雅歌 8 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

雅歌 8:1-14

1如果你是我的同胞兄弟就好了。

这样,在外头遇见你,

我也可以亲吻你,

没有人会取笑我。

2我可以把你带进我母亲的家——她教养了我。

我要给你喝石榴汁酿的醇酒。

3你的左手扶着我的头,

右手紧抱着我。

4耶路撒冷的少女啊,

我恳求你们,

不要叫醒或惊动爱情,

等它自发吧。

耶路撒冷的少女:

5那从旷野上来、靠在良人身旁的是谁呢?

女子:

我在苹果树下唤醒你,

你母亲在那里怀你养你,

为你受生产之苦。

6请把我印在你的心上,

刻在你的手臂上,

因为爱情如死亡一般坚固,

嫉妒像阴间一样残酷,

它燃起的火焰是烧灭一切的烈火。

7爱情,大水不能熄灭,

江河不能淹没。

若有人想倾其家财买爱情,

必遭唾弃。

女子的兄长:

8我们有一个小妹,

她的胸脯还没有发育。

若有人来提亲,

我们该怎么办?

9她若是墙,

我们要在上面建造银塔;

她若是门,

我们要用香柏木板围护她。

女子:

10我是一面墙,

双乳像城楼,

我在他眼中像找到平安的人。

11所罗门巴力·哈们有一个葡萄园,

他把葡萄园租给农夫,

租金是每人一千块银子。

12我的葡萄园,我自己作主。

所罗门啊,你的一千块银子自己留着,

二百块银子给管果园的人。

男子:

13你这住在园中的人啊,

同伴们都在聆听你的声音,

求你让我也听见吧!

女子:

14我的良人啊,

愿你像香草山上的羚羊和小鹿,

快快来到我身边!

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 8:1-14

1Ukanakhala kuti ndiwe mlongo wanga,

amene anayamwa mawere a amayi anga!

Ndikanakumana nawe pa njira,

ndikanakupsompsona,

ndipo palibe wina aliyense akanandinyoza.

2Ndikanakutenga

ndi kukulowetsa mʼnyumba ya amayi anga,

amayi amene anandiphunzitsa,

ndikanakupatsa vinyo wotsekemera kuti umwe,

zotsekemera za makangadza.

3Mutu wanga watsamira dzanja lake lamanzere

ndipo dzanja lake lamanja landikumbatira.

4Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani:

musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa

mpaka pamene chifunire ichocho.

Abwenzi

5Kodi ndani uyo akutuluka ku chipululuyo,

atatsamira wokondedwa wakeyo?

Mkazi

Ndinakudzutsa pa tsinde pa mtengo wa apulosi,

pamenepo ndi pamene amayi anachirira,

pamenepo ndi pamene wokubereka anamva ululu pokubala iweyo.

6Undiyike pamtima pako ngati chidindo,

ngati chidindo cha pa dzanja lako;

pakuti chikondi nʼchamphamvu ngati imfa,

nsanje ndiyaliwuma ngati manda.

Chikondi chimachita kuti lawilawi

ngati malawi a moto wamphamvu.

7Madzi ochuluka sangachizimitse chikondi,

mitsinje singachikokolole chikondicho.

Ngati wina apereka chuma chonse

cha mʼnyumba mwake chifukwa cha chikondi,

adzangonyozeka nazo kotheratu.

Abwenzi

8Ife tili naye mlongo wathu wamngʼono,

koma alibe mawere,

kodi tidzamuchitira chiyani mlongo wathuyu

pa tsiku limene adzamufunsire?

9Ngati iye ndi khoma,

tidzamumangira nsanja ya siliva.

Ngati iye ndi chitseko,

tidzamutchinga ndi matabwa a mkungudza.

Mkazi

10Ine ndili ngati khoma,

ndipo mawere anga ndi nsanja zake.

Tsono mʼmaso mwa bwenzi langa

ndine wobweretsa mtendere.

11Solomoni anali ndi munda wampesa ku Baala-Hamoni;

iyeyo anabwereketsa munda wamphesawo kwa alimi,

aliyense mwa iwo ankayenera kupereka

ndalama zasiliva 1,000 mʼmalo mwa zipatso zake.

12Koma munda wanga wampesa ndi wangawanga ndiponso wa ine ndekha.

Iwe Solomoni, khala nazo ndalama zasiliva 1,000

ndipo ndalama zasiliva 200 ndi za amene akusamalira mundawo.

Mwamuna

13Iwe amene umakhala mʼminda

uli pamodzi ndi anzako,

ndilole kuti ndimve liwu lako!

Mkazi

14Fulumira wokondedwa wanga,

ndipo ukhale ngati gwape

kapena mwana wa mbawala

wothamanga mʼmapiri mʼmene mumamera mbewu zokometsera chakudya.