马可福音 3 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

马可福音 3:1-35

治好手枯的人

1耶稣又进了会堂,那里有个人一只手是萎缩的。 2当时有好些人密切地监视耶稣,看祂是否会在安息日医治这个人,好找借口控告祂。

3耶稣对那一只手萎缩的人说:“起来,站在中间。” 4然后问众人:“在安息日应该行善还是作恶?救人还是害人?”他们都不吭声。

5耶稣生气地看着四周这些人,为他们的心刚硬而感到极其难过。祂对那人说:“把手伸出来!”那人一伸手,手就立刻复原了。 6法利赛人离开后,立刻和希律党的人策划怎样除掉耶稣。

群众跟随耶稣

7耶稣和门徒退到湖边,有一大群人从加利利来跟随祂。 8还有很多人听见耶稣所做的一切,就从犹太耶路撒冷以土买约旦河东,甚至泰尔西顿一带来找祂。 9耶稣见人多,就吩咐门徒为祂预备一条小船,以免人群拥挤祂。 10因为祂医好了很多人,凡有疾病的人都想挤过来摸祂。 11每当污鬼看见祂,就俯伏在祂面前,大喊:“你是上帝的儿子!” 12耶稣却严厉地吩咐它们不要泄露祂的身份。

选立十二使徒

13耶稣上了山,把合自己心意的人召集到跟前, 14从中选出十二个人,设立他们为使徒,让他们跟随自己,并且差遣他们出去传道, 15赐他们赶鬼的权柄。

16这十二位使徒是:西门——耶稣给他取名叫彼得17西庇太的儿子雅各雅各的兄弟约翰——耶稣给他们取名叫“半尼其”,就是“雷霆之子”的意思、 18安得烈腓力巴多罗买马太多马亚勒腓的儿子雅各达太、激进党人西门19及后来出卖耶稣的加略犹大

耶稣和别西卜

20耶稣刚进家门,人群又聚集起来,以致祂和门徒连吃饭的时间也没有。 21祂的亲属听见这个消息,就出来要拉住祂,因为人们说祂疯了。

22耶路撒冷下来的律法教师说:“祂被别西卜附体。”又说:“祂是靠鬼王赶鬼。”

23耶稣叫他们来,用比喻对他们说:“撒旦怎能驱逐撒旦呢? 24一个国内部自相纷争,必然崩溃。 25一个家内部自相纷争,必然破裂。 26同样,撒旦如果与自己为敌,自相纷争,就站立不住,必然灭亡。 27没有人能进入壮汉家里抢夺他的财物,除非先把那壮汉捆绑起来,才有可能抢劫他的家。

28“我实在告诉你们,世人一切的罪和亵渎的话都可以得到赦免, 29唯有亵渎圣灵的人永远得不到赦免,他们要永远担罪。” 30耶稣这样说是因为他们诬蔑祂被污鬼附身。

谁是耶稣的亲人

31这时候,耶稣的母亲和弟兄来了,他们站在外面,托人叫耶稣。 32有许多人围坐在耶稣身边,他们告诉祂说:“看啊!你的母亲和兄弟在外面找你。”

33耶稣说:“谁是我的母亲?谁是我的弟兄?” 34然后祂望着周围坐着的人说:“看啊!我的母亲、我的弟兄在这里。 35凡遵行上帝旨意的人就是我的弟兄、姊妹和母亲。”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Marko 3:1-35

Yesu Achiritsa Wolumala Dzanja

1Nthawi inanso analowa mʼsunagoge, ndipo munthu wa dzanja lolumala anali momwemo. 2Ena a iwo anafunafuna chifukwa chakuti akamuneneze Yesu, potero anamuyangʼanitsitsa kuti aone ngati angamuchiritse tsiku la Sabata. 3Yesu anati kwa munthu wolumala dzanjayo, “Imirira, bwera kuno kutsogolo.”

4Ndipo Yesu anawafunsa kuti, “Kodi chololedwa ndi chiyani pa tsiku la Sabata: kuchita chabwino kapena kuchita choyipa, kupulumutsa moyo kapena kupha?” Koma iwo anakhala chete.

5Yesu anawayangʼana ndi mkwiyo ndipo powawidwa mtima chifukwa cha mitima yawo yowuma anati kwa munthuyo, “Wongola dzanja lako.” Iye analiwongola, ndipo dzanja lake linachira. 6Kenaka Afarisi anatuluka nayamba kukonza chiwembu ndi Aherode mmene angamuphere Yesu.

