雅歌 3 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

雅歌 3:1-11

1我夜晚躺在床上,

思念着我心爱的人;

我寻找他,却找不到。

2我要起来寻遍城里的大街小巷,

我要寻找我心爱的人。

我寻找他,却寻不到。

3遇上了城中巡逻的守卫,

我就问他们:“你们看到我心爱的人了吗?”

4我刚离开他们,便找到了我心爱的人。

我拉着他,不让他走;

我把他带回娘家,

到怀我者的卧室。

5耶路撒冷的少女啊!

我指着羚羊和田野的母鹿吩咐你们,

不要叫醒或惊动爱情,

等它自发吧。

耶路撒冷的少女:

6那从旷野上来,形状像烟柱,

散发着商人贩卖的没药、乳香等各样芬芳之气的是什么呢?

7看啊,是所罗门的轿子,

周围是六十名勇士,

都是以色列的精兵。

8他们个个骁勇善战,手持利剑,

腰配战刀,防备夜间的偷袭。

9所罗门王用黎巴嫩木为自己制造了一顶轿子。

10银轿柱、金靠背、紫锦坐垫,

轿子里面的装饰都是耶路撒冷少女们用爱情编织的。

11锡安的少女啊,

出去看看所罗门王的风采吧!

他头上的王冠是他母亲在他成婚那天,

在他心中欢快之日为他戴上的。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 3:1-11

1Usiku wonse ndili pa bedi langa

ndinafunafuna amene mtima wanga umamukonda;

ndinamufunafuna koma osamupeza.

2Ndikudzuka tsopano ndipo ndidzayendayenda mu mzinda,

mʼmisewu yake ndi mʼmabwalo ake;

ndidzamufunafuna amene mtima wanga umamukonda.

Kotero ine ndinamufunafuna iyeyo koma osamupeza.

3Alonda anandipeza

pamene ankayendera mzinda.

“Kodi mwamuonako amene mtima wanga umamukonda?”

4Nditawapitirira pangʼono

ndinamupeza amene mtima wanga umamukonda.

Ndinamugwira ndipo sindinamulole kuti achoke

mpaka nditamulowetsa mʼnyumba ya amayi anga,

mʼchipinda cha amene anandibereka.

5Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani

pali gwape ndi mbawala yayikazi zakuthengo:

Musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa

mpaka pamene chifunire ichocho.

6Kodi ndani amene akubwera kuchokera ku chipululu

ngati utsi watolotolo,

wonunkhira mure ndi lubani,

zopangidwa kuchokera ku zonunkhira zonse za anthu amalonda?

7Ona! Chimenecho ndi chonyamulira Solomoni,

choperekezedwa ndi asilikali 60,

anthu amphamvu a ku Israeli,

8onse atanyamula lupanga,

onse odziwa bwino nkhondo,

aliyense ali ndi lupanga pambali pake,

kukonzekera zoopsa za usiku.

9Mfumu Solomoni anadzipangira chonyamulirachi;

anachipanga ndi matabwa ochokera ku Lebanoni.

10Milongoti yake anayipanga yasiliva,

kumbuyo kwake kwa golide.

Mipando yake inakutidwa ndi nsalu yapepo,

anakongoletsa mʼkati mwake ndi chikondi

cha akazi a ku Yerusalemu.

11Tukulani inu akazi a ku Ziyoni

ndipo mudzaone mfumu Solomoni atavala chipewa chaufumu,

chipewa chaufumu chimene amayi ake anamuveka

pa tsiku la ukwati wake,

tsiku limene mtima wake unasangalala.