenso chipatso!” Nthawi yomweyo mtengowo unafota.

20Ophunzira ataona zimenezi, anadabwa nafunsa kuti, “Kodi mtengo wamkuyuwu wauma msanga bwanji?”

21Yesu anayankha kuti, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti ngati muli ndi chikhulupiriro ndipo simukayika, simudzangochita zokha zachitika kwa mkuyuzi, koma mudzatha kuwuza phiri ili kuti, ‘Pita, kadziponye wekha mʼnyanja,’ ndipo zidzachitikadi. 22Ngati mukhulupirira, mudzalandira chilichonse chimene muchipempha mʼpemphero.”

Amufunsa Yesu za Ulamuliro Wake

23Yesu analowa mʼNyumba ya Mulungu, ndipo pamene ankaphunzitsa, akulu a ansembe ndi akuluakulu anabwera kwa Iye namufunsa kuti, “Muchita izi ndi ulamuliro wanji ndipo anakupatsani ndani ulamuliro umenewu?”

24Yesu anayankha kuti, “Inenso ndikufunsani funso limodzi, mukandiyankha, Inenso ndikukuwuzani ndi ulamuliro wa yani umene ndikuchitira izi. 25Ubatizo wa Yohane unachokera kuti? Kumwamba kapena kwa anthu?”

Anakambirana pakati pawo ndipo anati, “Tikati, ‘Kuchokera kumwamba,’ Iye adzafunsa kuti, ‘Bwanji simunakhulupirire?’ 26Koma tikati, ‘Kuchokera kwa anthu,’ ife tikuopa anthuwa, pakuti onse amakhulupirira kuti Yohane anali mneneri.”

27Choncho anamuwuza Yesu kuti, “Sitikudziwa.”

Pamenepo Iye anati, “Inenso sindikuwuzani kuti ndi ulamuliro wa yani umene ndichitira izi.”

Fanizo la Ana Amuna Awiri

28“Kodi muganiza bwanji? Panali munthu wina anali ndi ana aamuna awiri. Anapita kwa woyamba nati, ‘Mwanawe pita kagwire ntchito lero mʼmunda wamphesa.’

29“Iye anayankha kuti, ‘Sindipita,’ koma pambuyo pake anasintha maganizo napita.

30“Kenaka abambowo anapita kwa mwana winayo nanena chimodzimodzi. Iye anayankha kuti, ‘Ndipita abambo,’ koma sanapite.

31“Ndani wa awiriwa anachita chimene abambo ake amafuna?”

Anamuyankha nati, “Woyambayo.”

Yesu anawawuza kuti, “Ndikuwuzani zoonadi, kuti amisonkho ndi adama akulowa mu ufumu wa Mulungu inu musanalowemo.” 32Pakuti Yohane anabwera kwa inu kuti akuonetseni njira yachilungamo, koma inu simunakhulupirire iye, koma amisonkho ndi adama anamukhulupirira. Koma ngakhale munaona izi, simunatembenuke mtima ndi kumukhulupirira iye.

Fanizo la Alimi

33“Tamverani fanizo lina: Panali mwini munda amene anadzala mphesa. Anamanga mpanda kuzungulira mundawo, nakumba moponderamo mphesa ndipo anamanga nsanja. Kenaka anabwereketsa munda wamphesawo kwa alimi ena napita pa ulendo. 34Pamene nthawi yokolola inakwana, anatumiza antchito ake kwa matenanti aja kuti akatenge zipatso zake.

35“Alimi aja anagwira antchito ake; namenya mmodzi, napha wina, ndi kumuponya miyala wachitatuyo. 36Kenaka anatumiza antchito ena oposa oyambawo ndipo matenantiwo anawachitira chimodzimodzi. 37Pomalizira anatumiza mwana wake. Anati adzamuchitira ulemu mwana wanga.

38“Koma alimiwo ataona mwanayo anati kwa wina ndi mnzake, ‘Uyu ndiye olowa mʼmalo mwa abambo ake. Tiyeni timuphe ndipo titenge cholowa chake.’ 39Pamenepo anamutenga namuponyera kunja kwa munda wamphesa namupha.

40“Tsono akabwera mwini munda wamphesa adzachita nawo chiyani matenantiwo?”

41Iwo anayankha kuti, “Adzawapha moyipa alimi oyipawo ndipo adzabwereketsa mundawo kwa alimi ena amene adzamupatsa gawo lake la mbewu pa nthawi yokolola.”

42Yesu anawawuza kuti, “Kodi simunawerenge mʼmalemba kuti:

“ ‘Mwala umene omanga nyumba anawukana,

womwewo wasanduka mwala wofunika kwambiri wa pa ngodya.

Ambuye wachita izi,

ndipo ndi zodabwitsa mʼmaso mwathu.’

43“Nʼchifukwa chake ndi kukuwuzani kuti ufumu wa Mulungu udzalandidwa kwa inu ndipo udzapatsidwa kwa anthu amene adzabereka chipatso chake. 44Amene agwa pa mwalawu adzadukaduka, ndipo amene udzamugwere udzamuthudzula.”

45Akulu a ansembe ndi Afarisi atamva mafanizo a Yesu, anadziwa kuti ankanena iwo. 46Pamenepo anafuna njira yoti amugwirire, koma anaopa gulu la anthu chifukwa anthu onse ankakhulupirira kuti Iye anali mneneri.