Magulu a Anthu Amutsata Yesu

7Yesu anachoka pamodzi ndi ophunzira ake napita ku nyanja, ndipo gulu lalikulu la anthu lochokera ku Galileya linamutsata. 8Atamva zonse zimene amachita, anthu ambiri anabwera kwa Iye kuchokera ku Yudeya, Yerusalemu, Idumeya ndi madera a ku tsidya kwa mtsinje wa Yorodani ndi ozungulira Turo ndi Sidoni. 9Chifukwa cha gulu la anthu, anawuza ophunzira ake kuti apezeretu bwato likhale, kuti anthu angamupanikize. 10Pakuti anachiritsa ambiri, kotero kuti iwo amene anali ndi matenda amakankhana kutsogolo kuti amukhudze. 11Nthawi iliyonse mizimu yoyipa ikamuona, imagwa pansi pamaso pake ndi kufuwula kuti, “Inu ndinu Mwana wa Mulungu!” 12Koma anayichenjeza mwamphamvu kuti isanene kuti Iye anali ndani.

Yesu Asankha Ophunzira Khumi ndi Awiri

13Yesu anakwera ku phiri ndipo anayitana amene anawafuna, ndipo anabwera kwa Iye. 14Iye anasankha khumi ndi awiri, nawayika akhale atumwi; pokhala ndi Iye aziwatuma kukalalikira 15ndi kuti akhale ndi ulamuliro wotulutsa ziwanda. 16Awa ndi khumi ndi awiri amene anawasankha: Simoni (amene anapatsidwa dzina lakuti Petro); 17Yakobo mwana wa Zebedayo, ndi mʼbale wake Yohane (iwowa anawapatsa dzina lakuti Bowanege, ndiye kuti ana a bingu); 18Andreya, Filipo, Bartumeyu, Mateyu, Tomasi, Yakobo mwana wa Alufeyo, Tadeyo, Simoni Zelote, 19ndi Yudasi Isikarioti, amene anamupereka Iye.

Yesu ndi Belezebabu

20Pambuyo pake Yesu analowa mʼnyumba, ndipo gulu la anthu linasonkhananso, kotero kuti Iye pamodzi ndi ophunzira ake sanapeze mpata kuti adye. 21Anthu a ku banja lake atamva zimenezi, anapita kuti akamutenga, pakuti ankanena kuti, “Wazungulira mutu.”

22Ndipo aphunzitsi amalamulo omwe anachokera ku Yerusalemu anati, “Iye wagwidwa ndi Belezebabu! Ndi ulamuliro wa mkulu wa ziwanda akutulutsa ziwanda.”

23Pamenepo Yesu anawayitana nawayankhula mʼmafanizo nati: “Kodi Satana angatulutse bwanji Satana? 24Ngati ufumu ugawanikana mwa iwo okha, ufumu umenewo sungakhalitse. 25Ngati nyumba igawanikana mwa iyo yokha, nyumba imeneyo singathe kuyima. 26Ndipo ngati Satana adzitsutsa yekha sangathe kuyima; ulamuliro wake watha. 27Kunena zoona, palibe munthu angalowe mʼnyumba ya munthu wamphamvu ndi kutenga katundu wake pokhapokha atayamba wamumanga munthu wamphamvuyo. Pamenepo akhoza kumubera. 28Ndikukuwuzani zoona kuti machimo onse ndi zamwano zonse za anthu zidzakhululukidwa, 29koma aliyense amene achitira mwano Mzimu Woyera sadzakhululukidwa pakuti wachita tchimo losatha.”

30Ananena izi chifukwa anati, “Ali ndi mzimu woyipa.”

Amayi ndi Abale ake a Yesu

31Pamenepo amayi ndi abale ake a Yesu anafika. Atayima kunja, anatuma wina kuti akamuyitane Iye. 32Gulu la anthu linakhala momuzungulira Iye, ndipo anamuwuza kuti, “Amayi ndi abale anu ali panja akukufunani.”

33Iye anafunsa kuti, “Amayi ndi abale anga ndi ndani?”

34Pamenepo anayangʼana anthu amene anakhala momuzungurira ndipo anati, “Awa ndi amayi anga ndi abale anga! 35Aliyense amene achita chifuniro cha Mulungu ndi mʼbale wanga ndi mlongo wanga ndi amayi anga.”